Check out the new design

Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ * - Lexique des traductions


Traduction des sens Verset: (152) Sourate: Al 'Imran
وَلَقَدۡ صَدَقَكُمُ ٱللَّهُ وَعۡدَهُۥٓ إِذۡ تَحُسُّونَهُم بِإِذۡنِهِۦۖ حَتَّىٰٓ إِذَا فَشِلۡتُمۡ وَتَنَٰزَعۡتُمۡ فِي ٱلۡأَمۡرِ وَعَصَيۡتُم مِّنۢ بَعۡدِ مَآ أَرَىٰكُم مَّا تُحِبُّونَۚ مِنكُم مَّن يُرِيدُ ٱلدُّنۡيَا وَمِنكُم مَّن يُرِيدُ ٱلۡأٓخِرَةَۚ ثُمَّ صَرَفَكُمۡ عَنۡهُمۡ لِيَبۡتَلِيَكُمۡۖ وَلَقَدۡ عَفَا عَنكُمۡۗ وَٱللَّهُ ذُو فَضۡلٍ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithudi, Allah adakutsimikizirani lonjezo lake (lakuti muwagonjetsa adani). Choncho mudali kuwapha mwachilolezo Chake kufikira pamene mudafooka ndikuyamba kukangana za lamulolo, tero mudalinyozera pambuyo pokuonetsani zimene mumazikonda; (pamenepo mpomwe adasiya kukuthangatani). Alipo ena mwa inu amene akukonda dziko lapansi (zamdziko), ndipo alipo ena mwa inu amene akukonda tsiku lachimaliziro. Kenako (Allah) adakuchotsani pa iwo (adakusiitsani kuwamenya osakhulupirirawo) kuti akuyeseni mayeso. Koma Iye tsopano wakukhululukirani. Ndipo Allah ndi mwini kuchita zabwino pa okhulupirira.[94]
[94] Apa akulongosola chifukwa chomwe Asilamu adapezera mavuto. Iwo adapeza mavuto chifukwa choswa lamulo la Mtumiki (s.a.w) lomwe adawalamula. Mtumiki (s.a.w) adaika pa phiri anthu makumi asanu (50) omwe adali akatswiri olasa mipaliro. Adawauza kuti asachokepo kuti ateteze gulu la Asilamu kuti adani asawamenye nkhondo powadzelera kumbuyo. Adanenetsa kwa iwo kuti asachoke pamalopo ngakhale ataona kuti anzawo akupambana kapena akugonja, kufikira Mtumiki atawalamula kuti achokepo. Koma ena mwa iwo adanyoza lamuloli pamene adaona kuti anzawo chammunsi mwa phirilo akupambana ndipo akuthamangitsa adani ndi kuwapha ndikumatola zotolatola za pankhondo. Choncho, iwo anatsika paphiripo nkusakanikirana ndi anzawo nayamba kutola nawo zotola zapankhondo. Mtsogoleri wawo adayesera umu ndi umu kuwaletsa koma sadamumvere kupatula ochepa okha amene adatsala pa phiripo. Pompo ngwazi zina za m’gulu la adani awowo zitaona kuti anthu omwe adali pa phiri achokapo, zidalitembenuza gulu lawo lankhondo nkuyamba kuwamenya Asilamu chakumbuyo. Potero ambiri adaphedwa ndi kuvulala.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Verset: (152) Sourate: Al 'Imran
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ - Lexique des traductions

Traduit par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ.

Fermeture