Check out the new design

Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Khaled Ibrahim Betala * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Al-A'raaf   Versículo:
قَالَا رَبَّنَا ظَلَمۡنَآ أَنفُسَنَا وَإِن لَّمۡ تَغۡفِرۡ لَنَا وَتَرۡحَمۡنَا لَنَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡخَٰسِرِينَ
Iwo (Adam ndi mkazi wake) adati (modzichepetsa): “E Mbuye wathu! Tadzichitira tokha zoipa, ngati simutikhululukira ndi kuchita nafe chifundo ndiye kuti tikhala mwa otaika.”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ ٱهۡبِطُواْ بَعۡضُكُمۡ لِبَعۡضٍ عَدُوّٞۖ وَلَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُسۡتَقَرّٞ وَمَتَٰعٌ إِلَىٰ حِينٖ
(Allah) adati: “Tsikani pansi uku pali chidani pakati panu. Ndipo padziko lapansi ndipokhala panu ndi kusangalala kwanu mpaka m’nthawi yoikidwayo.”
Las Exégesis Árabes:
قَالَ فِيهَا تَحۡيَوۡنَ وَفِيهَا تَمُوتُونَ وَمِنۡهَا تُخۡرَجُونَ
(Allah) adatinso: “Muzikakhala moyo pamenepo, ndipo muzikafa pamenepo; ndipo momwemo mudzatulutsidwa (mutauka kwa akufa).”
Las Exégesis Árabes:
يَٰبَنِيٓ ءَادَمَ قَدۡ أَنزَلۡنَا عَلَيۡكُمۡ لِبَاسٗا يُوَٰرِي سَوۡءَٰتِكُمۡ وَرِيشٗاۖ وَلِبَاسُ ٱلتَّقۡوَىٰ ذَٰلِكَ خَيۡرٞۚ ذَٰلِكَ مِنۡ ءَايَٰتِ ٱللَّهِ لَعَلَّهُمۡ يَذَّكَّرُونَ
E inu ana a Adam! Ndithu tatsitsa kwa inu chovala chobisa umaliseche wanu ndi chodzikongoletsera nacho. Koma chovala choopa nacho Allah (pakudziyeretsa ku zoletsedwa) chimenecho ndicho chabwino koposa. Zimenezo ndi zizindikiro za (chisomo cha) Allah kuti iwo akumbukire.[180]
[180] Allah akutiuza kuti tivale nsalu zomwe Allah adatipangira kuti zikongoletse matupi athu. Komatu akutilamulanso kuti tivale nsalu zokongoletsa mitima yathu; nsalu yomwe njotsatira nayo malamulo a Allah ndi kusiya zomwe Iye waletsa; ndi kuchita zokhazo zomwe Allah walamula. Nsalu imeneyi ndi “takuwa” (kuopa Allah). Sibwino kukongoletsa kunja kwa thupi kokha pomwe mu mtima mwadzaza zauve.
Las Exégesis Árabes:
يَٰبَنِيٓ ءَادَمَ لَا يَفۡتِنَنَّكُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ كَمَآ أَخۡرَجَ أَبَوَيۡكُم مِّنَ ٱلۡجَنَّةِ يَنزِعُ عَنۡهُمَا لِبَاسَهُمَا لِيُرِيَهُمَا سَوۡءَٰتِهِمَآۚ إِنَّهُۥ يَرَىٰكُمۡ هُوَ وَقَبِيلُهُۥ مِنۡ حَيۡثُ لَا تَرَوۡنَهُمۡۗ إِنَّا جَعَلۡنَا ٱلشَّيَٰطِينَ أَوۡلِيَآءَ لِلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ
E inu ana a Adam! Satana asakusokonezeni monga momwe adawatulutsira makolo anu m’Munda wamtendere ndi kuwavula onse awiri chovala chawo kuti awasonyeze umaliseche wawo. Ndithu iye ndi mtundu wake akukuonani pomwe inu simukuwaona. Ndithu asatana tawachita kukhala abwenzi a osakhulupirira.
Las Exégesis Árabes:
وَإِذَا فَعَلُواْ فَٰحِشَةٗ قَالُواْ وَجَدۡنَا عَلَيۡهَآ ءَابَآءَنَا وَٱللَّهُ أَمَرَنَا بِهَاۗ قُلۡ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَأۡمُرُ بِٱلۡفَحۡشَآءِۖ أَتَقُولُونَ عَلَى ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Ndipo (osakhulupirira) akachita chauve amanena: “(Ichi) tidawapeza nacho makolo athu (akuchichita), ndiponso Allah watilamula chimenechi.” Nena: “Ndithu Allah salamula zonyansa. Kodi mukumunenera Allah zomwe simukuzidziwa?”
Las Exégesis Árabes:
قُلۡ أَمَرَ رَبِّي بِٱلۡقِسۡطِۖ وَأَقِيمُواْ وُجُوهَكُمۡ عِندَ كُلِّ مَسۡجِدٖ وَٱدۡعُوهُ مُخۡلِصِينَ لَهُ ٱلدِّينَۚ كَمَا بَدَأَكُمۡ تَعُودُونَ
Nena: “Mbuye wanga walamula chilungamo; ndiponso (wandiuza kuti ndikuuzeni kuti) lungamitsani nkhope zanu (kwa Iye) m’nthawi ya Swala iliyonse, ndipo mpembedzeni Iye Yekha momuyeretsera chipembedzo monga Iye adakulengani pachiyambi, momwemonso mudzabwerera kwa Iye.”
Las Exégesis Árabes:
فَرِيقًا هَدَىٰ وَفَرِيقًا حَقَّ عَلَيۡهِمُ ٱلضَّلَٰلَةُۚ إِنَّهُمُ ٱتَّخَذُواْ ٱلشَّيَٰطِينَ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَيَحۡسَبُونَ أَنَّهُم مُّهۡتَدُونَ
Gulu lina waliongola, pomwe gulu lina patsimikizika pa ilo kusokera chifukwa chakuti iwo adasankha asatana kukhala atetezi (awo) kusiya Allah; ndipo akuganiza kuti iwo ngoongoka.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Al-A'raaf
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Khaled Ibrahim Betala - Índice de traducciones

Traducida por Khaled Ibrahim Petala

Cerrar