Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Vers: (256) Surah / Kapitel: Al-Baqarah
لَآ إِكۡرَاهَ فِي ٱلدِّينِۖ قَد تَّبَيَّنَ ٱلرُّشۡدُ مِنَ ٱلۡغَيِّۚ فَمَن يَكۡفُرۡ بِٱلطَّٰغُوتِ وَيُؤۡمِنۢ بِٱللَّهِ فَقَدِ ٱسۡتَمۡسَكَ بِٱلۡعُرۡوَةِ ٱلۡوُثۡقَىٰ لَا ٱنفِصَامَ لَهَاۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٌ
Palibe kukakamiza (munthu kulowa) m’chipembedzo; kulungama kwaonekera poyera kusiyana ndi kusalungama. Choncho amene akumkana satana nakhulupirira Allah, ndiye kuti wagwira chigwiliro cholimba, chomwe sichisweka. Ndipo Allah Ngwakumva; Ngodziwa.[49]
[49] Arabu ena a mu Mzinda wa Madina, Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) asanasamukireko adali kutsata chipembedzo cha Chiyuda. Koma ambiri a iwo adali kupembedza mafano. Pamene chidadza Chisilamu pafupifupi onse omwe ankapembedza mafano adalowa m’ Chisilamu. Koma amene adali m’chipembedzo cha Chiyuda ndiochepa okha omwe adalowa m’Chisilamu. Ndipo ena ngakhale anali Arabu adatsalirabe m’chipembedzo cha Chiyuda. Choncho, omwe adali asilamu adafuna kukakamiza mwamphamvu amene adali m’chipembedzo cha Chiyuda kuti alowe m’Chisilamu. Koma Allah adawaletsa kuti palibe kumkakamiza kuti alowe m’Chisilamu yemwe sakufuna. Munthu aliyense adapatsidwa nzeru yomzindikiritsa chabwino ndi choipa. Ngati afuna kusokera nkufuna kwake iye mwini. Ndipo Allah adzamulanga pa tsiku lachimaliziro osati pano padziko lapansi.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Vers: (256) Surah / Kapitel: Al-Baqarah
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen