クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (97) 章: 婦人章
إِنَّ ٱلَّذِينَ تَوَفَّىٰهُمُ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ ظَالِمِيٓ أَنفُسِهِمۡ قَالُواْ فِيمَ كُنتُمۡۖ قَالُواْ كُنَّا مُسۡتَضۡعَفِينَ فِي ٱلۡأَرۡضِۚ قَالُوٓاْ أَلَمۡ تَكُنۡ أَرۡضُ ٱللَّهِ وَٰسِعَةٗ فَتُهَاجِرُواْ فِيهَاۚ فَأُوْلَٰٓئِكَ مَأۡوَىٰهُمۡ جَهَنَّمُۖ وَسَآءَتۡ مَصِيرًا
Ndithudi amene angelo atenga miyoyo yawo, ali odzichitira okha zoipa (posasamuka ku Makka), adzawauza kuti: “Mudachitanji (pachipembedzo chanu?)” Iwo adzati: “Tidali ofooka ndi oponderezedwa padziko; (choncho sitidathe kuchita mapemphero athu).” (Angelo) adzati: “Kodi dziko la Allah silidali lotambasuka kotero kuti inu nkusamukira kwina m’menemo?” Iwowo malo awo ndi Jahannam. Taonani kuipa kwa malo obwerera.[136]
[136] (Ndime 97-99) Kalelo Mtumiki (s.a.w) atasamukira ku Madina pamodzi ndi omtsatira ake, Asilamu adawalamula kuti asamukire ku Madinako kusiya nyumba zawo, chuma chawo, abale awo ndi ana awo. Izi zidali chonchi chifukwa iwo akanakhalabe m’midzi yawo pansi pautsogoleri wa anthu osakhulupilira sakanatha kukwaniritsa malamulo a Chisilamu. Tero Chisilamu chake sichikanakhala ndi ntchito. Ndipo Chisilamu chopanda ntchito si Chisilamunso. Tero nchifukwa chake apa akuwadzudzula amene sanasamuke kuti adzafa ndi imfa yoipa kupatula okhawo amene sanapeze njira yosamukira ku Madina chifukwa chakufooka kwa matupi awo. Amenewa madandaulo awo akhoza kuwavomera. Koma chachikulu nkuti ayesetse kusamukira ku Madina.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (97) 章: 婦人章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる