Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Versetto: (163) Sura: Al-Baqarah
وَإِلَٰهُكُمۡ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞۖ لَّآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ ٱلرَّحۡمَٰنُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo mulungu wanu ndi Mulungu mmodzi basi. Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye. Ngwachifundo chambiri, Ngwachisoni chosatha.[10]
[10] Tanthauzo la ndime iyi ndikuti Mulungu wanu wompembedza ndi mmodzi.
Palibe wompembedza mwachoonadi pa dziko lonse lapansi ndi kumwamba koma Iye Yekha. Iye Ngwachifundo chambiri, Wachisoni kwa zolengedwa Zake; Woyera ndiponso Wotukuka pachikhalidwe Chake chonse. Ndipo ali kutali ndi zimene akumunenerazo. Kodi asatukuke chotani ku zimene akumunenerazo chikhalirecho Iye ndi Yemwe adalenga thambo ndi zonse zam’menemo monga nyenyezi zikuluzikulu zomwe zikuyenda m’menemo mwadongosolo Lake lakuya popanda kuwombana ina ndi inzake. Ndipo m’dziko lapansi adaikamo zolengedwa zambiri zododometsa zomwe zikusonyeza mphamvu Zake zoposa, monga nyama zamoyo ndizomera zosiyanasiyana. Ndipo zikulozera kuti alipo amene adazilenga ndi amene akuziyang’anira yemwe ndi Allah. Dongosolo la zinthuzi likusonyeza kuti Allah ndi mmodzi chifukwa chakuti pakadakhala anzake othandizana naye pakadakhala chisokonezo, wina akadafuna china pomwe wina akufuna china.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Versetto: (163) Sura: Al-Baqarah
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi