Check out the new design

Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: En-Nisa   Ajet:
۞ إِنَّآ أَوۡحَيۡنَآ إِلَيۡكَ كَمَآ أَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ نُوحٖ وَٱلنَّبِيِّـۧنَ مِنۢ بَعۡدِهِۦۚ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰٓ إِبۡرَٰهِيمَ وَإِسۡمَٰعِيلَ وَإِسۡحَٰقَ وَيَعۡقُوبَ وَٱلۡأَسۡبَاطِ وَعِيسَىٰ وَأَيُّوبَ وَيُونُسَ وَهَٰرُونَ وَسُلَيۡمَٰنَۚ وَءَاتَيۡنَا دَاوُۥدَ زَبُورٗا
Ndithudi, takuvumbulutsira (chivumbulutso) monga momwe tidamuvumbulutsira Nuh (Nowa) ndi aneneri amene anadza pambuyo pake. Ndipo tidamuvumbulutsiranso Ibrahim, Ismail, Ishâq, Ya’qub ndi mbumba yake. Ndipo (tidamuvumbulutsiranso) Isa (Yesu), Ayyub (Yobu), Yunus (Yona), Haarun (Aroni) ndi Sulaiman, ndipo Daud tidampatsa Zabur (Masalimo).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَرُسُلٗا قَدۡ قَصَصۡنَٰهُمۡ عَلَيۡكَ مِن قَبۡلُ وَرُسُلٗا لَّمۡ نَقۡصُصۡهُمۡ عَلَيۡكَۚ وَكَلَّمَ ٱللَّهُ مُوسَىٰ تَكۡلِيمٗا
Ndipo (tidavumbulutsanso chivumbulutso) kwa atumiki omwe takusimbira kale nkhani zawo komanso kwa atumiki ena omwe sitinakusimbire (nkhani zawo); ndipo Allah adayankhula ndi Mûsa mwachindunji.
Tefsiri na arapskom jeziku:
رُّسُلٗا مُّبَشِّرِينَ وَمُنذِرِينَ لِئَلَّا يَكُونَ لِلنَّاسِ عَلَى ٱللَّهِ حُجَّةُۢ بَعۡدَ ٱلرُّسُلِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَزِيزًا حَكِيمٗا
(Iwo ndi) atumiki omwe adauza nkhani zabwino (kwa anthu abwino) ndi kuwachenjeza (oipa) kuti anthu asadzakhale ndi mtsutso pa Allah pambuyo pa (kudza kwa) atumikiwa. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Tefsiri na arapskom jeziku:
لَّٰكِنِ ٱللَّهُ يَشۡهَدُ بِمَآ أَنزَلَ إِلَيۡكَۖ أَنزَلَهُۥ بِعِلۡمِهِۦۖ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ يَشۡهَدُونَۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ شَهِيدًا
Koma Allah akuikira umboni zimene wakuvumbulutsira kuti (nzoona), adavumbulutsa mwanzeru Zake. Nawonso angelo akuikira umboni. Ndipo Allah akukwana kukhala mboni.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ قَدۡ ضَلُّواْ ضَلَٰلَۢا بَعِيدًا
Ndithu amene sadakhulupirire, nawatsekereza (anthu) kuyenda pa njira ya Allah, ndithudi asokera; kusokera kwakukulu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَظَلَمُواْ لَمۡ يَكُنِ ٱللَّهُ لِيَغۡفِرَ لَهُمۡ وَلَا لِيَهۡدِيَهُمۡ طَرِيقًا
Ndithudi, amene sadakhulupirire, namachita zoipa, sali Allah owakhululukira iwowo ndi kuwaongolera njira.
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِلَّا طَرِيقَ جَهَنَّمَ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٗا
Kupatula njira yomka ku Jahannam, mmenemo akakhala muyaya. Ndipo zimenezo nzopepuka kwa Allah.
Tefsiri na arapskom jeziku:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ قَدۡ جَآءَكُمُ ٱلرَّسُولُ بِٱلۡحَقِّ مِن رَّبِّكُمۡ فَـَٔامِنُواْ خَيۡرٗا لَّكُمۡۚ وَإِن تَكۡفُرُواْ فَإِنَّ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
E inu anthu! Ndithu Mtumiki wakudzerani ndi choonadi chochokera kwa Mbuye wanu. Choncho khulupirirani; ndi bwino kwa inu kutero. Koma ngati mukana, (dziwani kuti) zonse zakumwamba ndi zapansi nza Allah. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri Ngwanzeru zakuya.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: En-Nisa
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala - Sadržaj prijevodā

Halid Ibrahim Bejtala je preveo.

Zatvaranje