Check out the new design

Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: En-Neml   Ajet:
إِنِّي وَجَدتُّ ٱمۡرَأَةٗ تَمۡلِكُهُمۡ وَأُوتِيَتۡ مِن كُلِّ شَيۡءٖ وَلَهَا عَرۡشٌ عَظِيمٞ
“Ndithu ine ndapeza mkazi akuwalamulira (anthu a ku dziko la Saba), ndipo wapatsidwa chilichonse; ndiponso ali ndi chimpando chachifumu chachikulu.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَجَدتُّهَا وَقَوۡمَهَا يَسۡجُدُونَ لِلشَّمۡسِ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَزَيَّنَ لَهُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ أَعۡمَٰلَهُمۡ فَصَدَّهُمۡ عَنِ ٱلسَّبِيلِ فَهُمۡ لَا يَهۡتَدُونَ
“Ndampeza iye ndi anthu ake akulambira dzuwa kusiya Allah; ndipo satana wawakometsera zochita zawo zoipa; choncho wawatsekereza ku njira yolungama, tero sadaongoke.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَّاۤ يَسۡجُدُواْۤ لِلَّهِ ٱلَّذِي يُخۡرِجُ ٱلۡخَبۡءَ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَيَعۡلَمُ مَا تُخۡفُونَ وَمَا تُعۡلِنُونَ
“Kuti asamlambire Allah yemwe amatulutsa zobisika kumwamba ndi pansi; ndipo akudziwa zimene mukubisa ndi zimene muonetsa poyera.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱللَّهُ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَ رَبُّ ٱلۡعَرۡشِ ٱلۡعَظِيمِ۩
“Allah! Palibe wina wopembedzedwa mwachoona koma Iye basi; Mbuye wa Arsh (Mpando wachifumu) waukulu.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
۞ قَالَ سَنَنظُرُ أَصَدَقۡتَ أَمۡ كُنتَ مِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
(Sulaiman) adati “Tiona ngati wanena zoona kapena ngati) uli m’gulu la onama.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
ٱذۡهَب بِّكِتَٰبِي هَٰذَا فَأَلۡقِهۡ إِلَيۡهِمۡ ثُمَّ تَوَلَّ عَنۡهُمۡ فَٱنظُرۡ مَاذَا يَرۡجِعُونَ
“Pita ndi kalata yangayi, kaiponye kwa iwo; kenako ukadzipatule kwa iwo (ukakhale pambali) ndi kuona momwe azikayankhira.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالَتۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمَلَؤُاْ إِنِّيٓ أُلۡقِيَ إِلَيَّ كِتَٰبٞ كَرِيمٌ
(Mfumukazi) idati; “E inu nduna! Ndithu kalata yolemekezeka yaponyedwa kwa ine.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
إِنَّهُۥ مِن سُلَيۡمَٰنَ وَإِنَّهُۥ بِسۡمِ ٱللَّهِ ٱلرَّحۡمَٰنِ ٱلرَّحِيمِ
“Yachokera kwa Sulaiman, ndipo mawu ake ndi awa: ‘Mdzina la Allah, Wachifundo chambiri, Wachisoni.’
Tefsiri na arapskom jeziku:
أَلَّا تَعۡلُواْ عَلَيَّ وَأۡتُونِي مُسۡلِمِينَ
‘Musadzikweze kwa ine, ndipo idzani kwa ine muli ogonjera malamulo anga.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالَتۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡمَلَؤُاْ أَفۡتُونِي فِيٓ أَمۡرِي مَا كُنتُ قَاطِعَةً أَمۡرًا حَتَّىٰ تَشۡهَدُونِ
(Mfumukazi idaonjezera) kunena: “E inu nduna! ndilangizeni pankhani yangayi; sindilamula kanthu mpaka inu mutandibwerera.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالُواْ نَحۡنُ أُوْلُواْ قُوَّةٖ وَأُوْلُواْ بَأۡسٖ شَدِيدٖ وَٱلۡأَمۡرُ إِلَيۡكِ فَٱنظُرِي مَاذَا تَأۡمُرِينَ
(Nduna) zidati: “Ife ndife eni nyonga ndi eni kumenya nkhondo mwaukali; koma zonse zili ndi inu; choncho yang’anani mmene mungalamulire.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
قَالَتۡ إِنَّ ٱلۡمُلُوكَ إِذَا دَخَلُواْ قَرۡيَةً أَفۡسَدُوهَا وَجَعَلُوٓاْ أَعِزَّةَ أَهۡلِهَآ أَذِلَّةٗۚ وَكَذَٰلِكَ يَفۡعَلُونَ
(Mfumukazi) idati: “Ndithu mafumu akamalowa m’mudzi (wa anthu), amauononga motheratu, ndi kuwachita olemekezeka a m’menemo kukhala onyozeka. Mmenemo ndimomwe amachitira (nthawi zonse).”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَإِنِّي مُرۡسِلَةٌ إِلَيۡهِم بِهَدِيَّةٖ فَنَاظِرَةُۢ بِمَ يَرۡجِعُ ٱلۡمُرۡسَلُونَ
“Koma ine nditumiza mitulo kwa iwo ndi kuyembekezera zimene abwere nazo otumidwawo.”
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: En-Neml
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala - Sadržaj prijevodā

Halid Ibrahim Bejtala je preveo.

Zatvaranje