Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Versículo: (256) Surah: Suratu Al-Baqarah
لَآ إِكۡرَاهَ فِي ٱلدِّينِۖ قَد تَّبَيَّنَ ٱلرُّشۡدُ مِنَ ٱلۡغَيِّۚ فَمَن يَكۡفُرۡ بِٱلطَّٰغُوتِ وَيُؤۡمِنۢ بِٱللَّهِ فَقَدِ ٱسۡتَمۡسَكَ بِٱلۡعُرۡوَةِ ٱلۡوُثۡقَىٰ لَا ٱنفِصَامَ لَهَاۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٌ
Palibe kukakamiza (munthu kulowa) m’chipembedzo; kulungama kwaonekera poyera kusiyana ndi kusalungama. Choncho amene akumkana satana nakhulupirira Allah, ndiye kuti wagwira chigwiliro cholimba, chomwe sichisweka. Ndipo Allah Ngwakumva; Ngodziwa.[49]
[49] Arabu ena a mu Mzinda wa Madina, Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye) asanasamukireko adali kutsata chipembedzo cha Chiyuda. Koma ambiri a iwo adali kupembedza mafano. Pamene chidadza Chisilamu pafupifupi onse omwe ankapembedza mafano adalowa m’ Chisilamu. Koma amene adali m’chipembedzo cha Chiyuda ndiochepa okha omwe adalowa m’Chisilamu. Ndipo ena ngakhale anali Arabu adatsalirabe m’chipembedzo cha Chiyuda. Choncho, omwe adali asilamu adafuna kukakamiza mwamphamvu amene adali m’chipembedzo cha Chiyuda kuti alowe m’Chisilamu. Koma Allah adawaletsa kuti palibe kumkakamiza kuti alowe m’Chisilamu yemwe sakufuna. Munthu aliyense adapatsidwa nzeru yomzindikiritsa chabwino ndi choipa. Ngati afuna kusokera nkufuna kwake iye mwini. Ndipo Allah adzamulanga pa tsiku lachimaliziro osati pano padziko lapansi.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Versículo: (256) Surah: Suratu Al-Baqarah
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar