Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation * - Translations’ Index


Translation of the meanings Ayah: (4) Surah: Al-Balad
لَقَدۡ خَلَقۡنَا ٱلۡإِنسَٰنَ فِي كَبَدٍ
Ndithudi tamulenga munthu mmavuto (kuyambira chiyambi chake mpaka malekezero a moyo wake).[439]
[439] Munthu ali ndi mavuto ambiri amene nyama zina zilibe: chakudya amachipeza movutikira, ndipo kudya kwa iye nkofunikira pa moyo wake, chovala amachipeza movutikira pomwe iye ndiwoyenera kuvala. Sangathe kupilira ndi kutentha kapena kuzizira. Sangathenso kudziteteza popanda chida. Ndipo pamwamba pa izi, Allah wamukakamiza zinthu zambiri ndi kumuletsanso zinthu zambiri. Ndipo chilichonse chimene iye achita chikulembedwa. Pa tsiku lachimaliziro adzawerengedwa chilichonse chimene adachichita; chachikulu kapena chaching’ono.
Arabic explanations of the Qur’an:
 
Translation of the meanings Ayah: (4) Surah: Al-Balad
Surahs’ Index Page Number
 
Translation of the Meanings of the Noble Qur'an - Chewa translation - Translations’ Index

Translation of the Quran meanings into Chewa by Khaled Ibrahim Betala (ed. 2020)

close