Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Surah Al-Aḥzāb   Ayah:

Surah Al-Aḥzāb

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ ٱتَّقِ ٱللَّهَ وَلَا تُطِعِ ٱلۡكَٰفِرِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقِينَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلِيمًا حَكِيمٗا
E iwe Mneneri! Muope Allah, ndipo usamvere osakhulupirira ndi achiphamaso. Ndithu Allah Ngodziwa kwambiri; Wanzeru zakuya (m’zoyankhula ndi m’zochita Zake).[316]
[316] Sura iyi ikutchedwa Sura ya Ahzab kutanthauza kuti namtindi wa anthu. Zimenezi zidali chonchi kuti pamene Chisilamu chimafala mu mzinda wa Madina momwe mumakhalanso Ayuda, adachita nsanje yaikulu Ayudawo. Ndipo akuluakulu awo adaganiza zopita ku Makka kukakopa Arabu akumeneko kuti athandizane kuthira nkhondo Asilamu. Choncho Arabu a ku Makka adauza mitundu yonse yopembedza mafano kuti akamthire nkhondo Muhammad (s.a.w) ndi kuthetseratu chipembedzo cha Chisilamu. Tero adagwirizana ndipo adauzinga mzinda wa Madina mbali zonse. Koma Allah adatumiza angelo ndi chimphepo chamkuntho chomwe chidamwazamwaza katundu wawo. Pachifukwa ichi, onse adathawa.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱتَّبِعۡ مَا يُوحَىٰٓ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٗا
Ndipo tsata zimene zikuvumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako (pozigwiritsa ntchito). Ndithu Allah Ngodziwa zonse zimene mukuchita.
Tafsir berbahasa Arab:
وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱللَّهِۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَكِيلٗا
Ndipo yadzamira kwa Allah; ndipo Allah akukwana kukhala Msungi ndi Mtetezi (wako).
Tafsir berbahasa Arab:
مَّا جَعَلَ ٱللَّهُ لِرَجُلٖ مِّن قَلۡبَيۡنِ فِي جَوۡفِهِۦۚ وَمَا جَعَلَ أَزۡوَٰجَكُمُ ٱلَّٰٓـِٔي تُظَٰهِرُونَ مِنۡهُنَّ أُمَّهَٰتِكُمۡۚ وَمَا جَعَلَ أَدۡعِيَآءَكُمۡ أَبۡنَآءَكُمۡۚ ذَٰلِكُمۡ قَوۡلُكُم بِأَفۡوَٰهِكُمۡۖ وَٱللَّهُ يَقُولُ ٱلۡحَقَّ وَهُوَ يَهۡدِي ٱلسَّبِيلَ
Allah sadaike m’chifuwa cha munthu mitima iwiri. Ndipo sadachite akazi anu amene mukuwayesa ena mwa iwo monga amayi anu, kukhala mayi anu enieni. Ndipo sadachite ana anu ongowalera kukhala ana anu enieni (monga inu mukuwatchulira). Zimenezo ndi zolankhula zanu za pakamwa panu chabe. Koma Allah akunena choona; Iye akuongolera ku njira yoongoka.
Tafsir berbahasa Arab:
ٱدۡعُوهُمۡ لِأٓبَآئِهِمۡ هُوَ أَقۡسَطُ عِندَ ٱللَّهِۚ فَإِن لَّمۡ تَعۡلَمُوٓاْ ءَابَآءَهُمۡ فَإِخۡوَٰنُكُمۡ فِي ٱلدِّينِ وَمَوَٰلِيكُمۡۚ وَلَيۡسَ عَلَيۡكُمۡ جُنَاحٞ فِيمَآ أَخۡطَأۡتُم بِهِۦ وَلَٰكِن مَّا تَعَمَّدَتۡ قُلُوبُكُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمًا
Aitaneni ndi maina a atate awo. Kutero ndichilungamo kwa Allah. Koma ngati simukuwadziwa atate awo, (aitaneni ngati) ndiabale anu pachipembedzo; ndiponso ndi anzanu. Palibe uchimo kwa inu pa zimene mwazichita molakwitsa (mosazindikira). Koma (pali uchimo) pa zimene mitima yanu yachita mwadala. Ndipo Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni chosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
ٱلنَّبِيُّ أَوۡلَىٰ بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ مِنۡ أَنفُسِهِمۡۖ وَأَزۡوَٰجُهُۥٓ أُمَّهَٰتُهُمۡۗ وَأُوْلُواْ ٱلۡأَرۡحَامِ بَعۡضُهُمۡ أَوۡلَىٰ بِبَعۡضٖ فِي كِتَٰبِ ٱللَّهِ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُهَٰجِرِينَ إِلَّآ أَن تَفۡعَلُوٓاْ إِلَىٰٓ أَوۡلِيَآئِكُم مَّعۡرُوفٗاۚ كَانَ ذَٰلِكَ فِي ٱلۡكِتَٰبِ مَسۡطُورٗا
Mneneri ngofunika kwambiri kwa okhulupirira kuposa moyo wawo, (matupi awo ndi chuma chawo); ndipo akazi ake ndi amayi awo (amayi a Asilamu; nkoletsedwa kuwakwatira pambuyo pa imfa yake). Ndipo achibale pakati pawo ngoyenera (kulandira zamasiye pamalamulo a) m’buku la Allah kuposa Asilamu ena ngakhalenso Amuhajirina (amene adasamuka ku Makka kupita ku Madina chifukwa cha chipembedzo cha Chisilamu). Kupatula ngati mutachita zabwino kwa anzanu (sikolakwika). Izi zidalembedwa kale m’buku.[317]
[317] Ayah iyi ikufotokoza zakuletsedwa kukwatira akazi a Mtumiki (s.a.w), mwini wake atamwalira chifukwa choti akazi a Mtumiki (s.a.w) ndiamayi a Asilamu onse.
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِذۡ أَخَذۡنَا مِنَ ٱلنَّبِيِّـۧنَ مِيثَٰقَهُمۡ وَمِنكَ وَمِن نُّوحٖ وَإِبۡرَٰهِيمَ وَمُوسَىٰ وَعِيسَى ٱبۡنِ مَرۡيَمَۖ وَأَخَذۡنَا مِنۡهُم مِّيثَٰقًا غَلِيظٗا
Ndipo (akumbutse) pamene tidalandira kuchokera kwa Aneneri onse pangano lawo. Ndi kwa iwe, ndi kwa Nuh, Ibrahim, Mûsa, ndi Isa (Yesu) mwana wa Mariya. Ndipo tidatenga kwa iwo pangano lamphamvu (kuti adzafikitsa uthenga wa Allah kwa anthu ndi kuitanira anthu ku chipembedzo cha Allah).
Tafsir berbahasa Arab:
لِّيَسۡـَٔلَ ٱلصَّٰدِقِينَ عَن صِدۡقِهِمۡۚ وَأَعَدَّ لِلۡكَٰفِرِينَ عَذَابًا أَلِيمٗا
Kuti (Allah) adzafunse owona (aneneri) (tsiku la chimaliziro) pa zimene adanena (kwa anthu awo zakufikitsa uthenga woonadi kwa iwo). Ndipo Allah wawakonzera (osakhulupirira) chilango chopweteka.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱذۡكُرُواْ نِعۡمَةَ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ إِذۡ جَآءَتۡكُمۡ جُنُودٞ فَأَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ رِيحٗا وَجُنُودٗا لَّمۡ تَرَوۡهَاۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرًا
E inu amene mwakhulupirira! Kumbukirani chisomo cha Allah chimene chili pa inu, pamene adakudzerani magulu a nkhondo. Ndipo tidawatumizira mphepo ndi magulu a nkhondo (a angelo) amene simudawaone. Ndipo Allah akuona (zonse) zimene mukuchita.[318]
[318] Pamene Mtumiki (s.a.w) adali mu mzinda wa Madina adamzinga magulu ambiri a nkhondo omwe ena a iwo adali a mtundu wa Ghatfan, Ayuda a Chikuraidha ndi Ayuda a Bani Nadhir. Adali ochuluka 12,000.
Pamene Mtumiki (s.a.w) adamva za kudza kwawo adakumba chidzenje chachikulu kumbali ina ya mzinda wa Madina yomwe adaiganizira kuti adani angalowereko. Izi zidachitika potsatira malangizo a Salman Farisiyu. Kenako Mtumiki (s.a.w) adatuluka ndi ankhondo ake okwana 3,000 nakamanga mahema awo pafupi ndi chidzenjecho moyang’anizana ndi adani awo. Asilamu adagwidwa ndi mantha aakulu kotero kuti achiphamaso adayamba kuthawa. Koma pompo Allah adatumizira adaniwo chimphepo ndi magulu a nkhondo a angelo omwe sadathe kuwaona ndi maso awo, nawabalalitsa adaniwo ndi kuwatayira katundu wawo kutali.
Tafsir berbahasa Arab:
إِذۡ جَآءُوكُم مِّن فَوۡقِكُمۡ وَمِنۡ أَسۡفَلَ مِنكُمۡ وَإِذۡ زَاغَتِ ٱلۡأَبۡصَٰرُ وَبَلَغَتِ ٱلۡقُلُوبُ ٱلۡحَنَاجِرَ وَتَظُنُّونَ بِٱللَّهِ ٱلظُّنُونَا۠
Pamene adakudzerani cha kumtunda kwanu, ndi kunsi kwanu (kumtunda kwa dambo ndi kumunsi kwake), pamene maso adangoti tong’oo chammbali ndipo mitima idafika kum’mero (chifukwa cha mantha ndi kunjenjemera) uku mukumganizira Allah maganizo osiyanasiyana.
Tafsir berbahasa Arab:
هُنَالِكَ ٱبۡتُلِيَ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَزُلۡزِلُواْ زِلۡزَالٗا شَدِيدٗا
Panthawi imeneyo okhulupirira adayesedwa mayeso aakulu. Adanjenjemeretsedwa kunjenjemera kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِذۡ يَقُولُ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ وَٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ مَّا وَعَدَنَا ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥٓ إِلَّا غُرُورٗا
Ndipo pamene ankanena achiphamaso (achinyengo) ndi omwe m’mitima mwawo muli matenda: “Palibe chomwe adatilonjeza Allah ndi Mtumiki Wake koma chinyengo basi.”
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِذۡ قَالَت طَّآئِفَةٞ مِّنۡهُمۡ يَٰٓأَهۡلَ يَثۡرِبَ لَا مُقَامَ لَكُمۡ فَٱرۡجِعُواْۚ وَيَسۡتَـٔۡذِنُ فَرِيقٞ مِّنۡهُمُ ٱلنَّبِيَّ يَقُولُونَ إِنَّ بُيُوتَنَا عَوۡرَةٞ وَمَا هِيَ بِعَوۡرَةٍۖ إِن يُرِيدُونَ إِلَّا فِرَارٗا
Ndipo pamene gulu lina mwa iwo lidanena: “E inu nzika za mu Yathiriba (Madina)! Palibe njira kwa inu yokhalira (pa nkhondo yogonjayi). Choncho bwererani (ku nyumba zanu; msiyeni Muhammad alimbane yekha ndi adani ake).” Ndipo gulu lina la nkhondo lochokera mwa iwo limapempha chilolezo kwa Mneneri (s.a.w) ( chobwelera ku Madina) ponena (kuti): “Ndithu nyumba zathu nzamaliseche (zopanda chitetezo).” Koma izo sizamaliseche. Sakufuna china, koma kuthawa basi.
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَوۡ دُخِلَتۡ عَلَيۡهِم مِّنۡ أَقۡطَارِهَا ثُمَّ سُئِلُواْ ٱلۡفِتۡنَةَ لَأٓتَوۡهَا وَمَا تَلَبَّثُواْ بِهَآ إِلَّا يَسِيرٗا
Ndipo akadawalowera (magulu ankhondo a adaniwo), mbali zonse (za Mzindawo), kenako nkupemphedwa kuti atuluke m’Chisilamu ndi kumenyana ndi Asilamu, akadachita zimenezo; ndipo sakadayembekezera koma nthawi yochepa basi.
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَقَدۡ كَانُواْ عَٰهَدُواْ ٱللَّهَ مِن قَبۡلُ لَا يُوَلُّونَ ٱلۡأَدۡبَٰرَۚ وَكَانَ عَهۡدُ ٱللَّهِ مَسۡـُٔولٗا
Ndipo ndithu (awa amene adathawa pabwalo la nkhondo), adali atamulonjeza kale Allah (kuti iwo) sadzatembenuza misana (kuthawa). Ndipo lonjezo la Allah nlofunsidwa. (Choncho iwo adzafunsidwa pa zomwe adalonjeza kwa Allah).
Tafsir berbahasa Arab:
قُل لَّن يَنفَعَكُمُ ٱلۡفِرَارُ إِن فَرَرۡتُم مِّنَ ٱلۡمَوۡتِ أَوِ ٱلۡقَتۡلِ وَإِذٗا لَّا تُمَتَّعُونَ إِلَّا قَلِيلٗا
Nena: “Kuthawa sikungakuthandizeni ngati mukuthawa imfa kapena kuphedwa; choncho (kuthawa kwanuku) simusangalatsidwa (nako) koma pang’ono basi. (Kenako ikatha nthawi ya moyo wanu, mukufa).”
Tafsir berbahasa Arab:
قُلۡ مَن ذَا ٱلَّذِي يَعۡصِمُكُم مِّنَ ٱللَّهِ إِنۡ أَرَادَ بِكُمۡ سُوٓءًا أَوۡ أَرَادَ بِكُمۡ رَحۡمَةٗۚ وَلَا يَجِدُونَ لَهُم مِّن دُونِ ٱللَّهِ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا
Nena: “Kodi ndani amene angakutetezeni kwa Allah, ngati atafuna kukuchitirani choipa; kapena atafuna kukuchitirani chifundo?” Ndipo sadzapeza mthandizi ndi mtetezi kupatula Allah.
Tafsir berbahasa Arab:
۞ قَدۡ يَعۡلَمُ ٱللَّهُ ٱلۡمُعَوِّقِينَ مِنكُمۡ وَٱلۡقَآئِلِينَ لِإِخۡوَٰنِهِمۡ هَلُمَّ إِلَيۡنَاۖ وَلَا يَأۡتُونَ ٱلۡبَأۡسَ إِلَّا قَلِيلًا
Ndithu Allah akuwadziwa amene akudziletsa mwa inu (kupita ku nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) ndi kuletsanso anthu ena), ndi amene akuuza abale awo: “Bwerani kwa ife; (m’thaweni Muhammad {s.a.w}).” Ndiponso sapita ku nkhondo koma pang’ono pokha.
Tafsir berbahasa Arab:
أَشِحَّةً عَلَيۡكُمۡۖ فَإِذَا جَآءَ ٱلۡخَوۡفُ رَأَيۡتَهُمۡ يَنظُرُونَ إِلَيۡكَ تَدُورُ أَعۡيُنُهُمۡ كَٱلَّذِي يُغۡشَىٰ عَلَيۡهِ مِنَ ٱلۡمَوۡتِۖ فَإِذَا ذَهَبَ ٱلۡخَوۡفُ سَلَقُوكُم بِأَلۡسِنَةٍ حِدَادٍ أَشِحَّةً عَلَى ٱلۡخَيۡرِۚ أُوْلَٰٓئِكَ لَمۡ يُؤۡمِنُواْ فَأَحۡبَطَ ٱللَّهُ أَعۡمَٰلَهُمۡۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٗا
Okuchitirani inu umbombo (pa chikondi ndi pa chifundo; sakufunirani zabwino). Koma mantha akadza uwaona akukuyang’ana, uku maso awo akutembenuka (mophethiraphethira) monga a amene wakomoledwa ndi imfa. Koma mantha akachoka, akukupatsani masautso ndi malirime awo akuthwa; mbombo pa chabwino chilichonse. Iwowo sadakhulupirire ndipo choncho Allah wagwetsa malipiro a zochita zawo. Zimenezo nzosavuta kwa Allah.
Tafsir berbahasa Arab:
يَحۡسَبُونَ ٱلۡأَحۡزَابَ لَمۡ يَذۡهَبُواْۖ وَإِن يَأۡتِ ٱلۡأَحۡزَابُ يَوَدُّواْ لَوۡ أَنَّهُم بَادُونَ فِي ٱلۡأَعۡرَابِ يَسۡـَٔلُونَ عَنۡ أَنۢبَآئِكُمۡۖ وَلَوۡ كَانُواْ فِيكُم مَّا قَٰتَلُوٓاْ إِلَّا قَلِيلٗا
(Kufikira tsopano chifukwa cha mantha awo) akuganiza kuti magulu a nkhondo (adani) sadapitebe; ndipo magulu amenewo akadadzanso, akadalakalaka akadakhala kuchipululu pamodzi ndi arabu a kuchimidzi ndi kuti azikangofunsa za nkhani zanu. Akadakhala pamodzi ndi inu sadakamenyana (ndi adani) koma pang’ono pokha.[319]
[319] Kuyambira ndime 12 mpaka 20, Allah akufotokoza makhalidwe a anthu ena amene adangolowa m’Chisilamu ndi lirime lokha pomwe mitima yawo siidakhulupirire. Nthawi zambiri ankamchitira Mtumiki (s.a.w) zachinyengo. Mtumiki (s.a.w) akalamula lamulo loti akalimbane ndi adani achipembedzo cha Chisilamu, iwo amagwetsa ulesi anthu kuti asapite ku nkhondoko. Nthawi zambiri samawafunira Asilamu zabwino. Akangouzidwa kuti tiyeni ku nkhondo, amagwidwa ndi mantha.
Tafsir berbahasa Arab:
لَّقَدۡ كَانَ لَكُمۡ فِي رَسُولِ ٱللَّهِ أُسۡوَةٌ حَسَنَةٞ لِّمَن كَانَ يَرۡجُواْ ٱللَّهَ وَٱلۡيَوۡمَ ٱلۡأٓخِرَ وَذَكَرَ ٱللَّهَ كَثِيرٗا
Ndithu muli nacho chitsanzo chabwino mwa Mthenga wa Allah (m’kudzipereka kwake ndi khama lake pa njira ya Allah, ndi kupirira kwake ndi masautso) kwa yemwe akuopa Allah ndi tsiku lachimaliziro, namatchula Allah kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَمَّا رَءَا ٱلۡمُؤۡمِنُونَ ٱلۡأَحۡزَابَ قَالُواْ هَٰذَا مَا وَعَدَنَا ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥ وَصَدَقَ ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥۚ وَمَا زَادَهُمۡ إِلَّآ إِيمَٰنٗا وَتَسۡلِيمٗا
Ndipo pamene okhulupirira adaona magulu a nkhondo (a adani atawazinga mbali zonse), adati: “Ichi ndichimene Allah ndi Mtumiki Wake adatilonjeza (kuti tidzapeza masautso, kenako nkupambana), ndipo Allah ndi Mtumiki Wake adanena zoona.” Ndipo (ichi) sichidawaonjezere china, koma chikhulupiliro (mwa Allah) ndi kudzipereka.
Tafsir berbahasa Arab:
مِّنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ رِجَالٞ صَدَقُواْ مَا عَٰهَدُواْ ٱللَّهَ عَلَيۡهِۖ فَمِنۡهُم مَّن قَضَىٰ نَحۡبَهُۥ وَمِنۡهُم مَّن يَنتَظِرُۖ وَمَا بَدَّلُواْ تَبۡدِيلٗا
Mwa okhulupirira alipo amuna ena amene adakwaniritsa zomwe adamlonjeza Allah (kuti sadzathawa pa nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w), ena mwa iwo adamaliza moyo wawo (nakwaniritsa lonjezo lawo pofera pa njira ya Allah). Ndipo ena mwa iwo akuyembekezerabe (kufera pa njira ya Allah). Ndipo sadasinthe konse (lonjezo lawo).[320]
[320] Imamu Ibnu Jarir Taburiyu adalemba m’buku lake kuti Anasi Bun Malik adati:- M’bale wa bambo anga, Anasi bun Nadhari sadakhale nawo pa nkhondo ya Badri, ndipo adati: “Sindidakhale pamodzi ndi Mtumiki pa nkhondo yoyamba. Ngati Allah atandifikitsa pa nkhondo ina Allah adzaona zimene ndidzachita pomenya nkhondo modzipereka.” Pa tsiku la nkhondo ya Uhud, pamene Asilamu adabalalikana kuthawa ndipo iye adati:- “E Allah! Ine ndikudzipatula ku zomwe achita awa, osakhulupilira. Ndiponso ndikudandaula mzimene achita awa, Asilamu amene athawa.” Kenako adayenda ndi lupanga lake nakumana ndi Saad bun Muadhi, nati: “E iwe Saad! Ine ndikumva fungo la ku Munda wa mtendere pafupi ndi phiri ili la Uhud.” Kenako adachita nkhondo kufikira adaphedwa. Ndipo Saad adati: “E iwe Mtumiki wa Allah! Sindinathe kuchita chimene iye adachita.” Anasi bun Malik adati: “Tidampeza ali m’gulu lophedwa uku ali ndi mabala okwanira 80, ena otemedwa ndi malupanga, ndipo ena olasidwa ndi mikondo ndi mipaliro. Sitidamzindikire kufikira pamene adadza mlongo wake naamzindikira kupyolera m’nsonga za zala zake.” Ndipo Anasi adatinso: “Tidali kukambirana kuti ndime iyi ikukamba za iye.”
Tafsir berbahasa Arab:
لِّيَجۡزِيَ ٱللَّهُ ٱلصَّٰدِقِينَ بِصِدۡقِهِمۡ وَيُعَذِّبَ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ إِن شَآءَ أَوۡ يَتُوبَ عَلَيۡهِمۡۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
Kuti Allah awalipire owona chifukwa cha kuona kwawo; ndi kuti awalange achiphamaso ngati atafuna, kapena kuwalandira kulapa kwawo (ngati atalapa). Ndithu Allah Ngokhululuka kwabasi Ngwachisoni chosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
وَرَدَّ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ بِغَيۡظِهِمۡ لَمۡ يَنَالُواْ خَيۡرٗاۚ وَكَفَى ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ ٱلۡقِتَالَۚ وَكَانَ ٱللَّهُ قَوِيًّا عَزِيزٗا
Ndipo Allah adawabweza amene sadakhulupirire uku ali odzazidwa ndi mkwiyo m’mitima mwawo; sadapeze chabwino; (sadagonjetse Asilamu ndi kupeza zimene ankaziyembekezera monga zotola za pa nkhondo). Ndipo Allah adawakwaniritsira okhulupirira nkhondo (powatumizira adani mphepo yamkuntho ndi angelo). Ndipo, Allah Ngwamphamvu, Ngopambana, (sapambanidwa ndi chilichonse).
Tafsir berbahasa Arab:
وَأَنزَلَ ٱلَّذِينَ ظَٰهَرُوهُم مِّنۡ أَهۡلِ ٱلۡكِتَٰبِ مِن صَيَاصِيهِمۡ وَقَذَفَ فِي قُلُوبِهِمُ ٱلرُّعۡبَ فَرِيقٗا تَقۡتُلُونَ وَتَأۡسِرُونَ فَرِيقٗا
Ndipo adawatsitsa m’malinga mwawo amene adathandiza adaniwo mwa anthu a buku (Ayuda). Ndipo adathira mantha m’mitima mwawo. Ena mumawapha; ndipo ena mumawagwira.[321]
[321] Awa ndi Ayuda amene adasakanikirana ndi osakhulupilira (akafiri) a Chiarabu ochokera mu mtundu wa Banu Quraidhwa omwe adali ndi mapangano ndi Mtumiki (s.a.w) okhalirana mwa mtendere. Koma pamene adaswa mapangano pothandizana ndi adani a Mtumiki kuthira nkhondo Asilamu Mtumiki Muhammad (s.a.w) adawapitira ku malinga awo. Ndipo ena adawapha, pomwe ena adawagwira monga akaidi a pankhondo.
Tafsir berbahasa Arab:
وَأَوۡرَثَكُمۡ أَرۡضَهُمۡ وَدِيَٰرَهُمۡ وَأَمۡوَٰلَهُمۡ وَأَرۡضٗا لَّمۡ تَطَـُٔوهَاۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ قَدِيرٗا
Ndipo adakupatsani dziko lawo, nyumba zawo, chuma chawo, ndi nthaka imene simudaipondepo. Allah Ngokhoza chilichonse.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ قُل لِّأَزۡوَٰجِكَ إِن كُنتُنَّ تُرِدۡنَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا وَزِينَتَهَا فَتَعَالَيۡنَ أُمَتِّعۡكُنَّ وَأُسَرِّحۡكُنَّ سَرَاحٗا جَمِيلٗا
E iwe Mneneri! Nena kwa akazi ako (m’njira yowalangiza): “Ngati mufuna moyo wa dziko lapansi ndi zosangalatsa zake (ine ndilibe zosangalatsa za m’dziko, ndipo sindingakukakamizeni kuti mukhale ndi ine mu moyo wa umphawi; ngati mufuna) bwerani ndikupatsani cholekanira, chokusangalatsani, kenako ndikusiyeni kusiyana kwabwino (kopanda masautso).”
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِن كُنتُنَّ تُرِدۡنَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ وَٱلدَّارَ ٱلۡأٓخِرَةَ فَإِنَّ ٱللَّهَ أَعَدَّ لِلۡمُحۡسِنَٰتِ مِنكُنَّ أَجۡرًا عَظِيمٗا
“Ndipo ngati mukufuna Allah ndi Mtumiki Wake, ndi nyumba yomaliza, ndithu Allah wawakonzera ochita zabwino mwa inu malipiro aakulu.”
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰنِسَآءَ ٱلنَّبِيِّ مَن يَأۡتِ مِنكُنَّ بِفَٰحِشَةٖ مُّبَيِّنَةٖ يُضَٰعَفۡ لَهَا ٱلۡعَذَابُ ضِعۡفَيۡنِۚ وَكَانَ ذَٰلِكَ عَلَى ٱللَّهِ يَسِيرٗا
E inu akazi a Mneneri! Amene achite choipa choonekera mwa inu, amuonjezera chilango kawiri; ndipo zimenezi nzosavuta kwa Allah. [322]
[322] Mu Ayah imeneyi, akazi a Mtumiki (s.a.w) akuuzidwa kuti iwo akachimwa, Allah adzawalanga chilango chachikulu kuposa momwe akadalangidwira akazi ena omwe sali akazi a Mtumiki (s.a.w). Izi nchifukwa chakuti, iwo ndi atsogoleri; chilichonse chomwe iwo achita, choipa kapena chabwino, chidzatsatidwa ndi ena. Akachita chabwino, Allah adzawapatsa malipiro aakulu. Ndipo akachita choipa, adzawalanga ndi chilango chachikulu. Choncho aliyense amene ndi mtsogoleri, aonetsetse kuti akuchita zolungama zokhazokha.
Tafsir berbahasa Arab:
۞ وَمَن يَقۡنُتۡ مِنكُنَّ لِلَّهِ وَرَسُولِهِۦ وَتَعۡمَلۡ صَٰلِحٗا نُّؤۡتِهَآ أَجۡرَهَا مَرَّتَيۡنِ وَأَعۡتَدۡنَا لَهَا رِزۡقٗا كَرِيمٗا
۞ Koma yense mwa inu amene amvere Allah ndi Mneneri Wake, ndi kumachita zabwino, timpatsa malipiro ake kawiri ndi kumkonzera rizq laulemu.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰنِسَآءَ ٱلنَّبِيِّ لَسۡتُنَّ كَأَحَدٖ مِّنَ ٱلنِّسَآءِ إِنِ ٱتَّقَيۡتُنَّۚ فَلَا تَخۡضَعۡنَ بِٱلۡقَوۡلِ فَيَطۡمَعَ ٱلَّذِي فِي قَلۡبِهِۦ مَرَضٞ وَقُلۡنَ قَوۡلٗا مَّعۡرُوفٗا
E inu akazi a Mneneri! Inu simuli monga mmodzi wa akazi ena (omwe siakazi a Mtumiki, paulemelero) ngati muopa Allah. Choncho musalobodole mawu (mowakometsa poyankhulana ndi amuna,) kuti asalakelake (kuchita zoipa ndi inu) yemwe mu mtima mwake muli matenda (achiwerewere). Koma nenani zonena zabwino.
Tafsir berbahasa Arab:
وَقَرۡنَ فِي بُيُوتِكُنَّ وَلَا تَبَرَّجۡنَ تَبَرُّجَ ٱلۡجَٰهِلِيَّةِ ٱلۡأُولَىٰۖ وَأَقِمۡنَ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتِينَ ٱلزَّكَوٰةَ وَأَطِعۡنَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥٓۚ إِنَّمَا يُرِيدُ ٱللَّهُ لِيُذۡهِبَ عَنكُمُ ٱلرِّجۡسَ أَهۡلَ ٱلۡبَيۡتِ وَيُطَهِّرَكُمۡ تَطۡهِيرٗا
Ndipo khalani mnyumba zanu, ndipo musadzionetsere (kwa amuna) uku mutadzikongoletsa monga mmene ankaonetsera zokongoletsa zawo (akazi) a m’nthawi ya umbuli wakale. Ndipo pempherani Swala moyenera, perekani Zakaat, mverani Allah ndi Mtumiki Wake. Ndithu Allah akufuna kukuchotserani uve e, inu a kunyumba (ya Mneneri)! Ndi kuti akuyeretseni ndithu.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱذۡكُرۡنَ مَا يُتۡلَىٰ فِي بُيُوتِكُنَّ مِنۡ ءَايَٰتِ ٱللَّهِ وَٱلۡحِكۡمَةِۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ لَطِيفًا خَبِيرًا
Ndipo lowezani pamtima zimene zikunenedwa m’nyumba zanu; ndime za mawu a Allah ndi (zonena za Mtumiki) zanzeru. Ndithu Allah Ngodziwa zinthu zobisika kwambiri, ndi zapoyera.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ ٱلۡمُسۡلِمِينَ وَٱلۡمُسۡلِمَٰتِ وَٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ وَٱلۡقَٰنِتِينَ وَٱلۡقَٰنِتَٰتِ وَٱلصَّٰدِقِينَ وَٱلصَّٰدِقَٰتِ وَٱلصَّٰبِرِينَ وَٱلصَّٰبِرَٰتِ وَٱلۡخَٰشِعِينَ وَٱلۡخَٰشِعَٰتِ وَٱلۡمُتَصَدِّقِينَ وَٱلۡمُتَصَدِّقَٰتِ وَٱلصَّٰٓئِمِينَ وَٱلصَّٰٓئِمَٰتِ وَٱلۡحَٰفِظِينَ فُرُوجَهُمۡ وَٱلۡحَٰفِظَٰتِ وَٱلذَّٰكِرِينَ ٱللَّهَ كَثِيرٗا وَٱلذَّٰكِرَٰتِ أَعَدَّ ٱللَّهُ لَهُم مَّغۡفِرَةٗ وَأَجۡرًا عَظِيمٗا
Ndithu Asilamu achimuna ndi Asilamu achikazi; okhulupirira achimuna ndi okhulupirira achikazi; omvera achimuna ndi omvera achikazi; owona achimuna ndi owona achikazi; opirira achimuna ndi opirira achikazi; odzichepetsa achimuna ndi odzichepetsa achikazi; opereka sadaka achimuna ndi opereka sadaka achikazi; osala achimuna ndi osala achikazi; osunga umaliseche wawo (kuchiwerewere) achimuna ndi osunga umaliseche wawo achikazi; otamanda Allah kwambiri achimuna ndi otamanda Allah kwambiri achikazi, Allah wawakonzera chikhululuko ndi malipiro aakulu.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَا كَانَ لِمُؤۡمِنٖ وَلَا مُؤۡمِنَةٍ إِذَا قَضَى ٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥٓ أَمۡرًا أَن يَكُونَ لَهُمُ ٱلۡخِيَرَةُ مِنۡ أَمۡرِهِمۡۗ وَمَن يَعۡصِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَقَدۡ ضَلَّ ضَلَٰلٗا مُّبِينٗا
Ndipo sikoyenera kwa wokhulupirira wachimuna ndi wokhulupirira wachikazi, Allah ndi Mtumiki Wake akalamula chinthu, iwo nkukhala ndi chisankho pa zinthu zawo. Ndipo amene akunyoza Allah ndi Mtumiki Wake, ndithu wasokera; kusokera koonekera.[323]
[323] Ndime iyi ikunenetsa kuti sikoyenera kwa Msilamu kutsata maganizo ake pa chinthu chimene Allah ndi Mtumiki walamulapo lamulo, koma afunika kutsatira lamulo la Allah ndi Mtumiki, ndipo asakhale ndi chifuniro pa zinthu zomwe nza chipembedzo koma agonjere zimene Allah walamula ndi Mtumiki Wake. Kunyoza lamulo la Allah ndi Mtumiki kumachititsa kuti munthu atayike.
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِذۡ تَقُولُ لِلَّذِيٓ أَنۡعَمَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِ وَأَنۡعَمۡتَ عَلَيۡهِ أَمۡسِكۡ عَلَيۡكَ زَوۡجَكَ وَٱتَّقِ ٱللَّهَ وَتُخۡفِي فِي نَفۡسِكَ مَا ٱللَّهُ مُبۡدِيهِ وَتَخۡشَى ٱلنَّاسَ وَٱللَّهُ أَحَقُّ أَن تَخۡشَىٰهُۖ فَلَمَّا قَضَىٰ زَيۡدٞ مِّنۡهَا وَطَرٗا زَوَّجۡنَٰكَهَا لِكَيۡ لَا يَكُونَ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ حَرَجٞ فِيٓ أَزۡوَٰجِ أَدۡعِيَآئِهِمۡ إِذَا قَضَوۡاْ مِنۡهُنَّ وَطَرٗاۚ وَكَانَ أَمۡرُ ٱللَّهِ مَفۡعُولٗا
Ndipo (kumbuka) pamene udamuuza yemwe Allah adampatsa mtendere (pomuongolera ku Chisilamu, ndipo) iwenso udampatsa mtendere (pomulera ndi kumpatsa ufulu, yemwe ndi Zaid Bun Haritha, udati kwa iye): “Gwirizana ndi mkazi wako, ndipo wopa Allah.” Ukubisa mu mtima mwako chimene Allah afuna kuchisonyeza poyera (chomwe ndi kuti Allah akulamula kumkwatira mkazi ameneyo akamuleka Zaid Bun Haritha kuti chichoke chizolowezi choti mwana wongomulera chabe nkumuyesa mwana wako weniweni). Ndipo ukuopa anthu (kuti akudzudzula pa zimenezo), pomwe woyenera kumuopa ndi Allah. Choncho pamene Zaid adamaliza chilakolako chake pa mkazi ameneyo, tidakukwatitsa iwe kuti pasakhale masautso pa okhulupirira pokwatira akazi a ana awo akungowalera chabe ngati (anawo) atamaliza zilakolako zawo pa akaziwo, ndipo lamulo la Allah ndilochitika, (palibe chingalepheretse kuti lisachitike).[324]
[324] Polamula chinthu kuti chichitike kapena chisachitike, pafunika kuti iwe wolamula ukhale woyamba kutsata malamulowo. Ngati sutero, ndiye kuti malamulo akowo sangakhale ndi mphamvu. Mu ndime iyi muli chilolezo chomukwatira mkazi yemwe wasiyidwa ukwati ndi mwana yemwe adangoleredwa chabe ndi munthu amene amatcha mwanayo kuti ndi mwana wake chifukwa chomulera. Kalelo zoterezi sizimaloledwa. Choncho Mtumiki (s.a.w) adauzidwa kuti achite iye mwini zimenezi pofuna kuthetsa chikhalidwecho.
Tafsir berbahasa Arab:
مَّا كَانَ عَلَى ٱلنَّبِيِّ مِنۡ حَرَجٖ فِيمَا فَرَضَ ٱللَّهُ لَهُۥۖ سُنَّةَ ٱللَّهِ فِي ٱلَّذِينَ خَلَوۡاْ مِن قَبۡلُۚ وَكَانَ أَمۡرُ ٱللَّهِ قَدَرٗا مَّقۡدُورًا
Palibe tchimo pa Mneneri pa zimene Allah wamulamula. Chimenechi ndichizolowezi cha Allah (njira ya Allah) pa amene adanka kale. Ndipo lamulo la Allah ndi chikonzero (chomwe) chidakonzedwa. (Ndipo sichisinthidwa). [325]
[325] Ndime iyi ikumuuza Mtumiki (s.a.w) kuti palibe vuto pa iye ngakhale tchimo kapena kudzudzulidwa pa chomwe Allah wamulamula kuchichita monga kukwatira akazi ambiri. Ayuda amamunyoza ndi kumudzudzula chifukwa chokwatira akazi ambiri. Koma Allah adawayankha ndi mawu ake oti: “Iyi ndi njira ya Allah yomwe idalipo pa Aneneri akale! Daud adakwatira akazi 100. Ndipo Sulaimani akazi 300.
Tafsir berbahasa Arab:
ٱلَّذِينَ يُبَلِّغُونَ رِسَٰلَٰتِ ٱللَّهِ وَيَخۡشَوۡنَهُۥ وَلَا يَخۡشَوۡنَ أَحَدًا إِلَّا ٱللَّهَۗ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ حَسِيبٗا
(Aneneri) amene amafikitsa uthenga wa Allah (kwa anthu) uku akumuopa Iye, ndipo samamuopa aliyense koma Allah (yekha). Ndipo Allah Akukwana kukhala wowerengera (zochita za akapolo Ake).[326]
[326] Ndime iyi ikumuuza Mtumiki kuti amene adamulamula kuti awatsanzire pa zimene ankachita ndi iwo amene ankafikitsa uthenga wa Allah kwa anthu, ndipo samaopa kudzudzulidwa ndi aliyense pa chomwe Allah wawalamula kuchita, koma ankangoopa Allah Yekha. Choncho nawenso tsanzira khalidwe lawo ndi kuopa Allah Yekha.
Tafsir berbahasa Arab:
مَّا كَانَ مُحَمَّدٌ أَبَآ أَحَدٖ مِّن رِّجَالِكُمۡ وَلَٰكِن رَّسُولَ ٱللَّهِ وَخَاتَمَ ٱلنَّبِيِّـۧنَۗ وَكَانَ ٱللَّهُ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٗا
Muhammad (s.a.w) sali tate wa aliyense mwa amuna anu, koma iye ndi Mtumiki wa Allah, ndiponso wotsiriza mwa Aneneri. Ndipo Allah Ngodziwa chilichonse.[327]
[327] (“Khaatamu Nabiyyina) “Mneneri wotsirizira” tanthauzo lake ndi kuti Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndimneneri womalizira; palibe mneneri wina pambuyo pake mpaka kutha kwadziko lapansi. Ayah imeneyi ikutsutsa zonena za Akadiyani ndi enanso omwe akumutcha mtsogoleri wawo kuti ndi mneneri.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱذۡكُرُواْ ٱللَّهَ ذِكۡرٗا كَثِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Mkumbukireni Allah; kumkumbukira kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
وَسَبِّحُوهُ بُكۡرَةٗ وَأَصِيلًا
Ndipo mulemekezeni m’mawa ndi madzulo.[328]
[328] Allah wasankha nthawi ziwiri kuti zikhale zochulukitsa kumtamanda ndi kumulemekeza chifukwa chakuti zimenezi ndi nthawi zabwino zimene angelo amatsika kuchokera kumwamba.
Tafsir berbahasa Arab:
هُوَ ٱلَّذِي يُصَلِّي عَلَيۡكُمۡ وَمَلَٰٓئِكَتُهُۥ لِيُخۡرِجَكُم مِّنَ ٱلظُّلُمَٰتِ إِلَى ٱلنُّورِۚ وَكَانَ بِٱلۡمُؤۡمِنِينَ رَحِيمٗا
Iye ndi Amene akukuchitirani chifundo (ndi kukufunirani zabwino) nawonso Angelo Ake (akukupemphelerani kwa Allah) kuti akutulutseni mu mdima ndi kukuikani m’kuunika. Ndipo (Iye) Ngwachisoni zedi kwa okhulupirira.
Tafsir berbahasa Arab:
تَحِيَّتُهُمۡ يَوۡمَ يَلۡقَوۡنَهُۥ سَلَٰمٞۚ وَأَعَدَّ لَهُمۡ أَجۡرٗا كَرِيمٗا
Kulonjerana kwawo tsiku lokumana Naye, kudzakhala koti: “Mtendere!” Ndipo wawakonzera malipiro a ulemu.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ إِنَّآ أَرۡسَلۡنَٰكَ شَٰهِدٗا وَمُبَشِّرٗا وَنَذِيرٗا
E iwe Mneneri (wa Allah)! Ndithu Ife takutuma (kuti ukhale) mboni (pa anthu ako ndi pa mibadwo yonse). Wonena nkhani zabwino (kwa oopa Allah), ndi mchenjezi (kwa onyoza Allah).
Tafsir berbahasa Arab:
وَدَاعِيًا إِلَى ٱللَّهِ بِإِذۡنِهِۦ وَسِرَاجٗا مُّنِيرٗا
Ndi kuti ukhale woitanira (anthu) kwa Allah kupyolera m’chifuniro Chake. Ndi (kutinso ukhale) nyali younikira (anthu).
Tafsir berbahasa Arab:
وَبَشِّرِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ بِأَنَّ لَهُم مِّنَ ٱللَّهِ فَضۡلٗا كَبِيرٗا
Ndipo auze nkhani yabwino okhulupirira kuti iwo ali ndi zabwino zazikulu kwa Allah.
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَا تُطِعِ ٱلۡكَٰفِرِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَدَعۡ أَذَىٰهُمۡ وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱللَّهِۚ وَكَفَىٰ بِٱللَّهِ وَكِيلٗا
Ndipo usawamvere osakhulupirira ndi achiphamaso (pa zimene akufuna kuti uwapeputsire malamulo a Allah), usalabadire masautso awo, ndipo tsamira kwa Allah. Ndipo Allah akukwanira kukhala Mtetezi.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا نَكَحۡتُمُ ٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ ثُمَّ طَلَّقۡتُمُوهُنَّ مِن قَبۡلِ أَن تَمَسُّوهُنَّ فَمَا لَكُمۡ عَلَيۡهِنَّ مِنۡ عِدَّةٖ تَعۡتَدُّونَهَاۖ فَمَتِّعُوهُنَّ وَسَرِّحُوهُنَّ سَرَاحٗا جَمِيلٗا
E inu amene mwakhulupirira! Mukakwatira akazi okhulupirira, kenako ndikulekana nawo musadawakhudze, inu mulibe chiwerengero cha ‘Edda’ pa iwo choti nkuchiwerengera. Asangalatseni powapatsa cholekanira. siyananawoni; kusiyana kwabwino.[329]
[329] ‘Edda’ ndi nthawi imene mkazi amakhala pa chiyembekezero asanakwatiwe ndi mwamuna wina pambuyo posiyana. Edda zilipo za mitundu iwiri: yosiyana ukwati yomwe mkazi amayembekezera miyezi itatu ndi yomwalira mwamuna yomwe mkazi amayembekezera miyezi inayi ndi masiku khumi. Koma mkazi wapakati Edda yake imatha ndikubereka. Yang’anani ndemanga ya Qur’an ( 2 : 228 ).
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ إِنَّآ أَحۡلَلۡنَا لَكَ أَزۡوَٰجَكَ ٱلَّٰتِيٓ ءَاتَيۡتَ أُجُورَهُنَّ وَمَا مَلَكَتۡ يَمِينُكَ مِمَّآ أَفَآءَ ٱللَّهُ عَلَيۡكَ وَبَنَاتِ عَمِّكَ وَبَنَاتِ عَمَّٰتِكَ وَبَنَاتِ خَالِكَ وَبَنَاتِ خَٰلَٰتِكَ ٱلَّٰتِي هَاجَرۡنَ مَعَكَ وَٱمۡرَأَةٗ مُّؤۡمِنَةً إِن وَهَبَتۡ نَفۡسَهَا لِلنَّبِيِّ إِنۡ أَرَادَ ٱلنَّبِيُّ أَن يَسۡتَنكِحَهَا خَالِصَةٗ لَّكَ مِن دُونِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَۗ قَدۡ عَلِمۡنَا مَا فَرَضۡنَا عَلَيۡهِمۡ فِيٓ أَزۡوَٰجِهِمۡ وَمَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُمۡ لِكَيۡلَا يَكُونَ عَلَيۡكَ حَرَجٞۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
E iwe Mneneri! Ndithu Ife takuloleza (kukhala nawo pamodzi) akazi ako amene wawapatsa chiwongo chawo, ndi chimene dzanja lako lamanja lapeza (omwe ndi akazi ogwidwa pa nkhondo) chomwe Allah wakupatsa, ndi ana achikazi a m’bale wa atate ako, ndi ana achikazi a mlongo wa atate ako, ndi ana achikazi a atsibweni ako, ndi ana achikazi a m’bale wa mayi ako amene adasamuka pamodzi ndi iwe, ndi mkazi wokhulupirira atadzipereka yekha kwa Mneneri ngati Mneneri akufuna kumkwatira, chilolezo ichi ncha iwe wekha, osati okhulupirira onse. Ndithu tikudziwa malamulo amene tawakhazikitsa kwa iwo pa akazi awo, ndi chimene manja awo akumanja apeza; (takuchitira zimenezi iwe wekha Mneneri Muhammad {s.a.w}) kuti pasakhale masautso pa iwe (ngati ukufuna kukwatira mkazi wina chifukwa chofalitsa chipembedzo) ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri Ngwachisoni chosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
۞ تُرۡجِي مَن تَشَآءُ مِنۡهُنَّ وَتُـٔۡوِيٓ إِلَيۡكَ مَن تَشَآءُۖ وَمَنِ ٱبۡتَغَيۡتَ مِمَّنۡ عَزَلۡتَ فَلَا جُنَاحَ عَلَيۡكَۚ ذَٰلِكَ أَدۡنَىٰٓ أَن تَقَرَّ أَعۡيُنُهُنَّ وَلَا يَحۡزَنَّ وَيَرۡضَيۡنَ بِمَآ ءَاتَيۡتَهُنَّ كُلُّهُنَّۚ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ مَا فِي قُلُوبِكُمۡۚ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَلِيمٗا
Ukhoza kumchedwetsa (posagona m’nyumba mwake) amene wam’funa pakati pa iwo ndi kumuyandikitsa kwa iwe amene wam’funa. Ndipo amene wam’funa mwa amene udawapatuka, palibe tchimo pa iwe. Kuchita izi kuchititsa kuti maso awo atonthole (mitima yawo ikondwe) ndipo asadandaule; ndi kuyanjana nacho chimene wawapatsa onse. Ndipo Allah akudziwa zimene zili m’mitima mwanu. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri, Ngoleza, (salanga mwachangu).
Tafsir berbahasa Arab:
لَّا يَحِلُّ لَكَ ٱلنِّسَآءُ مِنۢ بَعۡدُ وَلَآ أَن تَبَدَّلَ بِهِنَّ مِنۡ أَزۡوَٰجٖ وَلَوۡ أَعۡجَبَكَ حُسۡنُهُنَّ إِلَّا مَا مَلَكَتۡ يَمِينُكَۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ رَّقِيبٗا
Pambuyo (pa akazi awa amene uli nawo) nkosaloledwa kwa iwe kukwatira akazi ena, (poonjezera pa chiwerengero cha akazi amene uli nawo). Ndiponso usasinthe (ofanana ndi chiwerengero chawo), (zonsezi nzoletsedwa kwa iwe) ngakhale kuti ubwino wawo utakusangalatsa, kupatula chimene dzanja lako lakumanja lapeza; ndipo Allah ndi M’yang’aniri wa chinthu chilichonse.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَدۡخُلُواْ بُيُوتَ ٱلنَّبِيِّ إِلَّآ أَن يُؤۡذَنَ لَكُمۡ إِلَىٰ طَعَامٍ غَيۡرَ نَٰظِرِينَ إِنَىٰهُ وَلَٰكِنۡ إِذَا دُعِيتُمۡ فَٱدۡخُلُواْ فَإِذَا طَعِمۡتُمۡ فَٱنتَشِرُواْ وَلَا مُسۡتَـٔۡنِسِينَ لِحَدِيثٍۚ إِنَّ ذَٰلِكُمۡ كَانَ يُؤۡذِي ٱلنَّبِيَّ فَيَسۡتَحۡيِۦ مِنكُمۡۖ وَٱللَّهُ لَا يَسۡتَحۡيِۦ مِنَ ٱلۡحَقِّۚ وَإِذَا سَأَلۡتُمُوهُنَّ مَتَٰعٗا فَسۡـَٔلُوهُنَّ مِن وَرَآءِ حِجَابٖۚ ذَٰلِكُمۡ أَطۡهَرُ لِقُلُوبِكُمۡ وَقُلُوبِهِنَّۚ وَمَا كَانَ لَكُمۡ أَن تُؤۡذُواْ رَسُولَ ٱللَّهِ وَلَآ أَن تَنكِحُوٓاْ أَزۡوَٰجَهُۥ مِنۢ بَعۡدِهِۦٓ أَبَدًاۚ إِنَّ ذَٰلِكُمۡ كَانَ عِندَ ٱللَّهِ عَظِيمًا
E inu amene mwakhulupirira! Musalowe m’nyumba za Mneneri pokhapokha chilolezo chitaperekedwa kwa inu kukadya, osati kukhala nkuyembekezera kupsa kwa chakudya. Koma mukaitanidwa, lowani. Ndipo mukamaliza kudya, balalikani; ndiponso musakambe nkhani zocheza. Chifukwa kutero kumavutitsa Mneneri. Ndipo iye amakuchitirani manyazi (kuti akutulutseni); koma Allah alibe manyazi ponena choona. Ndipo inu mukamawafunsa (akazi ake) za ziwiya, afunseni uku muli kuseri kwa Chotsekereza. Zimenezo ndi zoyera zedi ku mitima yanu ndi mitima yawo. Sikoyenera kwa inu kumvutitsa Mtumiki wa Allah, ndiponso nkosayenera kwa inu kukwatira akazi ake pambuyo pa imfa yake mpaka muyaya. Ndithu kutero ndi tchimo lalikulu kwa Allah.[330]
[330] Anasi (r.a) adanena kuti ndime iyi idatsika chifukwa cha anthu ena omwe ankangocheza m’nyumba ya Mtumiki (s.a.w), osatulukamo. Izi zidali motere: Pamene Mtumiki (s.a.w) adakwatira Zainabu Binti Jahashi, adachita phwando la chakudya ndipo adaitana anthu. Pamene adatha kudya ena a iwo adangokhala nkumacheza m’nyumba ya Mtumiki (madalitso ndi mtendere zikhale naye). Pamenepo nkuti mkazi wake atayang’anitsa nkhope yake ku khoma la nyumba. Zoterezi zidamuvuta Mtumiki (s.a.w) kuti awatulutse m’nyumbamo. Apa mpamene Allah adavumbulutsa ndimeyi.
Tafsir berbahasa Arab:
إِن تُبۡدُواْ شَيۡـًٔا أَوۡ تُخۡفُوهُ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٗا
Chilichonse chimene mungachionetse kapena kuchibisa Allah achidziwa. Ndithu chifukwa chakuti Allah Ngodziwa chilichonse.
Tafsir berbahasa Arab:
لَّا جُنَاحَ عَلَيۡهِنَّ فِيٓ ءَابَآئِهِنَّ وَلَآ أَبۡنَآئِهِنَّ وَلَآ إِخۡوَٰنِهِنَّ وَلَآ أَبۡنَآءِ إِخۡوَٰنِهِنَّ وَلَآ أَبۡنَآءِ أَخَوَٰتِهِنَّ وَلَا نِسَآئِهِنَّ وَلَا مَا مَلَكَتۡ أَيۡمَٰنُهُنَّۗ وَٱتَّقِينَ ٱللَّهَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ شَهِيدًا
Palibe tchimo pa iwo (akazi) kuonana ndi atate awo ngakhale ana awo, alongo awo, ana amuna alongo awo, ana a amuna a abale awo, akazi anzawo, ndi amene manja awo akumanja apeza. Ndipo opani Allah (inu akazi). Ndithu Allah ndimboni pa chilichonse.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ ٱللَّهَ وَمَلَٰٓئِكَتَهُۥ يُصَلُّونَ عَلَى ٱلنَّبِيِّۚ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ صَلُّواْ عَلَيۡهِ وَسَلِّمُواْ تَسۡلِيمًا
Ndithu Allah akumtsitsira madalitso Mneneri; nawonso angelo Ake (akumpemphelera chifukwa cha zochita zake zabwino). E inu amene mwakhulupirira! Mpemphereni madalitso ndi kumpemphera mtendere (chifukwa chokusonyezani njira yolungama).
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يُؤۡذُونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ لَعَنَهُمُ ٱللَّهُ فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِ وَأَعَدَّ لَهُمۡ عَذَابٗا مُّهِينٗا
Ndithu amene akumukwiyitsa Allah ndi kumuvutitsa Mtumiki Wake (ponyozera malamulo ake) Allah wawatembelera pa dziko lapansi (mpaka) pa tsiku la chimaliziro, ndipo wawakonzera chilango chosambula.
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱلَّذِينَ يُؤۡذُونَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ بِغَيۡرِ مَا ٱكۡتَسَبُواْ فَقَدِ ٱحۡتَمَلُواْ بُهۡتَٰنٗا وَإِثۡمٗا مُّبِينٗا
Ndipo amene akuvutitsa okhulupirira aamuna ndi okhulupirira aakazi popanda kuchimwa kulikonse, ndithu asenza chinyengo ndi tchimo loonekera.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّبِيُّ قُل لِّأَزۡوَٰجِكَ وَبَنَاتِكَ وَنِسَآءِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ يُدۡنِينَ عَلَيۡهِنَّ مِن جَلَٰبِيبِهِنَّۚ ذَٰلِكَ أَدۡنَىٰٓ أَن يُعۡرَفۡنَ فَلَا يُؤۡذَيۡنَۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمٗا
E iwe Mneneri! Uza akazi ako, ndi ana ako aakazi, ndi akazi a okhulupirira, kuti adziphimbe ndi nsalu zawo (akamatuluka m’nyumba), kutero kuchititsa kuti adziwike, asazunzidwe (ndi anthu achipongwe). Ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri Ngwachisoni.
Tafsir berbahasa Arab:
۞ لَّئِن لَّمۡ يَنتَهِ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ وَٱلَّذِينَ فِي قُلُوبِهِم مَّرَضٞ وَٱلۡمُرۡجِفُونَ فِي ٱلۡمَدِينَةِ لَنُغۡرِيَنَّكَ بِهِمۡ ثُمَّ لَا يُجَاوِرُونَكَ فِيهَآ إِلَّا قَلِيلٗا
Ngati sasiya (machitidwe awo oipa) achiphamaso (achinyengo), ndi amene m’mitima mwawo muli matenda (a chiwerewere), ndi ofalitsa mbiri zoipa mu mzinda, tikukhwirizira kwa iwo (kuti uwathire nkhondo). Kenako sadzakhala m’menemo pamodzi ndi iwe, koma nthawi yochepa.
Tafsir berbahasa Arab:
مَّلۡعُونِينَۖ أَيۡنَمَا ثُقِفُوٓاْ أُخِذُواْ وَقُتِّلُواْ تَقۡتِيلٗا
(Iwo) ngotembeleredwa; paliponse pamene apezeke, agwidwe ndi kuphedwa ndithu.
Tafsir berbahasa Arab:
سُنَّةَ ٱللَّهِ فِي ٱلَّذِينَ خَلَوۡاْ مِن قَبۡلُۖ وَلَن تَجِدَ لِسُنَّةِ ٱللَّهِ تَبۡدِيلٗا
(Awa ndi) machitidwe a Allah omwe adalipo pa omwe adamka kale. sungapeze kusintha pa machitidwe a Allah.
Tafsir berbahasa Arab:
يَسۡـَٔلُكَ ٱلنَّاسُ عَنِ ٱلسَّاعَةِۖ قُلۡ إِنَّمَا عِلۡمُهَا عِندَ ٱللَّهِۚ وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّ ٱلسَّاعَةَ تَكُونُ قَرِيبًا
Anthu akukufunsa za (kudza kwa) nthawi (ya tsiku la chitsiriziro). Nena: “Kuzindikira kwa nthawiyo kuli ndi Allah (Yekha). Nanga nchiyani chikudziwitse kuti nthawi ya chimaliziro iri pafupi?”
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ ٱللَّهَ لَعَنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ وَأَعَدَّ لَهُمۡ سَعِيرًا
Ndithu Allah wawatembelera osakhulupirira ndi kuwakonzera Moto woyaka kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ لَّا يَجِدُونَ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا
Adzakhala nrmenemo nthawi yaitali. Sadzapeza bwenzi ngakhale mthandizi.
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَ تُقَلَّبُ وُجُوهُهُمۡ فِي ٱلنَّارِ يَقُولُونَ يَٰلَيۡتَنَآ أَطَعۡنَا ٱللَّهَ وَأَطَعۡنَا ٱلرَّسُولَا۠
Tsiku limene nkhope zawo zikatembenuzidwa ku Moto (zikutenthedwa), uku akunena: “Kalanga ife! Tikadamumvera Allah ndi kumveranso Mtumiki (s.a.w), (sibwenzi tili m’chilangomu).”
Tafsir berbahasa Arab:
وَقَالُواْ رَبَّنَآ إِنَّآ أَطَعۡنَا سَادَتَنَا وَكُبَرَآءَنَا فَأَضَلُّونَا ٱلسَّبِيلَا۠
Ndipo adzanena: “E Mbuye wathu! Ndithu ife tidamvera olemekezeka athu ndi akuluakulu athu, choncho adatisokeza njira.”
Tafsir berbahasa Arab:
رَبَّنَآ ءَاتِهِمۡ ضِعۡفَيۡنِ مِنَ ٱلۡعَذَابِ وَٱلۡعَنۡهُمۡ لَعۡنٗا كَبِيرٗا
Mbuye wathu! Apatseni chilango pamwamba pa chilango ndipo atembelereni, kutembelera kwakukulu.”
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ ءَاذَوۡاْ مُوسَىٰ فَبَرَّأَهُ ٱللَّهُ مِمَّا قَالُواْۚ وَكَانَ عِندَ ٱللَّهِ وَجِيهٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musakhale monga amene adamvutitsa Mûsa; koma Allah adamuyeretsa kuzimene ankamnenera. Ndipo iye kwa Allah adali wolemekezeka.[331]
[331] M’ndime iyi, Allah akulangiza Asilamu kuti asamuvutitse Mtumiki ndi kumnenera mawu opanda ulemu monga momwe Ayuda ankamunenera Musa. Ana a Israeli adamunamizira Musa kuti ali ndi khate pathupi lake, kapena kuti ali ndi matenda a mwera (phudzi). Koma Allah adamuyeretsa kuzomwe adali kumunamizirazo. Adamuyeretsa motere monga momwe Bukhari akunenera muhadisi yomwe idalandiridwa kuchokera kwa Abu Huraira (r.a) kuti Mtumiki (s.a.w) adati: Musa adali munthu wamanyazi, ndipo amabisa thupi lake. Khungu lake silimaoneka chifukwa cha manyazi ake. Ndipo adamuvutitsa ena mwa ana a Israeli. Adati: “Sangadzibise motere koma pa khungu lake pali chochititsa manyazi, mwina khate kapena matenda amphepo yamwera (phudzi), kapena matenda ena aliwonse!” Ndipo Allah adafuna kumuyeretsa ku zimene ankamunamizirazo. Tsiku lina Musa adakhala payekha navula nsalu zake naika pa mwala. Kenako adayamba kusamba. Pamene adamaliza kusamba adacheukira komwe adaika nsalu zake kuti azitenge. Adaona mwala ukuthawitsa nsalu zake. Musa adatenga ndodo yake nkumathamangira mwalawo uku akunena: “Nsalu zanga, iwe mwala! Nsalu zanga iwe mwala!’’ Mpaka adadutsa pomwe adakhala akuluakulu a ana a Israeli namuona thupi lake lili losalala kwabasi; lopanda chilema chilichonse. Potero Allah adamuyeretsa ku zomwe ankamunenerazo.
Tafsir berbahasa Arab:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَقُولُواْ قَوۡلٗا سَدِيدٗا
E inu amene mwakhulupirira! Opani Allah (pokwaniritsa malamulo Ake, ndi kusiya zoletsedwa), ndipo nenani mawu olungama.
Tafsir berbahasa Arab:
يُصۡلِحۡ لَكُمۡ أَعۡمَٰلَكُمۡ وَيَغۡفِرۡ لَكُمۡ ذُنُوبَكُمۡۗ وَمَن يُطِعِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَقَدۡ فَازَ فَوۡزًا عَظِيمًا
Akukonzerani bwino zochita zanu ndi kukukhululukirani machimo anu. ndipo amene akumvera Allah ndi Mtumiki Wake, ndithu apambana; kupambana kwakukulu.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّا عَرَضۡنَا ٱلۡأَمَانَةَ عَلَى ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَٱلۡجِبَالِ فَأَبَيۡنَ أَن يَحۡمِلۡنَهَا وَأَشۡفَقۡنَ مِنۡهَا وَحَمَلَهَا ٱلۡإِنسَٰنُۖ إِنَّهُۥ كَانَ ظَلُومٗا جَهُولٗا
Ndithu Ife tidapereka udindo (otsatira malamulo) ku thambo ndi nthaka ndi mapiri; koma zidakana kuwusenza (udindowo); ndipo zidauopa. Koma munthu adawusenza; ndithu iye ngwachinyengo kwambiri ndiponso mbuli.
Tafsir berbahasa Arab:
لِّيُعَذِّبَ ٱللَّهُ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقَٰتِ وَٱلۡمُشۡرِكِينَ وَٱلۡمُشۡرِكَٰتِ وَيَتُوبَ ٱللَّهُ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمَۢا
Kuti Allah adzawalange achiphamaso aamuna ndi aakazi, ndi opembedza mafano achimuna ndi achikazi ndi kuti adzawakhululukire okhulupirira achimuna ndi achikazi. Ndipo Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni chosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Surah Al-Aḥzāb
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup