Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Verset: (233) Sourate: AL-BAQARAH
۞ وَٱلۡوَٰلِدَٰتُ يُرۡضِعۡنَ أَوۡلَٰدَهُنَّ حَوۡلَيۡنِ كَامِلَيۡنِۖ لِمَنۡ أَرَادَ أَن يُتِمَّ ٱلرَّضَاعَةَۚ وَعَلَى ٱلۡمَوۡلُودِ لَهُۥ رِزۡقُهُنَّ وَكِسۡوَتُهُنَّ بِٱلۡمَعۡرُوفِۚ لَا تُكَلَّفُ نَفۡسٌ إِلَّا وُسۡعَهَاۚ لَا تُضَآرَّ وَٰلِدَةُۢ بِوَلَدِهَا وَلَا مَوۡلُودٞ لَّهُۥ بِوَلَدِهِۦۚ وَعَلَى ٱلۡوَارِثِ مِثۡلُ ذَٰلِكَۗ فَإِنۡ أَرَادَا فِصَالًا عَن تَرَاضٖ مِّنۡهُمَا وَتَشَاوُرٖ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡهِمَاۗ وَإِنۡ أَرَدتُّمۡ أَن تَسۡتَرۡضِعُوٓاْ أَوۡلَٰدَكُمۡ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِذَا سَلَّمۡتُم مَّآ ءَاتَيۡتُم بِٱلۡمَعۡرُوفِۗ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٞ
Ndipo akazi omwe angobereka kumene ayamwitse ana awo zaka ziwiri zathunthu kwa yemwe akufuna kukwaniritsa kuyamwitsa. Ndiudindo wa abambo kuwapezera chakudya chawo ndi chovala chawo (ana awo ndi ) amayiwo, motsatira malamulo a Shariya. Ndipo mzimu wa munthu aliyense sukakamizidwa, koma m’mene ungathere. Ndipo mayi wa mwanayo asazunzidwe chifukwa cha mwana wakeyo. Nayenso bambo wa mwanayo asazunzike chifukwa cha mwana wakeyo. Ndipo lamuloli lilinso chimodzimodzi pa mlowam’malo (ngati bambo atamwalira). Ndipo onse awiri ngati atafuna kumletsa kuyamwa, mogwirizana pakati pa awiriwo, ndi mokambirana palibe kulakwa pa iwo awiriwo. Ndipo ngati mutafuna kuwapezera ana anu akazi ena owayamwitsa (omwe si amayi awo), palibe uchimo mwa inu ngati mwapereka chimene udalonjeza kuwapatsa (oyamwitsawo) mwa ubwino. Ndipo opani Allah; dziwaninso kuti Allah akuona zonse zimene mukuchita.[38]
[38] Mwana amayamwitsidwa ndi mayi wake m’nthawi yazaka ziwiri. Ndipo akhoza kumuyamwitsa mopitilira zaka ziwiri. Ndipo mayiyo akhoza ngati atagwirizana ndi tate wamwanayo kumsiitsa zaka ziwiri zisanakwane ngati ali ndi chitsimikizo choti mwanayo sapeza masautso. Ndipo tate ngati adalekana naye ukwati mayi wa mwanayo pomwe mayiyo akupitiriza kuyamwitsa mwanayo, nkofunika kwa tate wa mwanayo kupereka malipiro kwa mayi wa mwanayo, monga kumpezera chakudya, zovala, ndalama zolipilira pamalo pokhala ndi zina zotere. Mwamuna asanene kwa mkaziyo kuti: “Uyu mwana wako. Tero uwona chochita naye.’’ Pamenepo mpovuta chifukwa mkaziyo sangapeze munthu womthandiza iye ndi mwanayo. Makamaka izi zingachitike ngati mkaziyo sanakwatiwe ndi mwamuna wina. Nayenso mayi wamwanayo asamkhwimitsire mwamunayo malipiro operekedwawo. Koma zonse zikhale zaubwino. Ngati tate wamwanayo palibe, ndiye kuti mlowam’malo wa tateyo ndiye adzakwaniritse zimenezo.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Verset: (233) Sourate: AL-BAQARAH
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture