Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Versetto: (27) Sura: Al-Mâ’idah
۞ وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ ٱبۡنَيۡ ءَادَمَ بِٱلۡحَقِّ إِذۡ قَرَّبَا قُرۡبَانٗا فَتُقُبِّلَ مِنۡ أَحَدِهِمَا وَلَمۡ يُتَقَبَّلۡ مِنَ ٱلۡأٓخَرِ قَالَ لَأَقۡتُلَنَّكَۖ قَالَ إِنَّمَا يَتَقَبَّلُ ٱللَّهُ مِنَ ٱلۡمُتَّقِينَ
Ndipo awerengere nkhani mwachoonadi ya ana awiri a Adam, pamene adapereka nsembe. Ndipo idalandiridwa ya mmodzi wawo, koma ya winayo siidalandiridwe. (Amene nsembe yake siidalandiridwe) adati (kwa mnzake): “Ndithudi ndikupha.” Mnzakeyo adati: “Ndithudi, Allah amalandira nsembe ya amene akuopa (Allah).”[163]
[163] Iyi ndinkhani yoyamba ya munthu wopha mnzake. Ndipo amene adaphedwayu ndiye munthu woyamba kulawa imfa. Wopha mnzakeyo ataona kuti mnzake wafadi, iye adangoti kakasi, kusowa chochita naye. Tero adangomsenza kumsana nkumangozungilirazungulira naye, kuopa kubwera naye kunyumba kuti anzake angamdziwe kuti ndiye wamupha. Makolo awo adali Adam ndi Hava. Mwamwayi, khwangwala adatulukira nayamba kumenyana ndimnzake mpaka kumupha. Kenako namkwilira m’nthaka. Tsono naye uja wopha mnzake adatsanzira zomwe khwangwala adachita. Nakumba dzenje nkukwilira mnzakeyo. N.B! Munthu ncholengedwa chomalizira kudza pa dziko. Zidamtsogolera zolengedwa zonse ndi zaka miyandamiyanda.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Versetto: (27) Sura: Al-Mâ’idah
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi