Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Saad   Versículo:

Sura Saad

صٓۚ وَٱلۡقُرۡءَانِ ذِي ٱلذِّكۡرِ
Sad, ndikulumbira Qur’an (iyi) ya ulaliki (wothandiza).
Las Exégesis Árabes:
بَلِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ فِي عِزَّةٖ وَشِقَاقٖ
Koma amene sadakhulupirire ali mkudzitukumula ndi makani.
Las Exégesis Árabes:
كَمۡ أَهۡلَكۡنَا مِن قَبۡلِهِم مِّن قَرۡنٖ فَنَادَواْ وَّلَاتَ حِينَ مَنَاصٖ
Kodi ndimibadwo ingati taiwononga patsogolo pawo? Adakuwa kuitana (panthawi imeneyo), koma nthawi yopulumuka idali itatha.
Las Exégesis Árabes:
وَعَجِبُوٓاْ أَن جَآءَهُم مُّنذِرٞ مِّنۡهُمۡۖ وَقَالَ ٱلۡكَٰفِرُونَ هَٰذَا سَٰحِرٞ كَذَّابٌ
Ndipo anadabwa atawadzera mchenjezi wochokera mwa iwo. Ndipo osakhulupirira adati: “Uyu ndiwamatsenga; ngwabodza lamkunkhuniza!”
Las Exégesis Árabes:
أَجَعَلَ ٱلۡأٓلِهَةَ إِلَٰهٗا وَٰحِدًاۖ إِنَّ هَٰذَا لَشَيۡءٌ عُجَابٞ
Ha! Waichita milungu yambirimbiri ija kuti ikhale Mulungu Mmodzi Yekha? Ndithu ichi nchinthu chodabwitsa.”
Las Exégesis Árabes:
وَٱنطَلَقَ ٱلۡمَلَأُ مِنۡهُمۡ أَنِ ٱمۡشُواْ وَٱصۡبِرُواْ عَلَىٰٓ ءَالِهَتِكُمۡۖ إِنَّ هَٰذَا لَشَيۡءٞ يُرَادُ
Ndipo adanyamuka akuluakulu a mwa iwo nati: “Nyamukani muzikapitiriza kupembedza milungu yanu. Ndithu chinthu ichi (nchoipa); chikulinga ife (kuti tisiyane ndi milungu yathu).”
Las Exégesis Árabes:
مَا سَمِعۡنَا بِهَٰذَا فِي ٱلۡمِلَّةِ ٱلۡأٓخِرَةِ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا ٱخۡتِلَٰقٌ
“Sitidamve zimenezi (zakuti Mulungu Ndimmodzi ngakhale) m’chipembedzo chakale (Chikhrisitu). Ichi sikanthu, koma ndibodza lopeka.”
Las Exégesis Árabes:
أَءُنزِلَ عَلَيۡهِ ٱلذِّكۡرُ مِنۢ بَيۡنِنَاۚ بَلۡ هُمۡ فِي شَكّٖ مِّن ذِكۡرِيۚ بَل لَّمَّا يَذُوقُواْ عَذَابِ
“Kodi uthengawo (wakuti Mulungu Ndimmodzi) wavumbulutsidwa kwa iye pakati pathu?” Koma iwo akukaika ndi ulaliki Wanga. Koma sadalawebe chilango Changa.
Las Exégesis Árabes:
أَمۡ عِندَهُمۡ خَزَآئِنُ رَحۡمَةِ رَبِّكَ ٱلۡعَزِيزِ ٱلۡوَهَّابِ
Kodi iwo ali nazo nkhokwe za chifundo cha Mbuye wako, Wamphamvu zoposa, Wopatsa mochuluka?
Las Exégesis Árabes:
أَمۡ لَهُم مُّلۡكُ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَاۖ فَلۡيَرۡتَقُواْ فِي ٱلۡأَسۡبَٰبِ
Kapena ufumu wa kumwamba ndi pansi ndi zapakati pake, ngwawo. Ngati zili choncho atakwera makwelero (kuti akafike pamalo poti akalamulire zimene akufuna, ngati angathe kutero).
Las Exégesis Árabes:
جُندٞ مَّا هُنَالِكَ مَهۡزُومٞ مِّنَ ٱلۡأَحۡزَابِ
Awa (Aquraish kuonjezera pa kudzitama kwawo), nkagulu kochepa ndi kofooka. Kagonjetsedwa monga makamu ankhondo (omwe adagonjetsedwa kale omwe amatsutsana ndi aneneri akale).
Las Exégesis Árabes:
كَذَّبَتۡ قَبۡلَهُمۡ قَوۡمُ نُوحٖ وَعَادٞ وَفِرۡعَوۡنُ ذُو ٱلۡأَوۡتَادِ
Patsogolo pawo, anthu a Nuh, Âdi ndi Farawo, mwini nyumba zitalizitali (Pyramid), adatsutsa (aneneri awo).
Las Exégesis Árabes:
وَثَمُودُ وَقَوۡمُ لُوطٖ وَأَصۡحَٰبُ لۡـَٔيۡكَةِۚ أُوْلَٰٓئِكَ ٱلۡأَحۡزَابُ
Ndi Asamudu, ndi anthu a Luti ndi (anthu a Shuaib) eni mitengo yambiri yothothana, amenewo ndiwo makamu.
Las Exégesis Árabes:
إِن كُلٌّ إِلَّا كَذَّبَ ٱلرُّسُلَ فَحَقَّ عِقَابِ
Onsewa adatsutsa atumiki; basi chilango Changa chidatsimikizika (pa iwo).
Las Exégesis Árabes:
وَمَا يَنظُرُ هَٰٓؤُلَآءِ إِلَّا صَيۡحَةٗ وَٰحِدَةٗ مَّا لَهَا مِن فَوَاقٖ
Ndipo awa (Aquraish), sayembekeza china koma mkuwe umodzi wosabwereza. (Ndipo ukadzachitika, onse adzafa).
Las Exégesis Árabes:
وَقَالُواْ رَبَّنَا عَجِّل لَّنَا قِطَّنَا قَبۡلَ يَوۡمِ ٱلۡحِسَابِ
Ndipo akunena (mwachipongwe): “E Mbuye wathu! Tipatsirenitu gawo la chilango chathu lisanafike tsiku lachiwerengero.”
Las Exégesis Árabes:
ٱصۡبِرۡ عَلَىٰ مَا يَقُولُونَ وَٱذۡكُرۡ عَبۡدَنَا دَاوُۥدَ ذَا ٱلۡأَيۡدِۖ إِنَّهُۥٓ أَوَّابٌ
Pirira (iwe Mtumiki) ku zimene akunena (kwa iwe), ndipo kumbuka kapolo wathu Daud, wamphamvu (pa chipembedzo ndi za m’dziko lapansi). Ndithu iye ngotembenukira kwa Allah kwambiri.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّا سَخَّرۡنَا ٱلۡجِبَالَ مَعَهُۥ يُسَبِّحۡنَ بِٱلۡعَشِيِّ وَٱلۡإِشۡرَاقِ
Ndithu Ife tidawagonjetsa mapiri kuti pamodzi ndi iye alemekeze (Allah) mmawa ndi madzulo.
Las Exégesis Árabes:
وَٱلطَّيۡرَ مَحۡشُورَةٗۖ كُلّٞ لَّهُۥٓ أَوَّابٞ
Ndi mbalame zomwe zidasonkhanitsidwa zonse zimamvera iye.
Las Exégesis Árabes:
وَشَدَدۡنَا مُلۡكَهُۥ وَءَاتَيۡنَٰهُ ٱلۡحِكۡمَةَ وَفَصۡلَ ٱلۡخِطَابِ
Ndipo tidaulimbikitsa ufumu wake ndi kumpatsa uneneri ndi kuyankhula kwa luntha (kosiyanitsira choona ndi chonama).
Las Exégesis Árabes:
۞ وَهَلۡ أَتَىٰكَ نَبَؤُاْ ٱلۡخَصۡمِ إِذۡ تَسَوَّرُواْ ٱلۡمِحۡرَابَ
Kodi yakufika nkhani ya okangana pamene adakwera chipupa mpaka kuchipinda (cha Daud chochitira mapemphero)?
Las Exégesis Árabes:
إِذۡ دَخَلُواْ عَلَىٰ دَاوُۥدَ فَفَزِعَ مِنۡهُمۡۖ قَالُواْ لَا تَخَفۡۖ خَصۡمَانِ بَغَىٰ بَعۡضُنَا عَلَىٰ بَعۡضٖ فَٱحۡكُم بَيۡنَنَا بِٱلۡحَقِّ وَلَا تُشۡطِطۡ وَٱهۡدِنَآ إِلَىٰ سَوَآءِ ٱلصِّرَٰطِ
Pamene adamulowera Daud, adachita nawo mantha adati: “Usaope; (ife) ndife okangana awiri, mmodzi wathu wamchenjelera wina. Weruza pakati pathu mwachilungamo, usakondere, ndipo tisonyeze njira yoongoka.”
Las Exégesis Árabes:
إِنَّ هَٰذَآ أَخِي لَهُۥ تِسۡعٞ وَتِسۡعُونَ نَعۡجَةٗ وَلِيَ نَعۡجَةٞ وَٰحِدَةٞ فَقَالَ أَكۡفِلۡنِيهَا وَعَزَّنِي فِي ٱلۡخِطَابِ
“Ndithu uyu m’bale wanga ali ndi nkhosa makumi asanu ndi anayi mphambu zisanu ndi zinayi (99), pomwe ine ndili ndi imodzi.” Ndipo akuti: “Ndipatse nkhosa imodziyo kuti ndizikusungira.” Ndipo wandiposa pakuyankhula.
Las Exégesis Árabes:
قَالَ لَقَدۡ ظَلَمَكَ بِسُؤَالِ نَعۡجَتِكَ إِلَىٰ نِعَاجِهِۦۖ وَإِنَّ كَثِيرٗا مِّنَ ٱلۡخُلَطَآءِ لَيَبۡغِي بَعۡضُهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٍ إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَقَلِيلٞ مَّا هُمۡۗ وَظَنَّ دَاوُۥدُ أَنَّمَا فَتَنَّٰهُ فَٱسۡتَغۡفَرَ رَبَّهُۥ وَخَرَّۤ رَاكِعٗاۤ وَأَنَابَ۩
(Daud) adati: “Zoona, wakuchitira zosalungama pokupempha nkhosa yako imodzi kuti aiphatikize ndi nkhosa zake. Ndithu ambiri mwa ophatikizana nawo zinthu, ena amachenjelera ena kupatula amene akhulupirira ndi kumachita zabwino; ndipo iwo ngochepa.” Basi pamenepo Daud adaona kuti tamuyesa mayeso (ndipo sadapambane). Choncho adapempha chikhululuko kwa Mbuye wake; adagwa ndi kulambira ndi kubwerera kwa Mbuye wake.
Las Exégesis Árabes:
فَغَفَرۡنَا لَهُۥ ذَٰلِكَۖ وَإِنَّ لَهُۥ عِندَنَا لَزُلۡفَىٰ وَحُسۡنَ مَـَٔابٖ
Choncho tidamkhululukira iye zimenezo; ndithu iye ali nawo ulemelero kwa Ife ndi mabwelero abwino.
Las Exégesis Árabes:
يَٰدَاوُۥدُ إِنَّا جَعَلۡنَٰكَ خَلِيفَةٗ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَٱحۡكُم بَيۡنَ ٱلنَّاسِ بِٱلۡحَقِّ وَلَا تَتَّبِعِ ٱلۡهَوَىٰ فَيُضِلَّكَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۚ إِنَّ ٱلَّذِينَ يَضِلُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ لَهُمۡ عَذَابٞ شَدِيدُۢ بِمَا نَسُواْ يَوۡمَ ٱلۡحِسَابِ
“E iwe Daud! Ndithu ife takuchita iwe kukhala woyang’anira pa dziko; choncho weruza pakati pa anthuwa mwachilungamo; ndipo usatsatire zilakolako kuopa kuti zingakusokeretse ku njira ya Allah.” Ndithu amene akusokera ku njira ya Allah (potsatira zilakolako zawo), chilango chaukali chili pa iwo chifukwa cha kuiwala kwawo tsiku la chiwerengero.
Las Exégesis Árabes:
وَمَا خَلَقۡنَا ٱلسَّمَآءَ وَٱلۡأَرۡضَ وَمَا بَيۡنَهُمَا بَٰطِلٗاۚ ذَٰلِكَ ظَنُّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۚ فَوَيۡلٞ لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنَ ٱلنَّارِ
Ndipo sitidalenge thambo ndi nthaka ndi zapakati pake popanda cholinga. Zoterezo ndi maganizo a amene sadakhulupirire. Choncho kuonongeka kwakukulu ku Moto kuli kwa iwo amene sadakhulupirire.
Las Exégesis Árabes:
أَمۡ نَجۡعَلُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ كَٱلۡمُفۡسِدِينَ فِي ٱلۡأَرۡضِ أَمۡ نَجۡعَلُ ٱلۡمُتَّقِينَ كَٱلۡفُجَّارِ
Kodi tingawachite amene akhulupirira (Allah) ndi kuchita zabwino kukhala monga oononga pa dziko? Kapena tiwachite oopa (Allah) monga oipa?
Las Exégesis Árabes:
كِتَٰبٌ أَنزَلۡنَٰهُ إِلَيۡكَ مُبَٰرَكٞ لِّيَدَّبَّرُوٓاْ ءَايَٰتِهِۦ وَلِيَتَذَكَّرَ أُوْلُواْ ٱلۡأَلۡبَٰبِ
(Ili), ndibuku lochuluka madalitso lomwe talivumbulutsa kwa iwe kuti (anthu) azame kwambiri pomvetsetsa ndime zake; ndi kuti apeze nalo phunziro eni nzeru.
Las Exégesis Árabes:
وَوَهَبۡنَا لِدَاوُۥدَ سُلَيۡمَٰنَۚ نِعۡمَ ٱلۡعَبۡدُ إِنَّهُۥٓ أَوَّابٌ
Ndipo Daud tidampatsa (dalitso lobereka) Sulaiman, amene adali munthu wabwino. Ndithu iye adali wochulukitsa kutembenukira kwa Allah (ndi kudzichepetsa m’chikhalidwe chake chonse).
Las Exégesis Árabes:
إِذۡ عُرِضَ عَلَيۡهِ بِٱلۡعَشِيِّ ٱلصَّٰفِنَٰتُ ٱلۡجِيَادُ
(Kumbuka) pamene adasonyezedwa kwa iye nthawi yamadzulo akavalo ofatsa akaima; othamanga kwambiri, akayenda.
Las Exégesis Árabes:
فَقَالَ إِنِّيٓ أَحۡبَبۡتُ حُبَّ ٱلۡخَيۡرِ عَن ذِكۡرِ رَبِّي حَتَّىٰ تَوَارَتۡ بِٱلۡحِجَابِ
Ndipo adati: “Ndikukonda zinthu zabwino chifukwa chokumbukira Mbuye wanga,” kufikira pomwe (akavalowo) adabisika kuseri kwa chotsekereza (poikidwa m’makola mwawo pomwe iye amafunitsitsa kumawaonabe).
Las Exégesis Árabes:
رُدُّوهَا عَلَيَّۖ فَطَفِقَ مَسۡحَۢا بِٱلسُّوقِ وَٱلۡأَعۡنَاقِ
(Ndipo adati): “Abwezeni kwa ine.” Kenako adayamba kuwasisita m’miyendo ndi m’makosi (mwawo).
Las Exégesis Árabes:
وَلَقَدۡ فَتَنَّا سُلَيۡمَٰنَ وَأَلۡقَيۡنَا عَلَىٰ كُرۡسِيِّهِۦ جَسَدٗا ثُمَّ أَنَابَ
Ndithu Sulaiman tidamuyesa (mayeso); ndipo tidaika thupi pa mpando wake wachifumu; kenako adabwerera kwa Allah.
Las Exégesis Árabes:
قَالَ رَبِّ ٱغۡفِرۡ لِي وَهَبۡ لِي مُلۡكٗا لَّا يَنۢبَغِي لِأَحَدٖ مِّنۢ بَعۡدِيٓۖ إِنَّكَ أَنتَ ٱلۡوَهَّابُ
Adati: “E Mbuye wanga! Ndikhululukireni ndipo ndipatseni ufumu (umene) sangaupeze aliyense pambuyo panga; ndithu inu ndiwopatsa mochulukitsa.”
Las Exégesis Árabes:
فَسَخَّرۡنَا لَهُ ٱلرِّيحَ تَجۡرِي بِأَمۡرِهِۦ رُخَآءً حَيۡثُ أَصَابَ
Kenako tidaichita mphepo yoomba moleza kuti imgonjere, yomwe imayenda mwachifuniro chake (Sulaiman), paliponse pomwe wafuna.
Las Exégesis Árabes:
وَٱلشَّيَٰطِينَ كُلَّ بَنَّآءٖ وَغَوَّاصٖ
Ndiponso (tidamgonjetsera) asatana; ena mwa iwo omanga zomangamanga ndi obira m’nyanja zakuya.
Las Exégesis Árabes:
وَءَاخَرِينَ مُقَرَّنِينَ فِي ٱلۡأَصۡفَادِ
Ndi ena (mwa asatana) onjatidwa mmagoli ndi unyolo, (kuti asiye kusokoneza ena).
Las Exégesis Árabes:
هَٰذَا عَطَآؤُنَا فَٱمۡنُنۡ أَوۡ أَمۡسِكۡ بِغَيۡرِ حِسَابٖ
(Ndipo adauzidwa iye): “Izi (zomwc takudalitsa nazo) ndi zopatsa Zathu; choncho mpatse kapena mmane (amene wamfuna). Popanda kuwerengeredwa.”
Las Exégesis Árabes:
وَإِنَّ لَهُۥ عِندَنَا لَزُلۡفَىٰ وَحُسۡنَ مَـَٔابٖ
Ndithu (Sulaiman) ali nawo ulemelero waukulu woyandikira kwa Ife, ndi mabwelero abwino.
Las Exégesis Árabes:
وَٱذۡكُرۡ عَبۡدَنَآ أَيُّوبَ إِذۡ نَادَىٰ رَبَّهُۥٓ أَنِّي مَسَّنِيَ ٱلشَّيۡطَٰنُ بِنُصۡبٖ وَعَذَابٍ
Kumbuka, (iwe Mtumiki {s.a.w}) kapolo Wathu Ayubu, pamene adaitana Mbuye wake: “Ine wandikhudza satana ndi masautso ndi zowawa!”
Las Exégesis Árabes:
ٱرۡكُضۡ بِرِجۡلِكَۖ هَٰذَا مُغۡتَسَلُۢ بَارِدٞ وَشَرَابٞ
(Tidamuyankha kuitana kwake, ndipo tidamuuza): “Menyetsa miyendo yako (panthaka; patuluka madzi) ozizira osamba ndi kumwa (zikuchokera zomwe uli nazo).”
Las Exégesis Árabes:
وَوَهَبۡنَا لَهُۥٓ أَهۡلَهُۥ وَمِثۡلَهُم مَّعَهُمۡ رَحۡمَةٗ مِّنَّا وَذِكۡرَىٰ لِأُوْلِي ٱلۡأَلۡبَٰبِ
Ndipo tidamubwezera anthu ake, ndi kumpatsanso ena onga iwo (m’kuchuluka kwawo) powaphatikiza ndi omwe adali nawo; (tidachita zimenezi) chifukwa cha chifundo chochokera kwa Ife ndi kuti chikhale chikumbutso kwa eni nzeru.
Las Exégesis Árabes:
وَخُذۡ بِيَدِكَ ضِغۡثٗا فَٱضۡرِب بِّهِۦ وَلَا تَحۡنَثۡۗ إِنَّا وَجَدۡنَٰهُ صَابِرٗاۚ نِّعۡمَ ٱلۡعَبۡدُ إِنَّهُۥٓ أَوَّابٞ
“Ndipo gwira m’dzanja lako mtolo wa zikoti; menya ndi mtolowo ndipo usaswe lonjezo.” Ndithu Ife tidampeza ali wopirira. Taonani kukhala bwino kapolo! Ndithu iye ngotembenukira kwambiri kwa Allah.[343]
[343] Ayubu adalumbira kuti adzamenya mkazi wake ndi zikoti zingapo pamene adamupsera mtima chifukwa cha kuchedwa kufika kwa iye pomwe adakasaka mkaziyo chakudya panthawi yomwe ayubu amadwala. Ndipo Allah adamasula kulumbira kwake kuti atenge mtolo wa zikoti zomwe m’kati mwake mudali chiwerengero chomwe adalumbilira kuti adzammenya nacho, ndipo ammenye ndi mtolowo kuti akwaniritse kulumbira kwakeko. Allah adamchitira Ayubu chifundo chimenechi chifukwa chakuti adapilira pa masautso ake, komanso adamchitira chifundo mkaziyo chifukwa anali mkazi wochita zabwino.
Las Exégesis Árabes:
وَٱذۡكُرۡ عِبَٰدَنَآ إِبۡرَٰهِيمَ وَإِسۡحَٰقَ وَيَعۡقُوبَ أُوْلِي ٱلۡأَيۡدِي وَٱلۡأَبۡصَٰرِ
Kumbukira, (iwe Mtumiki {s.a.w}) akapolo athu Ibrahim, Ishâq ndi Ya’qub, eni mphamvu (pa ntchito yachipembedzo) ndi kuyang’ana kozindikira.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّآ أَخۡلَصۡنَٰهُم بِخَالِصَةٖ ذِكۡرَى ٱلدَّارِ
Ndithu Ife tidawasankha powapatsa chikhalidwe chabwino (chomwe) ndi kukumbukira Nyumba yomaliza (nthawi zonse).
Las Exégesis Árabes:
وَإِنَّهُمۡ عِندَنَا لَمِنَ ٱلۡمُصۡطَفَيۡنَ ٱلۡأَخۡيَارِ
Ndithu kwa Ife iwo adali mwa anthu abwino omwe adasankhidwa.
Las Exégesis Árabes:
وَٱذۡكُرۡ إِسۡمَٰعِيلَ وَٱلۡيَسَعَ وَذَا ٱلۡكِفۡلِۖ وَكُلّٞ مِّنَ ٱلۡأَخۡيَارِ
Ndipo kumbuka Ismail, Alyasa’ (Eliya), ndi Thulkifl (Yesaya); ndipo onsewo adali mwa anthu abwino.
Las Exégesis Árabes:
هَٰذَا ذِكۡرٞۚ وَإِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ لَحُسۡنَ مَـَٔابٖ
Ichi ndichikumbutso (kwa iwe ndi anthu ako). Ndipo ndithu oopa Allah ali ndi mabwelero abwino.
Las Exégesis Árabes:
جَنَّٰتِ عَدۡنٖ مُّفَتَّحَةٗ لَّهُمُ ٱلۡأَبۡوَٰبُ
(Awakonzera iwo) minda yamuyaya yotsekulidwa makomo ake kwa iwo.
Las Exégesis Árabes:
مُتَّكِـِٔينَ فِيهَا يَدۡعُونَ فِيهَا بِفَٰكِهَةٖ كَثِيرَةٖ وَشَرَابٖ
(Azidzakhala m’menemo) uku atatsamira (makama amtengo wapatali, ndipo adzakhala akusangalala) akuitanitsa mmenemo zipatso ndi zakumwa zambiri.
Las Exégesis Árabes:
۞ وَعِندَهُمۡ قَٰصِرَٰتُ ٱلطَّرۡفِ أَتۡرَابٌ
Ndipo (ku Munda wamtenderewo) adzakhala ndi akazi oyang’ana amuna awo okha basi, ofanana misinkhu.
Las Exégesis Árabes:
هَٰذَا مَا تُوعَدُونَ لِيَوۡمِ ٱلۡحِسَابِ
Izi ndi zomwe mukulonjezedwa pa tsiku la chiweruziro.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّ هَٰذَا لَرِزۡقُنَا مَا لَهُۥ مِن نَّفَادٍ
Ndithu izi ndizopatsa Zathu zosatha.
Las Exégesis Árabes:
هَٰذَاۚ وَإِنَّ لِلطَّٰغِينَ لَشَرَّ مَـَٔابٖ
Awa ndimalipiro (a oopa Allah)! Koma opyola malire (ndi kunyoza aneneri awo), ali ndi mabwelero oipa.
Las Exégesis Árabes:
جَهَنَّمَ يَصۡلَوۡنَهَا فَبِئۡسَ ٱلۡمِهَادُ
(Omwe ndi) Jahannam adzailowa (ndi kupseleramo). Taonani kuipa kwa malo wokakhazikikamo!
Las Exégesis Árabes:
هَٰذَا فَلۡيَذُوقُوهُ حَمِيمٞ وَغَسَّاقٞ
Awa ndimadzi wotentha kwambiri, ndi mafinya (a anthu a ku Moto). Choncho awalaweko!
Las Exégesis Árabes:
وَءَاخَرُ مِن شَكۡلِهِۦٓ أَزۡوَٰجٌ
Ndi zilango zina zambiri zonga zimenezi zamitundumitundu.
Las Exégesis Árabes:
هَٰذَا فَوۡجٞ مُّقۡتَحِمٞ مَّعَكُمۡ لَا مَرۡحَبَۢا بِهِمۡۚ إِنَّهُمۡ صَالُواْ ٱلنَّارِ
(Kudzanenedwa kwa opyola malire, omwe ndiatsogoleri a opembedza mafano): “Gulu ili lalikulu, lilowa nanu ku Moto; (omwe adali okutsatirani. Ndipo atsogoleri adzati): Siolandiridwa (mwamtendere). Ndithu iwo ngolowa ku Moto.”
Las Exégesis Árabes:
قَالُواْ بَلۡ أَنتُمۡ لَا مَرۡحَبَۢا بِكُمۡۖ أَنتُمۡ قَدَّمۡتُمُوهُ لَنَاۖ فَبِئۡسَ ٱلۡقَرَارُ
(Otsatira adzanena): “Ndithu tembeleroli likuyenera inu, (limene mukutitembelera ife) chifukwa inu ndiamene mudadzetsa chilangochi potinyenga ife (ndi kutiitanira kunjira yopotoka), taonani kuipa malo okhazikikamo (Jahannam)!”
Las Exégesis Árabes:
قَالُواْ رَبَّنَا مَن قَدَّمَ لَنَا هَٰذَا فَزِدۡهُ عَذَابٗا ضِعۡفٗا فِي ٱلنَّارِ
(Otsatira) adzanena: “E Mbuye wathu! Muonjezereni chilango ku Moto pamwamba pa chilango amene watidzetsera chilangochi.”
Las Exégesis Árabes:
وَقَالُواْ مَا لَنَا لَا نَرَىٰ رِجَالٗا كُنَّا نَعُدُّهُم مِّنَ ٱلۡأَشۡرَارِ
Ndipo (anthu a ku Moto) adzanena: “Kodi nchifukwa ninji sitikuwaona anthu aja omwe timawawerengera kuti ngoipa (pa dziko lapansi)?
Las Exégesis Árabes:
أَتَّخَذۡنَٰهُمۡ سِخۡرِيًّا أَمۡ زَاغَتۡ عَنۡهُمُ ٱلۡأَبۡصَٰرُ
Kodi tidawachitira chipongwe (pa dziko lapansi koma taonani sadalowe nafe ku Moto). Kapena kuti maso athu sakuwaona?”
Las Exégesis Árabes:
إِنَّ ذَٰلِكَ لَحَقّٞ تَخَاصُمُ أَهۡلِ ٱلنَّارِ
Ndithu zimenezo, zokangana anthu a ku Moto nzoona.
Las Exégesis Árabes:
قُلۡ إِنَّمَآ أَنَا۠ مُنذِرٞۖ وَمَا مِنۡ إِلَٰهٍ إِلَّا ٱللَّهُ ٱلۡوَٰحِدُ ٱلۡقَهَّارُ
Nena (kwa iwo): “Ndithu ine ndine mchenjezi (wochenjeza za chilango cha Allah). Palibe wopembedzedwa mwachoonadi, koma Allah Mmodzi Yekha Wopambana.
Las Exégesis Árabes:
رَبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا ٱلۡعَزِيزُ ٱلۡغَفَّٰرُ
Mbuye wathambo ndi nthaka, ndi zapakati pake; wamphamvu zoposa; Wokhululuka machimo kwambiri (kwa yemwe walapa ndi kumkhulupirira).”
Las Exégesis Árabes:
قُلۡ هُوَ نَبَؤٌاْ عَظِيمٌ
Nena (kwa iwo iwe Mtumiki {s.a.w}): “Ichi (chimene ndakuchenjezani nachochi) ndinkhani yaikulu.”
Las Exégesis Árabes:
أَنتُمۡ عَنۡهُ مُعۡرِضُونَ
“Inu, za chimenechi, mukunyozera!”
Las Exégesis Árabes:
مَا كَانَ لِيَ مِنۡ عِلۡمِۭ بِٱلۡمَلَإِ ٱلۡأَعۡلَىٰٓ إِذۡ يَخۡتَصِمُونَ
“Sindimadziwa chilichonse za akuluakulu a pamwamba (angelo) pamene amakangana (za kulengedwa kwa Adam).”
Las Exégesis Árabes:
إِن يُوحَىٰٓ إِلَيَّ إِلَّآ أَنَّمَآ أَنَا۠ نَذِيرٞ مُّبِينٌ
Palibe china chimene chavumbulutsidwa kwa ine, koma (kuti ndikuuzeni mawu awa oti): “Ine ndine mchenjezi (wanu) woonekera.”
Las Exégesis Árabes:
إِذۡ قَالَ رَبُّكَ لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ إِنِّي خَٰلِقُۢ بَشَرٗا مِّن طِينٖ
(Akumbutse) pamene Mbuye wako adanena kwa angelo: “Ine ndilenga munthu kuchokera ku dothi, (yemwe ndi Adam).”
Las Exégesis Árabes:
فَإِذَا سَوَّيۡتُهُۥ وَنَفَخۡتُ فِيهِ مِن رُّوحِي فَقَعُواْ لَهُۥ سَٰجِدِينَ
“Ndikammaliza ndi kumuuzira mzimu wochokera kwa Ine, igwani pansi momulemekeza.”
Las Exégesis Árabes:
فَسَجَدَ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ كُلُّهُمۡ أَجۡمَعُونَ
Choncho angelo onse anagwa pansi momulemekeza.
Las Exégesis Árabes:
إِلَّآ إِبۡلِيسَ ٱسۡتَكۡبَرَ وَكَانَ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Kupatula Iblis; adadzikweza, ndipo adali mmodzi mwa okana.
Las Exégesis Árabes:
قَالَ يَٰٓإِبۡلِيسُ مَا مَنَعَكَ أَن تَسۡجُدَ لِمَا خَلَقۡتُ بِيَدَيَّۖ أَسۡتَكۡبَرۡتَ أَمۡ كُنتَ مِنَ ٱلۡعَالِينَ
(Allah) adati: “E iwe Iblis! Nchiyani chakuletsa kugwa pansi ndi kuchilemekeza chimene ndachilenga ndi manja Anga (popanda kutuma wina)? Kodi wadzikweza kapena uli mmodzi wa odziika pamwamba?”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ أَنَا۠ خَيۡرٞ مِّنۡهُ خَلَقۡتَنِي مِن نَّارٖ وَخَلَقۡتَهُۥ مِن طِينٖ
(Iblis) adanena: “Ine ndine wabwino kuposa iye (Adam); chifukwa ine mudandilenga kuchokera ku Moto, ndipo iye mudamulenga kuchokera kudongo.”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ فَٱخۡرُجۡ مِنۡهَا فَإِنَّكَ رَجِيمٞ
(Allah) adanena (kwa Iblis): “Tuluka m’menemo (m’gulu la angelo apamwamba); ndithu iwe ngopirikitsidwa (ku chifundo cha Allah).”
Las Exégesis Árabes:
وَإِنَّ عَلَيۡكَ لَعۡنَتِيٓ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلدِّينِ
“Ndipo ndithu matembelero Anga akhala pa iwe kufikira tsiku lamalipiro.”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ رَبِّ فَأَنظِرۡنِيٓ إِلَىٰ يَوۡمِ يُبۡعَثُونَ
(Iblis) adati: “E Mbuye wanga! Ndipatseni nthawi kufikira tsiku louka ku imfa.”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ فَإِنَّكَ مِنَ ٱلۡمُنظَرِينَ
(Allah) adati: “Ndithu iwe ndiwe mmodzi wa wopatsidwa nthawi.”
Las Exégesis Árabes:
إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡوَقۡتِ ٱلۡمَعۡلُومِ
“Kufikira tsiku la nthawi yodziwika (imene yaikidwa).”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ فَبِعِزَّتِكَ لَأُغۡوِيَنَّهُمۡ أَجۡمَعِينَ
(Iblis) adati: “Choncho kupyolera mu ulemelero Wanu ndikulumbira kuti ndiwasokoneza onse.”
Las Exégesis Árabes:
إِلَّا عِبَادَكَ مِنۡهُمُ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
“Kupatula akapolo Anu omwe ali osankhidwa (oyeretsedwa) mwa iwo. (Pa iwo ndilibe nyonga zilizonse).”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ فَٱلۡحَقُّ وَٱلۡحَقَّ أَقُولُ
(Allah) adati: “Ndikulumbira mwachoonadi ndipo ndikunena choona.”
Las Exégesis Árabes:
لَأَمۡلَأَنَّ جَهَنَّمَ مِنكَ وَمِمَّن تَبِعَكَ مِنۡهُمۡ أَجۡمَعِينَ
“Ndithudi, ndidzazadzitsa Jahannam ndi ochokera ku mtundu wako ndi omwe adzakutsate mwa iwo (ana a Adam) onse.”
Las Exégesis Árabes:
قُلۡ مَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٖ وَمَآ أَنَا۠ مِنَ ٱلۡمُتَكَلِّفِينَ
Nena (iwe Mtumiki{s.a.w}, kwa anthu ako): “Sindikukupemphani malipiro pa zimenezi ndiponso ine simmodzi wa odzikakamiza (pa zinthu zosandiyenera).
Las Exégesis Árabes:
إِنۡ هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
(Qur’an) sichina koma ndichikumbutso ndi chiphunzitso kwa zolengedwa zonse.
Las Exégesis Árabes:
وَلَتَعۡلَمُنَّ نَبَأَهُۥ بَعۡدَ حِينِۭ
Ndipo posachedwa mudziwa, (inu otsutsa, kuona kwa) nkhani zake.”
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Saad
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar