《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (15) 章: 奈哈里
وَأَلۡقَىٰ فِي ٱلۡأَرۡضِ رَوَٰسِيَ أَن تَمِيدَ بِكُمۡ وَأَنۡهَٰرٗا وَسُبُلٗا لَّعَلَّكُمۡ تَهۡتَدُونَ
Ndipo adaika panthaka mapiri ataliatali kuti (nthaka) isagwedezeke nanu; ndipo (adaika) mitsinje ndi misewu kuti muongoke (potsata njira yeniyeni ndikukafika komwe mukufuna).[249]
[249] Allah adakhazikitsa mapiri ataliatali, olimba kuti nthaka isamagwedezeke pafupipafupi. Abu Suud adati: “Ndithudi nthaka idalengedwa ngati mpira ndikukhala yogwedezeka pazifukwa zochepa asanailengere mapiri monga momwe zimagwedezekera nyenyezi zinzake. koma pamene adailengera mapiri idakhazikika. Zoterezi ndi pachifukwa chakuti anthu akhazikike bwino.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (15) 章: 奈哈里
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭