وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا * - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان


وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (5) سوره‌تی: سورەتی النساء
وَلَا تُؤۡتُواْ ٱلسُّفَهَآءَ أَمۡوَٰلَكُمُ ٱلَّتِي جَعَلَ ٱللَّهُ لَكُمۡ قِيَٰمٗا وَٱرۡزُقُوهُمۡ فِيهَا وَٱكۡسُوهُمۡ وَقُولُواْ لَهُمۡ قَوۡلٗا مَّعۡرُوفٗا
Ozerezeka musawapatse chuma chanu chomwe Allah wachichita kukhala cholimbitsa matupi anu ndi moyo wanu. Koma adyetseni nacho ndikuwaveka nacho ndikuwauza mawu abwino (monga kuti: Mukadzakula ndikukhala olungama, tidzakupatsani chuma chanu).[108]
[108] Ayang’aniri a ana amasiye, monga momwe awauzira kuti asawachenjelere ana amasiye koma kuti awapatse chuma chawo mokwanira, apa akuwauzanso kuti apitirize kuyang’anira chuma cha ana amasiyewo. Asawapatse pomwe sali ozindikira zinthu, ali ofooka m’maganizo pomwe sakuzindikira kufunika kwa chuma kuopa kuti angasakaze chumacho. Tero asawapatse ngakhale misinkhu yawo ili yaikulu. Koma apitirize kuwasungira chumacho ndi kumawauza mawu abwino ponena kuti: “Mpaka pano ndikuona kuti mwanokha simungathe kuchiyendetsa bwino chuma chanu. Tero ndiloleni ndikusungirenibe mpaka nthawi yochepa kutsogoloku. Ndikadzaona kuti nzeru zakhazikika apo mpomwe ndidzakupatsani chumachi.”
تەفسیرە عەرەبیەکان:
 
وه‌رگێڕانی ماناكان ئایه‌تی: (5) سوره‌تی: سورەتی النساء
پێڕستی سوره‌ته‌كان ژمارەی پەڕە
 
وه‌رگێڕانی ماناكانی قورئانی پیرۆز - وەرگێڕاوی شیشوا - پێڕستی وه‌رگێڕاوه‌كان

وەرگێڕاوی ماناکانی قورئانی پیرۆز بۆ زمانی شیشیوا، وەرگێڕان: خالد إبراهيم بيتالا. چاپی ساڵی 2020ز.

داخستن