ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی آیه: (168) سوره: سوره بقره
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ كُلُواْ مِمَّا فِي ٱلۡأَرۡضِ حَلَٰلٗا طَيِّبٗا وَلَا تَتَّبِعُواْ خُطُوَٰتِ ٱلشَّيۡطَٰنِۚ إِنَّهُۥ لَكُمۡ عَدُوّٞ مُّبِينٌ
E, inu anthu! Idyani zabwino zimene zili m’nthaka zomwe zili zololedwa; ndipo musatsate mapazi a satana. Iye kwa inu ndi mdani woonekeratu.[11]
[11] E inu anthu! Idyani za mdziko lapansi zomwe zili zabwino zimene Allah wakulolezani ndipo musapenekere chilolezo chake. Musadye chinthu chosaloledwa monga kudya chinthu cha wina m’njira ya chinyengo. Musakwatule chuma chamnzanu.
Ndipo chenjerani ndi njira za satana yemwe amakukometserani zoipa. Dziwani kuti iyeyu ndi mdani wanu monga adalili mdani watate wanu Adam. Dziwaninso kuti satanayo salamula kuchita zabwino koma zoipa zokhazokha.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی آیه: (168) سوره: سوره بقره
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن