Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Versículo: (158) Capítulo: Sura Al-Baqara
۞ إِنَّ ٱلصَّفَا وَٱلۡمَرۡوَةَ مِن شَعَآئِرِ ٱللَّهِۖ فَمَنۡ حَجَّ ٱلۡبَيۡتَ أَوِ ٱعۡتَمَرَ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِ أَن يَطَّوَّفَ بِهِمَاۚ وَمَن تَطَوَّعَ خَيۡرٗا فَإِنَّ ٱللَّهَ شَاكِرٌ عَلِيمٌ
Ndithudi, Safaa ndi Marwa ndizizindikiro zolemekezera chipembedzo cha Allah. Choncho, amene akukachita mapemphero a Hajj ku nyumbayo, kapena kuchita Umrah, sikulakwa kwa iye kuzungulira pamenepo (pakati pamapiri amenewo). Ndipo amene achite chabwino modzipereka (adzalipidwa). Ndithudi Allah Ngothokoza; Ngodziwa.[8]
[8] Hajj ndi Umrah ndimapemphero amene sangachitike pamalo pena paliponse kupatula mu mzinda wa Makka. Kachitidwe ka mapemphero awiriwa nkofanana. Koma pamakhala kusiyana pang’ono pakati pa Hajj ndi Umrah. Kusiyana kwake kuli motere: Hajj siichitika nthawi iliyonse koma m’miyezi yake yodziwika. Ndipo kutha kwamiyezi ya Hajj ndi masiku khumi am’khumi loyamba a m’mwezi wa Thul Hijjah. Pomwe Umrah ikhoza kuchitika m’mwezi uliwonse umene munthu wafuna.
Pamapiripo Chisilamu chisanadze adaikapo mafano omwe anthu achikunja panthawiyo adali kuwapembedza. Tero pamene Chisilamu chidadza Asilamu ena sadali kuona bwino kukachitira mapemphero pa mapiriwo poganizira za mafano amene adalipo kalelo. Koma adawauza kuti palibe kuipa kulikonse kuchitirapo mapemphero pa malopo chifukwa mafanowo adawachotsapo.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Versículo: (158) Capítulo: Sura Al-Baqara
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar