Check out the new design

Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Khalid Ibrahim Betyala * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Sura: Al-An‘âm   Versetto:
۞ وَلَوۡ أَنَّنَا نَزَّلۡنَآ إِلَيۡهِمُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ وَكَلَّمَهُمُ ٱلۡمَوۡتَىٰ وَحَشَرۡنَا عَلَيۡهِمۡ كُلَّ شَيۡءٖ قُبُلٗا مَّا كَانُواْ لِيُؤۡمِنُوٓاْ إِلَّآ أَن يَشَآءَ ٱللَّهُ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ يَجۡهَلُونَ
۞ Ndipo ngati tikadawatumizira angelo (kuti adzaikire umboni za uneneri wako), ndipo akufa nkuwayankhula, (naonso nkuvomereza kuti izi nzoona; kuonjezera apo) nkuwasonkhanitsira chinthu chilichonse pamaso pawo, sakadakhulupirira pokhapokha Allah akadafuna koma ambiri a iwo sazindikira.
Esegesi in lingua araba:
وَكَذَٰلِكَ جَعَلۡنَا لِكُلِّ نَبِيٍّ عَدُوّٗا شَيَٰطِينَ ٱلۡإِنسِ وَٱلۡجِنِّ يُوحِي بَعۡضُهُمۡ إِلَىٰ بَعۡضٖ زُخۡرُفَ ٱلۡقَوۡلِ غُرُورٗاۚ وَلَوۡ شَآءَ رَبُّكَ مَا فَعَلُوهُۖ فَذَرۡهُمۡ وَمَا يَفۡتَرُونَ
Ndipo nchomwechi tidamuikira adani mneneri aliyense (omwe) ndi asatana a mu anthu ndi asatana a m’ziwanda, (omwe) amadziwitsana wina ndi mnzake mawu okometsa ncholinga chonyenga. Ndipo Mbuye wako akadafuna, sakadatha kuchita zimenezi choncho asiye ndi zimene akupeka.
Esegesi in lingua araba:
وَلِتَصۡغَىٰٓ إِلَيۡهِ أَفۡـِٔدَةُ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡأٓخِرَةِ وَلِيَرۡضَوۡهُ وَلِيَقۡتَرِفُواْ مَا هُم مُّقۡتَرِفُونَ
Ndi kuti ipendekere ku mawu amenewo mitima ya anthu osakhulupirira tsiku la chimaliziro, ndi kuyanjana nawo (mawuo) ndikutinso apeze (machimo) omwe amawapeza.
Esegesi in lingua araba:
أَفَغَيۡرَ ٱللَّهِ أَبۡتَغِي حَكَمٗا وَهُوَ ٱلَّذِيٓ أَنزَلَ إِلَيۡكُمُ ٱلۡكِتَٰبَ مُفَصَّلٗاۚ وَٱلَّذِينَ ءَاتَيۡنَٰهُمُ ٱلۡكِتَٰبَ يَعۡلَمُونَ أَنَّهُۥ مُنَزَّلٞ مِّن رَّبِّكَ بِٱلۡحَقِّۖ فَلَا تَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمُمۡتَرِينَ
(Nena:) “Kodi ndifune woweruza wina kusiya Allah, pomwe Iye ndi Yemwe adavumbulutsa buku kwa inu lofotokoza chilichonse?” Ndipo omwe tidawapatsa buku akudziwa kuti (Qur’an) yavumbulutsidwa ndi Mbuye wako mwachoonadi. Choncho, usakhale mwa okaikira.
Esegesi in lingua araba:
وَتَمَّتۡ كَلِمَتُ رَبِّكَ صِدۡقٗا وَعَدۡلٗاۚ لَّا مُبَدِّلَ لِكَلِمَٰتِهِۦۚ وَهُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndipo mawu a Mbuye wako akwanira moona ndi mwachilungamo. Palibe amene angathe kusintha mawu Ake. Iye Ngwakumva, Ngodziwa.
Esegesi in lingua araba:
وَإِن تُطِعۡ أَكۡثَرَ مَن فِي ٱلۡأَرۡضِ يُضِلُّوكَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۚ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّ وَإِنۡ هُمۡ إِلَّا يَخۡرُصُونَ
Ngati umvera ambiri amene ali pa dziko lapansi, akusokeretsa pa njira ya Allah. Satsatira koma zakungoganizira. Ndipo sali chilichonse koma akungonama
Esegesi in lingua araba:
إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ مَن يَضِلُّ عَن سَبِيلِهِۦۖ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِٱلۡمُهۡتَدِينَ
Ndithu Mbuye wako ndi Yemwe akudziwa bwino amene asokera ku njira Yake, ndiponso Iye akudziwa bwino za oongoka.
Esegesi in lingua araba:
فَكُلُواْ مِمَّا ذُكِرَ ٱسۡمُ ٱللَّهِ عَلَيۡهِ إِن كُنتُم بِـَٔايَٰتِهِۦ مُؤۡمِنِينَ
Choncho, idyani (nyama) zomwe dzina la Allah latchulidwapo (pozizinga osati zofa zokha), ngati inu mukhulupiriradi Ayah (zizindikiro) Zake.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Sura: Al-An‘âm
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Khalid Ibrahim Betyala - Indice Traduzioni

La sua traduzione - Khaled Ibrahim Bitala.

Chiudi