Check out the new design

Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: El-A'araf   Ajet:
وَجَٰوَزۡنَا بِبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ ٱلۡبَحۡرَ فَأَتَوۡاْ عَلَىٰ قَوۡمٖ يَعۡكُفُونَ عَلَىٰٓ أَصۡنَامٖ لَّهُمۡۚ قَالُواْ يَٰمُوسَى ٱجۡعَل لَّنَآ إِلَٰهٗا كَمَا لَهُمۡ ءَالِهَةٞۚ قَالَ إِنَّكُمۡ قَوۡمٞ تَجۡهَلُونَ
Ndipo tidawaolotsa ana a Israyeli pa nyanja (ndi kupulumuka ku masautso a Farawo), nadza kwa anthu omwe adali kupembedza mafano awo. (Iwo) adati: “E iwe Mûsa! Nafenso tipangire mulungu (wamafano) monga milungu yomwe ali nayo iwo.” (Mneneri Mûsa) adati: “Ndithudi, inu ndinu anthu osazindikira.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ مُتَبَّرٞ مَّا هُمۡ فِيهِ وَبَٰطِلٞ مَّا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
“Ndithudi awa aonongedwa m’zomwe ali nazozi, ndiponso ndizachabe zomwe akhala akuchita.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالَ أَغَيۡرَ ٱللَّهِ أَبۡغِيكُمۡ إِلَٰهٗا وَهُوَ فَضَّلَكُمۡ عَلَى ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Kodi ndikufunireni mulungu wina kusiya Allah chikhalirecho Iye wakuchitirani zabwino zoposa pa zolengedwa zonse?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِذۡ أَنجَيۡنَٰكُم مِّنۡ ءَالِ فِرۡعَوۡنَ يَسُومُونَكُمۡ سُوٓءَ ٱلۡعَذَابِ يُقَتِّلُونَ أَبۡنَآءَكُمۡ وَيَسۡتَحۡيُونَ نِسَآءَكُمۡۚ وَفِي ذَٰلِكُم بَلَآءٞ مِّن رَّبِّكُمۡ عَظِيمٞ
Ndipo kumbukirani pamene tidakupulumutsani (m’manja) mwa anthu a Farawo omwe adali kukuzunzani ndi chilango choyipa ndipo anali kupha ana anu aamuna ndi kusiya ana anu aakazi. Pa ichi padali mayeso aakulu ochokera kwa Mbuye wanu.
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ وَوَٰعَدۡنَا مُوسَىٰ ثَلَٰثِينَ لَيۡلَةٗ وَأَتۡمَمۡنَٰهَا بِعَشۡرٖ فَتَمَّ مِيقَٰتُ رَبِّهِۦٓ أَرۡبَعِينَ لَيۡلَةٗۚ وَقَالَ مُوسَىٰ لِأَخِيهِ هَٰرُونَ ٱخۡلُفۡنِي فِي قَوۡمِي وَأَصۡلِحۡ وَلَا تَتَّبِعۡ سَبِيلَ ٱلۡمُفۡسِدِينَ
Ndipo tidamlonjeza Mûsa masiku makumi atatu (kuti achite mapemphero kuti kenako timpatse Taurat). Ndipo tidawakwaniritsa ndi masiku khumi; chomwecho lidakwanira pangano la Mbuye wake (lopita kukampatsa Tauratiyo) m’masiku makumi anayi. Ndipo Mûsa adati kwa m’bale wake Harun: “Lowa m’malo mwanga pa (kuwatsogolera) anthu angawa. Ndipo konza; usatsate njira ya oononga.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَمَّا جَآءَ مُوسَىٰ لِمِيقَٰتِنَا وَكَلَّمَهُۥ رَبُّهُۥ قَالَ رَبِّ أَرِنِيٓ أَنظُرۡ إِلَيۡكَۚ قَالَ لَن تَرَىٰنِي وَلَٰكِنِ ٱنظُرۡ إِلَى ٱلۡجَبَلِ فَإِنِ ٱسۡتَقَرَّ مَكَانَهُۥ فَسَوۡفَ تَرَىٰنِيۚ فَلَمَّا تَجَلَّىٰ رَبُّهُۥ لِلۡجَبَلِ جَعَلَهُۥ دَكّٗا وَخَرَّ مُوسَىٰ صَعِقٗاۚ فَلَمَّآ أَفَاقَ قَالَ سُبۡحَٰنَكَ تُبۡتُ إِلَيۡكَ وَأَنَا۠ أَوَّلُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Pamene Mûsa adafika kumalo achipangano Chathucho, ndipo Mbuye wake namulankhula, (Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Dzionetseni kwa ine kuti ndikuoneni.” Allah adati: “Sungathe kundiona; koma yang’ana phirilo (lomwe lili patsogolo pako). Ngati likhazikika pamalo pake (popanda kusweka), ukhoza kundiona.” Choncho Mbuye wake pamene adadzionetsa kwa phirilo, adalichita kukhala loswekasweka ndipo Mussa adagwa ndi kukomoka. Pamene adatsitsimuka adati: “(Ha! Ndikutsimikizadi kuti) Inu ndinu Wolemekezeka. Ndalapa kwa Inu, ndipo ndine woyamba mwa okhulupirira (izi).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: El-A'araf
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala - Sadržaj prijevodā

Halid Ibrahim Bejtala je preveo.

Zatvaranje