Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Оят: (163) Сура: Бақара сураси
وَإِلَٰهُكُمۡ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞۖ لَّآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ ٱلرَّحۡمَٰنُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo mulungu wanu ndi Mulungu mmodzi basi. Palibe wopembedzedwa mwachoonadi koma Iye. Ngwachifundo chambiri, Ngwachisoni chosatha.[10]
[10] Tanthauzo la ndime iyi ndikuti Mulungu wanu wompembedza ndi mmodzi.
Palibe wompembedza mwachoonadi pa dziko lonse lapansi ndi kumwamba koma Iye Yekha. Iye Ngwachifundo chambiri, Wachisoni kwa zolengedwa Zake; Woyera ndiponso Wotukuka pachikhalidwe Chake chonse. Ndipo ali kutali ndi zimene akumunenerazo. Kodi asatukuke chotani ku zimene akumunenerazo chikhalirecho Iye ndi Yemwe adalenga thambo ndi zonse zam’menemo monga nyenyezi zikuluzikulu zomwe zikuyenda m’menemo mwadongosolo Lake lakuya popanda kuwombana ina ndi inzake. Ndipo m’dziko lapansi adaikamo zolengedwa zambiri zododometsa zomwe zikusonyeza mphamvu Zake zoposa, monga nyama zamoyo ndizomera zosiyanasiyana. Ndipo zikulozera kuti alipo amene adazilenga ndi amene akuziyang’anira yemwe ndi Allah. Dongosolo la zinthuzi likusonyeza kuti Allah ndi mmodzi chifukwa chakuti pakadakhala anzake othandizana naye pakadakhala chisokonezo, wina akadafuna china pomwe wina akufuna china.
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Оят: (163) Сура: Бақара сураси
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Қуръон Карим маъноларининг чевача таржимаси, мутаржим: Холид Иброҳим Бетала, 2020 йилда нашр қилинган

Ёпиш