Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Ajet: (153) Sura: Sura en-Nisa
يَسۡـَٔلُكَ أَهۡلُ ٱلۡكِتَٰبِ أَن تُنَزِّلَ عَلَيۡهِمۡ كِتَٰبٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِۚ فَقَدۡ سَأَلُواْ مُوسَىٰٓ أَكۡبَرَ مِن ذَٰلِكَ فَقَالُوٓاْ أَرِنَا ٱللَّهَ جَهۡرَةٗ فَأَخَذَتۡهُمُ ٱلصَّٰعِقَةُ بِظُلۡمِهِمۡۚ ثُمَّ ٱتَّخَذُواْ ٱلۡعِجۡلَ مِنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ فَعَفَوۡنَا عَن ذَٰلِكَۚ وَءَاتَيۡنَا مُوسَىٰ سُلۡطَٰنٗا مُّبِينٗا
Anthu amene adapatsidwa buku (Ayuda) akukupempha (iwe Mtumiki) kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi, adampemphanso Mûsa zazikulu kuposa zimenezi pomwe adati: “Tiwonetse Allah poyera.” Choncho udawagwira moto wamphenzi chifukwa cha kuipitsa kwao (motowo udachotsa miyoyo yawo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Zitatero Allah adawapatsa moyo kachiwiri). Kenako iwo adapanga thole (mwana wang’ombe monga mulungu wawo) pambuyo powafikira chisonyezo choonekera. Koma tidawakhululukira zimenezo, ndipo tidampatsa Mûsa chisonyezo choonekera poyera.[153]
[153] Ayuda adauza mtumiki Muhammad (s.a.w) kuti sangakhulupirire pokhapokha amuone akukwera kumwamba popanda kugwilira chilichonse ndi kubwera pansi pano buku lili m’manja mwake mutalembedwa umboni wa Allah woti iye Muhammad ndi Mtumiki Wakedi. Ndipo Allah akuti makhalidwe otsutsana ndi aneneri siachilendo kwa Ayuda. Ndipo Musa atalephera kuchita zimenezo adamuda. Tero adapanga fano (lamwana wang’ombe ‘thole’) naliyesa mulungu wawo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Ajet: (153) Sura: Sura en-Nisa
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje