Check out the new design

Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: Hud   Ajet:

Hûd

الٓرۚ كِتَٰبٌ أُحۡكِمَتۡ ءَايَٰتُهُۥ ثُمَّ فُصِّلَتۡ مِن لَّدُنۡ حَكِيمٍ خَبِيرٍ
Alif-Lam-Ra. Ili ndi buku lomwe ndime zake zakonzedwa bwino ndipo zafotokozedwa mwatsatanetsatane kuchokera kwa Allah Mwini nzeru zakuya Wodziwa chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَّا تَعۡبُدُوٓاْ إِلَّا ٱللَّهَۚ إِنَّنِي لَكُم مِّنۡهُ نَذِيرٞ وَبَشِيرٞ
(Wachita zimenezi) kuti musampembedze wina wake koma Allah yekha. Ndithudi ine kwa inu ndimchenjezi wochokera kwa Iye ndiponso wokuuzani nkhani zabwino.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَنِ ٱسۡتَغۡفِرُواْ رَبَّكُمۡ ثُمَّ تُوبُوٓاْ إِلَيۡهِ يُمَتِّعۡكُم مَّتَٰعًا حَسَنًا إِلَىٰٓ أَجَلٖ مُّسَمّٗى وَيُؤۡتِ كُلَّ ذِي فَضۡلٖ فَضۡلَهُۥۖ وَإِن تَوَلَّوۡاْ فَإِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٖ كَبِيرٍ
Ndikuti mupemphe chikhululuko kwa Mbuye wanu ndipo mulape kwa Iye. Akupatsani chisangalalo chabwino mpakana m’nthawi yoikidwa. Ndipo adzampatsa (tsiku lachimaliziro) aliyense wochita zabwino ubwino wake. Koma, ngati mupotoka ine kwanga nkukuoperani za chilango cha tsiku lalikulu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِلَى ٱللَّهِ مَرۡجِعُكُمۡۖ وَهُوَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٌ
Kobwerera kwanu nkwa Allah basi. Iye ali ndi mphamvu pa chilichonse.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَآ إِنَّهُمۡ يَثۡنُونَ صُدُورَهُمۡ لِيَسۡتَخۡفُواْ مِنۡهُۚ أَلَا حِينَ يَسۡتَغۡشُونَ ثِيَابَهُمۡ يَعۡلَمُ مَا يُسِرُّونَ وَمَا يُعۡلِنُونَۚ إِنَّهُۥ عَلِيمُۢ بِذَاتِ ٱلصُّدُورِ
Tamverani! Iwo akubisa zimene zili m’mitima yawo kuti amubise Iye (Allah). Mverani! Ndithudi pamene akuzifunda nsalu zawo Iye akudziwa zimene akuzibisa ndi zimene akuzionetsa. Ndithudi Iye ndiwodziwa za mzifuwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: Hud
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala - Sadržaj prijevodā

Halid Ibrahim Bejtala je preveo.

Zatvaranje