Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Verset: (6) Sourate: AR-RA’D
وَيَسۡتَعۡجِلُونَكَ بِٱلسَّيِّئَةِ قَبۡلَ ٱلۡحَسَنَةِ وَقَدۡ خَلَتۡ مِن قَبۡلِهِمُ ٱلۡمَثُلَٰتُۗ وَإِنَّ رَبَّكَ لَذُو مَغۡفِرَةٖ لِّلنَّاسِ عَلَىٰ ظُلۡمِهِمۡۖ وَإِنَّ رَبَّكَ لَشَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
Ndipo akukufulumizitsa kuti ubweretse choipa (chomwe ndi chilango chawo) m’malo mwa chabwino; ndithu chikhalirecho zilango zambiri zidapita kale (zomwe akadayenera kuchenjera nazo)! Koma Mbuye wako ndi mwini chikhululuko kwa anthu pa uchimo wawo. Ndipo ndithu Mbuye wako Ngolanga mwaukali.[238]
[238] China chodabwitsa cha anthu osakhulupilira mwa Allah ndiko kupempha chilango kuti chiwadzere m’malo mopempha zabwino. Iwo ankanena monga momwe zilili m’ndime ya 32 m’Sûrat Anfal kuti: “Ngati izi zimene wadza nazo Muhammad (s.a.w) nzoona zochokera kwa inu (Allah), choncho timenyeni ndi chimvula chamiyala yochokera ku mitambo; kapena chilango china chilichonse chopweteka. Koma ife sitimutsatirabe.” Umo ndi momwe idalimbira mitima ya osakhulupilira.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Verset: (6) Sourate: AR-RA’D
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture