Check out the new design

Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Khalid Ibrahim Betyala * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Sura: An-Naml   Versetto:
۞ فَمَا كَانَ جَوَابَ قَوۡمِهِۦٓ إِلَّآ أَن قَالُوٓاْ أَخۡرِجُوٓاْ ءَالَ لُوطٖ مِّن قَرۡيَتِكُمۡۖ إِنَّهُمۡ أُنَاسٞ يَتَطَهَّرُونَ
۞ Koma anthu ake sadayankhe yankho lina koma ili (lakuti): “Apirikitseni otsatira Luti m’mudzi mwanumu; ndithu iwo ndianthu odziyeretsa (asakhale pamodzi ndi ife adama).”
Esegesi in lingua araba:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ إِلَّا ٱمۡرَأَتَهُۥ قَدَّرۡنَٰهَا مِنَ ٱلۡغَٰبِرِينَ
Choncho tidampulumutsa iye ndi otsatira kupatula mkazi wake; tidamkozera kukhala mmodzi mwa otsalira (kuti aonongedwe pamodzi ndi oonongedwa, chifukwa cha ntchito zake zoipa ngakhale kuti adali mkazi wa mneneri).
Esegesi in lingua araba:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَسَآءَ مَطَرُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Ndipo tidawavumbwitsira mvula (yamiyala); iyipirenji mvula ya ochenjezedwa (koma osachenjezeka)!
Esegesi in lingua araba:
قُلِ ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ وَسَلَٰمٌ عَلَىٰ عِبَادِهِ ٱلَّذِينَ ٱصۡطَفَىٰٓۗ ءَآللَّهُ خَيۡرٌ أَمَّا يُشۡرِكُونَ
Nena: “Kuyamikidwa konse kwabwino nkwa Allah, ndipo mtendere ukhale pa akapolo Ake omwe adawasankha. Kodi wabwino ndi Allah kapena zimene akumphatikiza nazozo?”
Esegesi in lingua araba:
أَمَّنۡ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ وَأَنزَلَ لَكُم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَنۢبَتۡنَا بِهِۦ حَدَآئِقَ ذَاتَ بَهۡجَةٖ مَّا كَانَ لَكُمۡ أَن تُنۢبِتُواْ شَجَرَهَآۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ بَلۡ هُمۡ قَوۡمٞ يَعۡدِلُونَ
(E iwe Mtumiki! Pitiriza kuwafunsa) kodi kapena (wabwino) ndiamene adalenga thambo ndi nthaka (ndi zam’menemo) ndi kukutsitsirani madzi (mvula yothandiza) kuchokera kumwamba, choncho ndi madziwo timameretsa madimba okongola. Inu simungathe kumeretsa mitengo yake. Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu (wina)? Koma iwo (Akafiri) ndi anthu opotoka.
Esegesi in lingua araba:
أَمَّن جَعَلَ ٱلۡأَرۡضَ قَرَارٗا وَجَعَلَ خِلَٰلَهَآ أَنۡهَٰرٗا وَجَعَلَ لَهَا رَوَٰسِيَ وَجَعَلَ بَيۡنَ ٱلۡبَحۡرَيۡنِ حَاجِزًاۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ بَلۡ أَكۡثَرُهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Kodi kapena (wabwino) ndiamene adapanga nthaka kukhala malo okhazikika ndi kuika mitsinje pakati pake ndi kuipangira mapiri, ndi kuika chitsekerezo pakati pa nyanja ziwiri (nyanja ya madzi amchere, ndi yamadzi ozizira)? Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu wina? Koma ambiri a iwo sadziwa.
Esegesi in lingua araba:
أَمَّن يُجِيبُ ٱلۡمُضۡطَرَّ إِذَا دَعَاهُ وَيَكۡشِفُ ٱلسُّوٓءَ وَيَجۡعَلُكُمۡ خُلَفَآءَ ٱلۡأَرۡضِۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ قَلِيلٗا مَّا تَذَكَّرُونَ
Kapena (wabwino) ndiyemwe amamuyankha wozunzika akamampempha ndi kumchotsera masautso ake ndi kukuchitani inu kukhala oyendetsa dziko lapansi? Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu wina? Ndithu kulangizika kwanu nkochepa.
Esegesi in lingua araba:
أَمَّن يَهۡدِيكُمۡ فِي ظُلُمَٰتِ ٱلۡبَرِّ وَٱلۡبَحۡرِ وَمَن يُرۡسِلُ ٱلرِّيَٰحَ بُشۡرَۢا بَيۡنَ يَدَيۡ رَحۡمَتِهِۦٓۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ تَعَٰلَى ٱللَّهُ عَمَّا يُشۡرِكُونَ
Kapena (wabwino) ndiyemwe amakuongolerani mu mdima wa pamtunda ndi panyanja ndi kutumiza mphepo kuti ikudzetsereni nkhani yabwino patsogolo pa chifundo chake (mvula isanagwe)? Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu wina? Allah watukuka ku zimene akumuphatikiza nazo.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Sura: An-Naml
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Khalid Ibrahim Betyala - Indice Traduzioni

La sua traduzione - Khaled Ibrahim Bitala.

Chiudi