Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa * - Lexique des traductions


Traduction des sens Verset: (16) Sourate: SABA
فَأَعۡرَضُواْ فَأَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ سَيۡلَ ٱلۡعَرِمِ وَبَدَّلۡنَٰهُم بِجَنَّتَيۡهِمۡ جَنَّتَيۡنِ ذَوَاتَيۡ أُكُلٍ خَمۡطٖ وَأَثۡلٖ وَشَيۡءٖ مِّن سِدۡرٖ قَلِيلٖ
Koma adanyozera (lamulo la Allah); choncho tidawatumizira chigumula champhamvu chamadzi otchingidwa (chomwe chidawamiza ndi kuononga minda yawo). Ndipo tidawasinthira minda yawo (yabwino) kukhala minda iwiri yazipatso zowawa, ndi mitengo ya bwemba ndi mitengo pang’ono ya masawu.[335]
[335] Anthu am’mudzi wa Saba’a komwe nkudziko la Yemeni, Allah adawapatsa madalitso ambiri pamene iwo amatsatira malamuio Ake ndi kumthokoza. Adawadalitsa ndi minda ya zipatso zokoma zomwe zidalibe nyengo yeniyeni yobalira, kotero kuti azimayi ankangosenza madengu nkumangoyenda pansi pa mitengo ndipo mwadzidzidzi ankangoona madengu ali odzaza ndi zipatso zoyoyoka m’mitengoyo. Koma pamene adasiya kumuyamika Allah ndi kutsatira malamulo Ake, adawaonongera mindayo ndi chigumula ndi kuwasinthitsira zipatso zawo ndi zipatso zopanda pake.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Verset: (16) Sourate: SABA
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - Traduction en chewa - Lexique des traductions

Traduction des sens du noble Coran en langue chewa, par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ (édition 2020).

Fermeture