クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (121) 章: イムラ―ン家章
وَإِذۡ غَدَوۡتَ مِنۡ أَهۡلِكَ تُبَوِّئُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ مَقَٰعِدَ لِلۡقِتَالِۗ وَٱللَّهُ سَمِيعٌ عَلِيمٌ
(Kumbukira) pamene unachoka m’mawa kusiya banja lako kuti uwakonzere Asilamu malo omenyanira (nkhondo). Ndipo Allah Ngwakumva, Ngodziwa.[83]
[83] Apa akunena nkhani ya nkhondo yachiwiri yaikulu kwabasi pambiri ya Chisilamu, nkhondo ya Uhudi. Nkhondo imeneyi Asilamu adakumana ndi masautso akulu chifukwa cha Asilamu ena amene adaswa lamulo la Mtumiki (s.a.w). Ndiponso chifukwa cha anthu ena omwe adalowa Chisilamu mwachiphamaso, (achiphamaso) omwe adapita ku nkhondo pamodzi ndi Mtumiki (s.a.w) koma adakathawa kunkhondoko. Ndipo adali ochuluka gawo limodzi mwa magawo atatu a Asilamu (1/3). Pothawapo adathawa ochuluka kuposa nambala yatchulidwayi. Koma ena mwa iwo adabwerera nkudzalumikizananso ndi gulu la nkhondo la Mtumiki (s.a.w).
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (121) 章: イムラ―ン家章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる