۞ Allah sakonda kutulutsa mawu ofalitsa kuipa (kwa anthu) kupatula yekhayo wachitiridwa zoipa. Ndipo Allah Ngwakumva, Ngodziwa.[151]
[151] Indedi, Allah sakonda anthu ofalitsa zoipa za anzawo popanda choipa chilichonse chimene awachitira. Koma munthu amene ena amchitira choipa akumlola kutchula kuipa komwe ena amchitira pokamnenera kwa muweruzi kuti muweruziyo amuthandize pa amene amchitira zoipawo. Koma kulengeza kuipa kwa anthu ena nkosaloledwa m’chisilamu. Ndipo ndi uchimo waukulu.
Ndithudi amene sakhulupirira Allah ndi atumiki Ake, ndikumafuna kulekanitsa pakati pa Allah ndi atumiki Ake, ndikumanena kuti: “Ena tikuwakhulupirira, koma ena tikuwakana,” ndikumafunanso kukhonza njira yapakati pa zimenezo,[152]
[152] Aliyense mwa anthu yemwe Allah wamuvomereza kuti ndi mtumiki Wake, ndipo iwe nkukana kumkhulupilira, monga Ayuda mmene amamkanira mneneri Isa (Yesu), ndi Akhrisitu mmene amamkanira mneneri Muhammad (s.a.w), kutereko nkusakhulupilira Allah. Asilamu amavomereza aneneri onse owona amene adadza Muhammad (s.a.w) asadabadwe. Asilamu akuvomereza aneneri onse monga momwe Allah wafotokozera m’Qur’an. Ndipo savomereza omwe Allah sadawavomereze kuti ndi aneneri ake, monga Mirza Gulam Ahmad ndi Bahai. Oterewa ndi amene akunama kuti adapatsidwa uneneri pambuyo pa Mneneri Muhammad (s.a.w). Amene akukhulupilira amenewa ndiye kuti ngopandukira Allah. Tero tichenjere ndi udyerekezi wa Akadiani ndi Abahai ndi ena otere.
Anthu amene adapatsidwa buku (Ayuda) akukupempha (iwe Mtumiki) kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi, adampemphanso Mûsa zazikulu kuposa zimenezi pomwe adati: “Tiwonetse Allah poyera.” Choncho udawagwira moto wamphenzi chifukwa cha kuipitsa kwao (motowo udachotsa miyoyo yawo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Zitatero Allah adawapatsa moyo kachiwiri). Kenako iwo adapanga thole (mwana wang’ombe monga mulungu wawo) pambuyo powafikira chisonyezo choonekera. Koma tidawakhululukira zimenezo, ndipo tidampatsa Mûsa chisonyezo choonekera poyera.[153]
[153] Ayuda adauza mtumiki Muhammad (s.a.w) kuti sangakhulupirire pokhapokha amuone akukwera kumwamba popanda kugwilira chilichonse ndi kubwera pansi pano buku lili m’manja mwake mutalembedwa umboni wa Allah woti iye Muhammad ndi Mtumiki Wakedi. Ndipo Allah akuti makhalidwe otsutsana ndi aneneri siachilendo kwa Ayuda. Ndipo Musa atalephera kuchita zimenezo adamuda. Tero adapanga fano (lamwana wang’ombe ‘thole’) naliyesa mulungu wawo.
Ndipo tidatukula phiri la Al-Tur pamwamba pawo (Ayudawo) polandira pangano lawo; tidati kwa iwo: “Lowani pachipata (cha dziko ili la Sham) mutawerama.” Tidatinso kwa iwo: “Musalumphe malire pa nkhani ya Sabata.” Ndipo tidalandira kwa iwo pangano lokhwima.[154]
[154] (Ndime 154-156) Allah akupitiriza kufotokoza zoipa zawo. Ndipo zina mwa izo ndiizi: (a) Adakana kutsatira malamulo am’Taurat. Ndipo Allah adazula phiri naliimitsa pamwamba pa mitu yawo nawauza kuti: “Ngati simulola kulonjeza kuti mdzatsata zomwe zili m’Taurat, likusinjani phiri ili. (b) Adakana kulowera pachipata kudziko la Shamu (Kenani) monga momwe Allah adawalangizira. Ndipo adalowa monga momwe iwo amafunira. Shamu ndi dziko lomwe Allah adawapatsa kuti akalowemo ndi kukhazikika pambuyo posamuka ku Eguputo (Egypt). Koma iwo sadathokoze chisomochi potsata zomwe Allah adawauza. (c) Pambuyo polowa m’dzikolo adawauza kuti alemekeze tsiku la Sabata kuti likhale tsiku lamapemphero okhaokha. Lisakhale tsiku logwira ntchito. Koma iwo adachitachita ndale zawo mpaka lidasanduka tsiku logwira ntchito. (d) Ena mwa aneneri awo pamene adawaletsa iwo machitidwe amenewa mwaukali adawapha. (e) Mneneri Muhammad pamene adawafotokozera zizindikiro zomwe zinali m’mabuku mwawo zimene zimasonyeza utumiki wake sadamulabadire. Nanena kuti :“Mitima yathu yakutidwa. Siikumvetsa chilichonse chimene ukunena”. (f) Mneneri Isa (Yesu) pamene adawafotokozera za utumiki wake ndi kuwasonyeza zozizwitsa ndi zonse zomwe zidachitika m’kubadwa kwake, iwo adati Mariya adatenga pakati m’njira yachiwerewere pomwe iwo amadziwa kuti akungonama. (g) Adakonza chiwembu kuti aphe Isa (Yesu). Koma Allah adachiononga chiwembu chawocho pomuveka munthu wina nkhope ya Isa (Yesu) amene adali wamkulu wawo yemwe ankafunisitsa kupha Isa (Yesu). Tero adampachika mnzawoyo pamtanda. Pambuyo pake, akuluakulu aChiyuda adazindikira zonse zomwe zidachitikazi. Ndipo adangonyozera ngati kuti sichidachitike chilichonse chododometsa chifukwa choopa kuti anthu angawaukire. M’malomwake ankangodzidzudzula okha m’mtima mwawo.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
ئەنجامەکانی گەڕان:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".