ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی * - لیست ترجمه ها


ترجمهٔ معانی آیه: (1) سوره: سوره قدر

سوره قدر

إِنَّآ أَنزَلۡنَٰهُ فِي لَيۡلَةِ ٱلۡقَدۡرِ
Ndithu taivumbulutsa (Qur’an) mu usiku wa Qadr (usiku wolemekezeka).[464]
[464] Qur’an mwachidziwikire idali kuvumbulutsidwa pang’onopang’ono kuchokera ku thambo loyamba (Baitul Izza). Choncho, usiku umene idatsika kuchokera ku thambo la seveni (Lauh Mahafudwi) kupita ku thambo loyamba udali usiku wotchedwa Laila-tul-Qadr (usiku wolemekezeka kwambiri) ndipo ndichifukwa chake kukunenedwa kuti Qur’an idatsitsidwa mu usiku wa Qadr. Umenewu ndi usiku umodzi mkati mwa mwezi wa Ramadan omwe uli wodalitsidwa kuposa miyezi chikwi chimodzi. Tanthauzo lake apa ndikuti munthu ngati achita ntchito zabwino mu usiku umenewu amapeza malipiro kuposa a yemwe wachita ntchito zabwino kokwanira miyezi chikwi chimodzi. Koma Allah adaubisa usiku umenewu. Sukudziwika kuti uli pa deti lanji ncholinga choti anthu alimbike kuchita mapemphero mwezi wonse wa Ramadan; koma ukuyembekezedwa kuti uli mu masiku khumi omaliza, makamaka usiku wodzukira pa 21, 23, 25, 27 ndi 29 kwa yemwe akufuna kupeza madalitso a usiku umenewu alimbike kuchita mapemphero kwambiri mwezi wonse.
تفسیرهای عربی:
 
ترجمهٔ معانی آیه: (1) سوره: سوره قدر
فهرست سوره ها شماره صفحه
 
ترجمهٔ معانی قرآن کریم - ترجمهٔ چوایی - لیست ترجمه ها

ترجمهٔ معانی قرآن کریم به زبان چوایی، برگردان: خالد ابراهیم بیتالا. نسخهٔ سال ۲۰۲۰ میلادی.

بستن