クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (2) 章: 食卓章
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تُحِلُّواْ شَعَٰٓئِرَ ٱللَّهِ وَلَا ٱلشَّهۡرَ ٱلۡحَرَامَ وَلَا ٱلۡهَدۡيَ وَلَا ٱلۡقَلَٰٓئِدَ وَلَآ ءَآمِّينَ ٱلۡبَيۡتَ ٱلۡحَرَامَ يَبۡتَغُونَ فَضۡلٗا مِّن رَّبِّهِمۡ وَرِضۡوَٰنٗاۚ وَإِذَا حَلَلۡتُمۡ فَٱصۡطَادُواْۚ وَلَا يَجۡرِمَنَّكُمۡ شَنَـَٔانُ قَوۡمٍ أَن صَدُّوكُمۡ عَنِ ٱلۡمَسۡجِدِ ٱلۡحَرَامِ أَن تَعۡتَدُواْۘ وَتَعَاوَنُواْ عَلَى ٱلۡبِرِّ وَٱلتَّقۡوَىٰۖ وَلَا تَعَاوَنُواْ عَلَى ٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡعُدۡوَٰنِۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَۖ إِنَّ ٱللَّهَ شَدِيدُ ٱلۡعِقَابِ
E inu amene mwakhulupirira! Musanyozere kupatulika kwa zizindikiro za Allah (pochiyesa chosapatulika chomwe Allah wachichita kukhala chopatulika; monga kutuluka m’mapemphero a Hajj usadakwaniritse), kapenanso (kunyozera) kupatulika kwa mwezi wopatulika (poyambitsa nkhondo mmenemo), kapena (kupatulika kwa nyama zomwe zatumizidwa ku Makka monga) nsembe, kapena (kuchotsa kupatulika kwa) makoza (omwe nyamazo zimavekedwa monga chizindikiro chosonyeza kuti ndinsembe ya ku Makka), kapena (kupatulika kwa) omwe akulinga kupita kunyumba yopatulika (ku Makka), (omwe akupita kumeneko) ndi cholinga chofunafuna ubwino wa Mbuye wawo ndi chiyanjo Chake. Ndipo ngati mutatuluka m’mapemphero anu a Hajj mukhoza kuchita ulenje (ngati mutafuna); ndipo kusakuchititseni kuwada anthu chifukwa chakuti adakutsekerezani kufika ku Msikiti Wopatulika (wa ku Makka) kuti mulumphe malire (pobwezera mtopola umene adakuchitirani). Koma thandizanani pa zabwino ndikuopa (Allah); musathandizane pa machimo ndi pa chidani. Ndipo muopeni Allah. Ndithu Allah Ngwaukali pokhaulitsa.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (2) 章: 食卓章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる