Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Ayah: (33) Surah: Saba’
وَقَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُواْ لِلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ بَلۡ مَكۡرُ ٱلَّيۡلِ وَٱلنَّهَارِ إِذۡ تَأۡمُرُونَنَآ أَن نَّكۡفُرَ بِٱللَّهِ وَنَجۡعَلَ لَهُۥٓ أَندَادٗاۚ وَأَسَرُّواْ ٱلنَّدَامَةَ لَمَّا رَأَوُاْ ٱلۡعَذَابَۚ وَجَعَلۡنَا ٱلۡأَغۡلَٰلَ فِيٓ أَعۡنَاقِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۖ هَلۡ يُجۡزَوۡنَ إِلَّا مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo amene adaponderezedwa adzanena kwa amene adadzikweza: “Iyayi, koma (mumachita) ndale za usiku ndi usana (zotitsekereza nazo ku chikhulupiliro) pamene mumatilamula kuti tinkanire Allah ndikumpangira Iye milungu inzake.” Iwo adzabisa madandaulo pamene adzaona chilango. Ndipo tidzaika magoli m’makosi mwa amene sadakhulupirire; kodi angalipidwe china, osati zija ankachita?[337]
[337] M’ndime iyi, Allah akutifotokozera kuti pa tsiku la chimaliziro padzakhala kukangana pakati pa atsogeleri ndi anthu otsogoleredwa. Izi zidzachitika pamene otsogoleredwa adzatsimikiza kuti atsogoleri awo amawasokeza; ankangowalangiza zachabe. Potero adzakhala ndi madandaulo aakulu chifukwa chotsatira anthu osokera. Komatu madandaulo oterewa sadzawapindulira chilichonse popeza mwayi udzakhala utatha kale. Choncho nkofunika kuti potsata mtsogoleri aliyense tiyambe taganizira komwe akunka nafe; tisangokokedwa ngati nyama pakuti Allah adatipatsa dalitso lanzeru. Choncho tigwiritse ntchito bwino nzeru tsoka lisanatigwere.
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Ayah: (33) Surah: Saba’
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close