クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (22) 章: 雷電章
وَٱلَّذِينَ صَبَرُواْ ٱبۡتِغَآءَ وَجۡهِ رَبِّهِمۡ وَأَقَامُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَأَنفَقُواْ مِمَّا رَزَقۡنَٰهُمۡ سِرّٗا وَعَلَانِيَةٗ وَيَدۡرَءُونَ بِٱلۡحَسَنَةِ ٱلسَّيِّئَةَ أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ عُقۡبَى ٱلدَّارِ
Ndi omwenso amapirira chifukwa chofuna chiyanjo cha Mbuye wawo ndi kupemphera Swala ndi kupereka mu zomwe tawapatsa, mobisa ndi moonekera, ndi kuchotsa choipa ndi chabwino (pochita chabwino pa choipacho); iwo ndi omwe adzapeza malipiro (abwino) a ku Nyumba ya tsiku la chimaliziro.[241]
[241] Kunena koti: “Kupereka mobisa ndi moonekera.” kukusonyeza kuti sadaka zomwe munthu akupereka asazifunire nthawi yake yeniyeni yoperekera. Koma nthawi iliyonse. Ngati nkofunika kupereka mobisa kuopera kuti omwe akupatsidwawo asanyozeke kumaso kwa anthu, apereke mobisa. Ndipo ngati nkofunika kupereka moonetsera, ncholinga choti anthu ena atsanzire, monga kusonkhetsa kwa poyera, apereke moonekera. Tsono kunena kwakuti: “Kuchotsa choipa ndi chabwino,” kukutanthauza kuti anthu amenewa akawachitira zoipa ena, iwo sabwezera zoipazo. Koma amapitiriza kuchitira anthu oipawo zabwino.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (22) 章: 雷電章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる