Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo * - Tippudi firooji ɗii


Firo maanaaji Aaya: (93) Simoore: Simoore koreeji imraan
۞ كُلُّ ٱلطَّعَامِ كَانَ حِلّٗا لِّبَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ إِلَّا مَا حَرَّمَ إِسۡرَٰٓءِيلُ عَلَىٰ نَفۡسِهِۦ مِن قَبۡلِ أَن تُنَزَّلَ ٱلتَّوۡرَىٰةُۚ قُلۡ فَأۡتُواْ بِٱلتَّوۡرَىٰةِ فَٱتۡلُوهَآ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Zakudya zonse zidali zololedwa kwa ana a Israyeli kupatula chimene adadziretsa Israyeli mwini wake Taurat isadavumbulutsidwe. Nena: “Bwerani ndi Tauratiyo ndipo iwerengeni ngati mukunena zoona.”[74]
[74] Ayuda adauza Mtumiki (s.a.w) kuti: “Iwe sukutsata chikhalidwe cha Ibrahim ngakhale umadzinyenga kuti ukumtsata. Nanga bwanji ukudya nyama ya ngamira, pomwe mneneri Ibrahim sadali kudya ngamira?” Apa Allah akuwatsutsa kuti ngabodza. Ndipo buku lawo la Taurat ndilo mboni pa bodza lawoli. atavundukula buku lawo la Taurat apeza kuti yemwe adadziletsa kudya ngamira ndi Yakobo, yemwe ankadziwikanso kuti Israeli, osati mneneri Ibrahim.Yakobo njemwe adasala kudya nyama ya ngamira mwa chifuniro chake. Ndipo izi adazichita popanda kukakamizidwa ndi Allah.
Faccirooji aarabeeji:
 
Firo maanaaji Aaya: (93) Simoore: Simoore koreeji imraan
Tippudi cimooje Tonngoode hello ngoo
 
Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo - Tippudi firooji ɗii

Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo fayde e ɗemngal siisii, fari ɗum ko Kaaliid piitalaa. Tummbutere hitaande 2020

Uddude