Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Ayah: (15) Surah: An-Nahl
وَأَلۡقَىٰ فِي ٱلۡأَرۡضِ رَوَٰسِيَ أَن تَمِيدَ بِكُمۡ وَأَنۡهَٰرٗا وَسُبُلٗا لَّعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Ndipo adaika panthaka mapiri ataliatali kuti (nthaka) isagwedezeke nanu; ndipo (adaika) mitsinje ndi misewu kuti muongoke (potsata njira yeniyeni ndikukafika komwe mukufuna).[249]
[249] Allah adakhazikitsa mapiri ataliatali, olimba kuti nthaka isamagwedezeke pafupipafupi. Abu Suud adati: “Ndithudi nthaka idalengedwa ngati mpira ndikukhala yogwedezeka pazifukwa zochepa asanailengere mapiri monga momwe zimagwedezekera nyenyezi zinzake. koma pamene adailengera mapiri idakhazikika. Zoterezi ndi pachifukwa chakuti anthu akhazikike bwino.
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Ayah: (15) Surah: An-Nahl
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close