Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Ayah: (50) Surah: Surah Al-Aḥzāb
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ إِنَّآ أَحۡلَلۡنَا لَكَ أَزۡوَٰجَكَ ٱلَّٰتِيٓ ءَاتَيۡتَ أُجُورَهُنَّ وَمَا مَلَكَتۡ يَمِينُكَ مِمَّآ أَفَآءَ ٱللَّهُ عَلَيۡكَ وَبَنَاتِ عَمِّكَ وَبَنَاتِ عَمَّٰتِكَ وَبَنَاتِ خَالِكَ وَبَنَاتِ خَٰلَٰتِكَ ٱلَّٰتِي هَاجَرۡنَ مَعَكَ وَٱمۡرَأَةٗ مُّؤۡمِنَةً إِن وَهَبَتۡ نَفۡسَهَا لِلنَّبِيِّ إِنۡ أَرَادَ ٱلنَّبِيُّ أَن يَسۡتَنكِحَهَا خَالِصَةٗ لَّكَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۗ قَدۡ عَلِمۡنَا مَا فَرَضۡنَا عَلَيۡهِمۡ فِيٓ أَزۡوَٰجِهِمۡ وَمَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ لِكَيۡلَا يَكُونَ عَلَيۡكَ حَرَجٞۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
E iwe Mneneri! Ndithu Ife takuloleza (kukhala nawo pamodzi) akazi ako amene wawapatsa chiwongo chawo, ndi chimene dzanja lako lamanja lapeza (omwe ndi akazi ogwidwa pa nkhondo) chomwe Allah wakupatsa, ndi ana achikazi a m’bale wa atate ako, ndi ana achikazi a mlongo wa atate ako, ndi ana achikazi a atsibweni ako, ndi ana achikazi a m’bale wa mayi ako amene adasamuka pamodzi ndi iwe, ndi mkazi wokhulupirira atadzipereka yekha kwa Mneneri ngati Mneneri akufuna kumkwatira, chilolezo ichi ncha iwe wekha, osati okhulupirira onse. Ndithu tikudziwa malamulo amene tawakhazikitsa kwa iwo pa akazi awo, ndi chimene manja awo akumanja apeza; (takuchitira zimenezi iwe wekha Mneneri Muhammad {s.a.w}) kuti pasakhale masautso pa iwe (ngati ukufuna kukwatira mkazi wina chifukwa chofalitsa chipembedzo) ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri Ngwachisoni chosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Ayah: (50) Surah: Surah Al-Aḥzāb
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup