Check out the new design

Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: En-Neml   Ajet:
۞ فَمَا كَانَ جَوَابَ قَوۡمِهِۦٓ إِلَّآ أَن قَالُوٓاْ أَخۡرِجُوٓاْ ءَالَ لُوطٖ مِّن قَرۡيَتِكُمۡۖ إِنَّهُمۡ أُنَاسٞ يَتَطَهَّرُونَ
۞ Koma anthu ake sadayankhe yankho lina koma ili (lakuti): “Apirikitseni otsatira Luti m’mudzi mwanumu; ndithu iwo ndianthu odziyeretsa (asakhale pamodzi ndi ife adama).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ إِلَّا ٱمۡرَأَتَهُۥ قَدَّرۡنَٰهَا مِنَ ٱلۡغَٰبِرِينَ
Choncho tidampulumutsa iye ndi otsatira kupatula mkazi wake; tidamkozera kukhala mmodzi mwa otsalira (kuti aonongedwe pamodzi ndi oonongedwa, chifukwa cha ntchito zake zoipa ngakhale kuti adali mkazi wa mneneri).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَسَآءَ مَطَرُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Ndipo tidawavumbwitsira mvula (yamiyala); iyipirenji mvula ya ochenjezedwa (koma osachenjezeka)!
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلِ ٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ وَسَلَٰمٌ عَلَىٰ عِبَادِهِ ٱلَّذِينَ ٱصۡطَفَىٰٓۗ ءَآللَّهُ خَيۡرٌ أَمَّا يُشۡرِكُونَ
Nena: “Kuyamikidwa konse kwabwino nkwa Allah, ndipo mtendere ukhale pa akapolo Ake omwe adawasankha. Kodi wabwino ndi Allah kapena zimene akumphatikiza nazozo?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمَّنۡ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ وَأَنزَلَ لَكُم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ مَآءٗ فَأَنۢبَتۡنَا بِهِۦ حَدَآئِقَ ذَاتَ بَهۡجَةٖ مَّا كَانَ لَكُمۡ أَن تُنۢبِتُواْ شَجَرَهَآۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ بَلۡ هُمۡ قَوۡمٞ يَعۡدِلُونَ
(E iwe Mtumiki! Pitiriza kuwafunsa) kodi kapena (wabwino) ndiamene adalenga thambo ndi nthaka (ndi zam’menemo) ndi kukutsitsirani madzi (mvula yothandiza) kuchokera kumwamba, choncho ndi madziwo timameretsa madimba okongola. Inu simungathe kumeretsa mitengo yake. Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu (wina)? Koma iwo (Akafiri) ndi anthu opotoka.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمَّن جَعَلَ ٱلۡأَرۡضَ قَرَارٗا وَجَعَلَ خِلَٰلَهَآ أَنۡهَٰرٗا وَجَعَلَ لَهَا رَوَٰسِيَ وَجَعَلَ بَيۡنَ ٱلۡبَحۡرَيۡنِ حَاجِزًاۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ بَلۡ أَكۡثَرُهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Kodi kapena (wabwino) ndiamene adapanga nthaka kukhala malo okhazikika ndi kuika mitsinje pakati pake ndi kuipangira mapiri, ndi kuika chitsekerezo pakati pa nyanja ziwiri (nyanja ya madzi amchere, ndi yamadzi ozizira)? Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu wina? Koma ambiri a iwo sadziwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمَّن يُجِيبُ ٱلۡمُضۡطَرَّ إِذَا دَعَاهُ وَيَكۡشِفُ ٱلسُّوٓءَ وَيَجۡعَلُكُمۡ خُلَفَآءَ ٱلۡأَرۡضِۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ قَلِيلٗا مَّا تَذَكَّرُونَ
Kapena (wabwino) ndiyemwe amamuyankha wozunzika akamampempha ndi kumchotsera masautso ake ndi kukuchitani inu kukhala oyendetsa dziko lapansi? Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu wina? Ndithu kulangizika kwanu nkochepa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَمَّن يَهۡدِيكُمۡ فِي ظُلُمَٰتِ ٱلۡبَرِّ وَٱلۡبَحۡرِ وَمَن يُرۡسِلُ ٱلرِّيَٰحَ بُشۡرَۢا بَيۡنَ يَدَيۡ رَحۡمَتِهِۦٓۗ أَءِلَٰهٞ مَّعَ ٱللَّهِۚ تَعَٰلَى ٱللَّهُ عَمَّا يُشۡرِكُونَ
Kapena (wabwino) ndiyemwe amakuongolerani mu mdima wa pamtunda ndi panyanja ndi kutumiza mphepo kuti ikudzetsereni nkhani yabwino patsogolo pa chifundo chake (mvula isanagwe)? Kodi pamodzi ndi Allah pali mulungu wina? Allah watukuka ku zimene akumuphatikiza nazo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: En-Neml
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala - Sadržaj prijevodā

Halid Ibrahim Bejtala je preveo.

Zatvaranje