Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (5) Surah: Soerat An-nisa (de vrouwen)
وَلَا تُؤۡتُواْ ٱلسُّفَهَآءَ أَمۡوَٰلَكُمُ ٱلَّتِي جَعَلَ ٱللَّهُ لَكُمۡ قِيَٰمٗا وَٱرۡزُقُوهُمۡ فِيهَا وَٱكۡسُوهُمۡ وَقُولُواْ لَهُمۡ قَوۡلٗا مَّعۡرُوفٗا
Ozerezeka musawapatse chuma chanu chomwe Allah wachichita kukhala cholimbitsa matupi anu ndi moyo wanu. Koma adyetseni nacho ndikuwaveka nacho ndikuwauza mawu abwino (monga kuti: Mukadzakula ndikukhala olungama, tidzakupatsani chuma chanu).[108]
[108] Ayang’aniri a ana amasiye, monga momwe awauzira kuti asawachenjelere ana amasiye koma kuti awapatse chuma chawo mokwanira, apa akuwauzanso kuti apitirize kuyang’anira chuma cha ana amasiyewo. Asawapatse pomwe sali ozindikira zinthu, ali ofooka m’maganizo pomwe sakuzindikira kufunika kwa chuma kuopa kuti angasakaze chumacho. Tero asawapatse ngakhale misinkhu yawo ili yaikulu. Koma apitirize kuwasungira chumacho ndi kumawauza mawu abwino ponena kuti: “Mpaka pano ndikuona kuti mwanokha simungathe kuchiyendetsa bwino chuma chanu. Tero ndiloleni ndikusungirenibe mpaka nthawi yochepa kutsogoloku. Ndikadzaona kuti nzeru zakhazikika apo mpomwe ndidzakupatsani chumachi.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (5) Surah: Soerat An-nisa (de vrouwen)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit