Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Ayah: (158) Surah: Al-Baqarah
۞ إِنَّ ٱلصَّفَا وَٱلۡمَرۡوَةَ مِن شَعَآئِرِ ٱللَّهِۖ فَمَنۡ حَجَّ ٱلۡبَيۡتَ أَوِ ٱعۡتَمَرَ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِ أَن يَطَّوَّفَ بِهِمَاۚ وَمَن تَطَوَّعَ خَيۡرٗا فَإِنَّ ٱللَّهَ شَاكِرٌ عَلِيمٌ
Ndithudi, Safaa ndi Marwa ndizizindikiro zolemekezera chipembedzo cha Allah. Choncho, amene akukachita mapemphero a Hajj ku nyumbayo, kapena kuchita Umrah, sikulakwa kwa iye kuzungulira pamenepo (pakati pamapiri amenewo). Ndipo amene achite chabwino modzipereka (adzalipidwa). Ndithudi Allah Ngothokoza; Ngodziwa.[8]
[8] Hajj ndi Umrah ndimapemphero amene sangachitike pamalo pena paliponse kupatula mu mzinda wa Makka. Kachitidwe ka mapemphero awiriwa nkofanana. Koma pamakhala kusiyana pang’ono pakati pa Hajj ndi Umrah. Kusiyana kwake kuli motere: Hajj siichitika nthawi iliyonse koma m’miyezi yake yodziwika. Ndipo kutha kwamiyezi ya Hajj ndi masiku khumi am’khumi loyamba a m’mwezi wa Thul Hijjah. Pomwe Umrah ikhoza kuchitika m’mwezi uliwonse umene munthu wafuna.
Pamapiripo Chisilamu chisanadze adaikapo mafano omwe anthu achikunja panthawiyo adali kuwapembedza. Tero pamene Chisilamu chidadza Asilamu ena sadali kuona bwino kukachitira mapemphero pa mapiriwo poganizira za mafano amene adalipo kalelo. Koma adawauza kuti palibe kuipa kulikonse kuchitirapo mapemphero pa malopo chifukwa mafanowo adawachotsapo.
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Ayah: (158) Surah: Al-Baqarah
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close