《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (27) 章: 玛仪戴
۞ وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ ٱبۡنَيۡ ءَادَمَ بِٱلۡحَقِّ إِذۡ قَرَّبَا قُرۡبَانٗا فَتُقُبِّلَ مِنۡ أَحَدِهِمَا وَلَمۡ يُتَقَبَّلۡ مِنَ ٱلۡأٓخَرِ قَالَ لَأَقۡتُلَنَّكَۖ قَالَ إِنَّمَا يَتَقَبَّلُ ٱللَّهُ مِنَ ٱلۡمُتَّقِينَ
Ndipo awerengere nkhani mwachoonadi ya ana awiri a Adam, pamene adapereka nsembe. Ndipo idalandiridwa ya mmodzi wawo, koma ya winayo siidalandiridwe. (Amene nsembe yake siidalandiridwe) adati (kwa mnzake): “Ndithudi ndikupha.” Mnzakeyo adati: “Ndithudi, Allah amalandira nsembe ya amene akuopa (Allah).”[163]
[163] Iyi ndinkhani yoyamba ya munthu wopha mnzake. Ndipo amene adaphedwayu ndiye munthu woyamba kulawa imfa. Wopha mnzakeyo ataona kuti mnzake wafadi, iye adangoti kakasi, kusowa chochita naye. Tero adangomsenza kumsana nkumangozungilirazungulira naye, kuopa kubwera naye kunyumba kuti anzake angamdziwe kuti ndiye wamupha. Makolo awo adali Adam ndi Hava. Mwamwayi, khwangwala adatulukira nayamba kumenyana ndimnzake mpaka kumupha. Kenako namkwilira m’nthaka. Tsono naye uja wopha mnzake adatsanzira zomwe khwangwala adachita. Nakumba dzenje nkukwilira mnzakeyo. N.B! Munthu ncholengedwa chomalizira kudza pa dziko. Zidamtsogolera zolengedwa zonse ndi zaka miyandamiyanda.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (27) 章: 玛仪戴
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭