Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Ajet: (1) Sura: Sura el-Feth

Sura el-Feth

إِنَّا فَتَحۡنَا لَكَ فَتۡحٗا مُّبِينٗا
Ndithu takugonjetsera (iwe Mtumiki{s.a.w}mzinda wa Makka) kugonjetsa kwakukulu koonekera poyera.[346]
[346] M’chaka cha chisanu ndi chimodzi chisamukire Mtumiki (s.a.w), Mtumiki (s.a.w) adapita ku Makka kuchokera ku Madina pamodzi ndi omtsatira ake kuti akachite Umrah imene ndi Hajj yaing’ono. Koma atayandikira ku Makka, Aquraish adamuletsa kulowa mu mzindamo kuti asachite mapemphero a Umrah. Ndipo atakambiranakambirana adamvana mfundo zingapo, zina mwa izo ndi:-
(i) Asamenyane nthawi imeneyo.
(ii) Abwelere ndipo adzabwere chaka chotsatiracho mwezi wonga umenewo kudzachita mapemphero. Panthawiyo sadzawaletsa kulowa mu mzindawo.
(iii) Asiye kumenyana pakati pawo kwa zaka khumi, ndi kumayenderana m’mene angafunire; Aquraish azipita ku Madina ngati atafuna, popanda kuzunzidwa.
(iv) Mafuko ena a Arabu adaloledwa kulowa nawo m’pangano limeneli kuti asamthire nkhondo Mtumiki (s.a.w), ndipo iyenso asawathire nkhondo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Ajet: (1) Sura: Sura el-Feth
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje