Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Surah Al-Muzzammil   Ayah:

Surah Al-Muzzammil

يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمُزَّمِّلُ
E iwe wadzifunditsa (ndi nsalu!)
Tafsir berbahasa Arab:
قُمِ ٱلَّيۡلَ إِلَّا قَلِيلٗا
Imilira usiku (upemphere), kupatula nthawi yochepa.
Tafsir berbahasa Arab:
نِّصۡفَهُۥٓ أَوِ ٱنقُصۡ مِنۡهُ قَلِيلًا
Theka lake kapena chepetsa thekalo pang’ono (mpaka ufike chimodzi mwa zigawo zitatu za usiku).
Tafsir berbahasa Arab:
أَوۡ زِدۡ عَلَيۡهِ وَرَتِّلِ ٱلۡقُرۡءَانَ تَرۡتِيلًا
Kapena wonjezapo (mpaka ufike zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za usiku;) ndipo werenga Qur’an mofatsa (lemba ndi lemba).
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّا سَنُلۡقِي عَلَيۡكَ قَوۡلٗا ثَقِيلًا
Ife tikuvumbulutsira iwe (Mneneri) mawu olemera (yomwe ndi Qur’an).
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ نَاشِئَةَ ٱلَّيۡلِ هِيَ أَشَدُّ وَطۡـٔٗا وَأَقۡوَمُ قِيلًا
Ndithu kudzuka usiku ndi kuchita mapemphero kumalowelera (mu mtima) kwambiri, ndipo zoyankhula zake zimakhala zoongoka ndi zolunjika bwino (kuposa mapemphero amasana).
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ لَكَ فِي ٱلنَّهَارِ سَبۡحٗا طَوِيلٗا
Ndithu masana uli ndi zochitachita zambiri; (umatanganidwa ndi ntchito yauthenga; dzipatse danga usiku polimbika kupemphera).
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱذۡكُرِ ٱسۡمَ رَبِّكَ وَتَبَتَّلۡ إِلَيۡهِ تَبۡتِيلٗا
Ndipo tchula dzina la Mbuye wako (Amene adalenga ndi kulera zinthu), ndipo udzipereke kwathunthu kwa Iye.
Tafsir berbahasa Arab:
رَّبُّ ٱلۡمَشۡرِقِ وَٱلۡمَغۡرِبِ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ فَٱتَّخِذۡهُ وَكِيلٗا
(Iye ndiye) Mbuye wa kuvuma ndi kuzambwe; palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye. Mchiteni kukhala Mtetezi (wanu pa zinthu zanu zonse).
Tafsir berbahasa Arab:
وَٱصۡبِرۡ عَلَىٰ مَا يَقُولُونَ وَٱهۡجُرۡهُمۡ هَجۡرٗا جَمِيلٗا
Ndipo pirira pa zimene akunena. Ndipo apewe (ndi mtima wako); kupewa kwabwino.
Tafsir berbahasa Arab:
وَذَرۡنِي وَٱلۡمُكَذِّبِينَ أُوْلِي ٱلنَّعۡمَةِ وَمَهِّلۡهُمۡ قَلِيلًا
Ndisiye Ine ndi otsutsa eni kupeza bwino; ndipo alekelere kanthawi kochepa.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ لَدَيۡنَآ أَنكَالٗا وَجَحِيمٗا
Ndithudi, tili ndi mitundumitundu ya unyolo ndi Moto woyaka,
Tafsir berbahasa Arab:
وَطَعَامٗا ذَا غُصَّةٖ وَعَذَابًا أَلِيمٗا
Ndi chakudya chotsamwitsa ndi chilango chowawa.
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَ تَرۡجُفُ ٱلۡأَرۡضُ وَٱلۡجِبَالُ وَكَانَتِ ٱلۡجِبَالُ كَثِيبٗا مَّهِيلًا
Tsiku limene nthaka ndi mapiri zidzagwedezeka; (kugwedezeka kwa mphamvu kotero kuti) mapiri adzakhala ngati mulu wa mchenga woyoyoka.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّآ أَرۡسَلۡنَآ إِلَيۡكُمۡ رَسُولٗا شَٰهِدًا عَلَيۡكُمۡ كَمَآ أَرۡسَلۡنَآ إِلَىٰ فِرۡعَوۡنَ رَسُولٗا
Ndithu Ife takutumizirani Mthenga amene adzakhala mboni yanu (tsiku la chimaliziro; monga momwe tidamtumizira (Mûsa) kukhala Mtumiki kwa Firiauni.
Tafsir berbahasa Arab:
فَعَصَىٰ فِرۡعَوۡنُ ٱلرَّسُولَ فَأَخَذۡنَٰهُ أَخۡذٗا وَبِيلٗا
Koma Firiauni adamnyoza Mtumikiyo; ndipo tidamulanga chilango chokhwima.
Tafsir berbahasa Arab:
فَكَيۡفَ تَتَّقُونَ إِن كَفَرۡتُمۡ يَوۡمٗا يَجۡعَلُ ٱلۡوِلۡدَٰنَ شِيبًا
Kodi mungadzitchinjirize chotani ngati mukana (chilango cha) tsiku (lomwe) lidzachititsa ana kukhala ndi imvi?
Tafsir berbahasa Arab:
ٱلسَّمَآءُ مُنفَطِرُۢ بِهِۦۚ كَانَ وَعۡدُهُۥ مَفۡعُولًا
Thambo (pamodzi ndi mphamvu zake ndi kukula kwake), lidzang’ambika (tsiku limenelo) chifukwa cha kuopsa kwa tsikulo, lonjezo la (Allah) lidzakwaniritsidwa (palibe wolipinga).
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ هَٰذِهِۦ تَذۡكِرَةٞۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ سَبِيلًا
Ndithudi, ma Ayah awa (amene akunena za kuwopsa kwa Qiyâma) ndichikumbutso. Choncho amene akufuna (kuthandizika nawo) ayende panjira ya Mbuye wake (pokwaniritsa malamulo Ake ndi kuleka zoipa).
Tafsir berbahasa Arab:
۞ إِنَّ رَبَّكَ يَعۡلَمُ أَنَّكَ تَقُومُ أَدۡنَىٰ مِن ثُلُثَيِ ٱلَّيۡلِ وَنِصۡفَهُۥ وَثُلُثَهُۥ وَطَآئِفَةٞ مِّنَ ٱلَّذِينَ مَعَكَۚ وَٱللَّهُ يُقَدِّرُ ٱلَّيۡلَ وَٱلنَّهَارَۚ عَلِمَ أَن لَّن تُحۡصُوهُ فَتَابَ عَلَيۡكُمۡۖ فَٱقۡرَءُواْ مَا تَيَسَّرَ مِنَ ٱلۡقُرۡءَانِۚ عَلِمَ أَن سَيَكُونُ مِنكُم مَّرۡضَىٰ وَءَاخَرُونَ يَضۡرِبُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ يَبۡتَغُونَ مِن فَضۡلِ ٱللَّهِ وَءَاخَرُونَ يُقَٰتِلُونَ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۖ فَٱقۡرَءُواْ مَا تَيَسَّرَ مِنۡهُۚ وَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتُواْ ٱلزَّكَوٰةَ وَأَقۡرِضُواْ ٱللَّهَ قَرۡضًا حَسَنٗاۚ وَمَا تُقَدِّمُواْ لِأَنفُسِكُم مِّنۡ خَيۡرٖ تَجِدُوهُ عِندَ ٱللَّهِ هُوَ خَيۡرٗا وَأَعۡظَمَ أَجۡرٗاۚ وَٱسۡتَغۡفِرُواْ ٱللَّهَۖ إِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمُۢ
Ndithu Mbuye wako akudziwa kuti iwe ukuima (kupemphera) pafupifupi magawo awiri mwa magawo atatu a usiku kapena theka lake, kape’nanso gawo limodzi mwa magawo atatu a usiku, pamodzi ndi gulu la omwe uli nawo. Ndipo Allah ndi Amene amadziwa bwino muyeso wa (nthawi za) usiku ndi usana, wadziwa kuti simungathe kuwerengera zimenezo, choncho wakukhululukirani. Werengani ndime imene yapepuka yochokera m’Qur’an. Wadziwa kuti ena mwa inu adzakhala odwala; (kudzawavuta kuimilira ndi kuchezera usiku), ndipo ena adzakhala akuyendayenda pa dziko (ndi cholinga cha malonda ndi ntchito) kunka nafunafuna ubwino wa Allah. Ndipo ena adzakhala akumenya nkhondo pa njira ya Allah (ncholinga chotukula mawu Ake), werengani chimene chapepuka chochokera mmenemo (m’Qur’an). Ndipo pitirizani kupemphera Swala, perekani chopereka (chimene chakakamizidwa kwa inu). Ndipo mkongozeni Allah ngongole yabwino. Ndipo chilichonse chabwino chimene mwadzitsogozera mudzachipeza kwa Allah chili chabwino (kuposa zomwe mudazisiya m’mbuyo) ndi malipiro akulu zedi ndipo mpempheni Allah chikhululuko (pa uchimo wanu ndi chikhululuko pakunyozera kwanu kuchita zabwino). Ndithu Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Surah Al-Muzzammil
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup