Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Ar-Rahmaan   Aja (Korano eilutė):

Sūra Ar-Rahmaan

ٱلرَّحۡمَٰنُ
(Allah) Wachifundo chochuluka!
Tafsyrai arabų kalba:
عَلَّمَ ٱلۡقُرۡءَانَ
Waphunzitsa Qur’an.
Tafsyrai arabų kalba:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ
Adalenga munthu.
Tafsyrai arabų kalba:
عَلَّمَهُ ٱلۡبَيَانَ
Adamphunzitsa kuyankhula.
Tafsyrai arabų kalba:
ٱلشَّمۡسُ وَٱلۡقَمَرُ بِحُسۡبَانٖ
Dzuwa ndi mwezi zikuyenda mwachiwerengero.
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلنَّجۡمُ وَٱلشَّجَرُ يَسۡجُدَانِ
Zomera zopanda tsinde ndi mitengo, zikulambira (Allah pachilichonse chimene wafuna mwa izo).
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلسَّمَآءَ رَفَعَهَا وَوَضَعَ ٱلۡمِيزَانَ
Ndipo thambo adalitukula kumwamba ndipo adakhazikitsa sikelo (ya chilungamo).
Tafsyrai arabų kalba:
أَلَّا تَطۡغَوۡاْ فِي ٱلۡمِيزَانِ
Kuti musapyole malire ndi kuchita chinyengo poyesa.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَقِيمُواْ ٱلۡوَزۡنَ بِٱلۡقِسۡطِ وَلَا تُخۡسِرُواْ ٱلۡمِيزَانَ
Choncho yesani sikelo mwachilungamo ndipo musapungule muyeso.
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلۡأَرۡضَ وَضَعَهَا لِلۡأَنَامِ
Ndipo nthaka adaiyala (ndi kuikonza) kuti ikhale ya zolengedwa.
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهَا فَٰكِهَةٞ وَٱلنَّخۡلُ ذَاتُ ٱلۡأَكۡمَامِ
M’menemo muli zipatso ndi mitengo ya kanjedza yokhala ndi mapava (a zipatso).
Tafsyrai arabų kalba:
وَٱلۡحَبُّ ذُو ٱلۡعَصۡفِ وَٱلرَّيۡحَانُ
Ndi mbewu zamakoko (kuti chikhale chakudya cha inu ndi ziweto zanu), ndipo mulinso m’menemo mmera wafungo labwino.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ مِن صَلۡصَٰلٖ كَٱلۡفَخَّارِ
Adalenga munthu kuchokera ku dongo lolira monga ziwiya zadongo.
Tafsyrai arabų kalba:
وَخَلَقَ ٱلۡجَآنَّ مِن مَّارِجٖ مِّن نَّارٖ
Ndipo adalenga ziwanda kuchokera ku malawi a moto (wopanda utsi.)
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
رَبُّ ٱلۡمَشۡرِقَيۡنِ وَرَبُّ ٱلۡمَغۡرِبَيۡنِ
Mbuye wa kuvuma kuwiri ndiponso Mbuye wa kuzambwe kuwiri.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
مَرَجَ ٱلۡبَحۡرَيۡنِ يَلۡتَقِيَانِ
Adaika nyanja ziwiri zokumana (yamadzi amchere, ndi yamadzi ozizira).
Tafsyrai arabų kalba:
بَيۡنَهُمَا بَرۡزَخٞ لَّا يَبۡغِيَانِ
Pakati pake pali chitsekerezo, sizilowana;
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
يَخۡرُجُ مِنۡهُمَا ٱللُّؤۡلُؤُ وَٱلۡمَرۡجَانُ
M’menemo mumatuluka ngale zing’onozing’ono ndi ngale zikuluzikulu.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
وَلَهُ ٱلۡجَوَارِ ٱلۡمُنشَـَٔاتُ فِي ٱلۡبَحۡرِ كَٱلۡأَعۡلَٰمِ
Ndipo (Iye) ali nazo zombo (zimene zapangidwa ndi manja anu), zoyenda panyanja, zazikuluzikulu ngati mapiri.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
كُلُّ مَنۡ عَلَيۡهَا فَانٖ
Zonse zili pamenepo (pa dziko) nzakutha.
Tafsyrai arabų kalba:
وَيَبۡقَىٰ وَجۡهُ رَبِّكَ ذُو ٱلۡجَلَٰلِ وَٱلۡإِكۡرَامِ
Ndipo idzatsala nkhope ya Mbuye wako yaulemelero ndi mtendere.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
يَسۡـَٔلُهُۥ مَن فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ كُلَّ يَوۡمٍ هُوَ فِي شَأۡنٖ
(Onse) akumwamba ndi pansi akupempha Iye (zofuna zawo)! Tsiku lililonse Iye ali ndi zochita (monga kupatsa uyu ulemelero, ndi kutsitsa uyu).
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa zamitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
سَنَفۡرُغُ لَكُمۡ أَيُّهَ ٱلثَّقَلَانِ
Posachedwapa (patsiku la chiweruziro), tidzaikapo mtima pa chiwerengero chanu (cha zochita zanu) inu anthu ndi ziwanda.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
يَٰمَعۡشَرَ ٱلۡجِنِّ وَٱلۡإِنسِ إِنِ ٱسۡتَطَعۡتُمۡ أَن تَنفُذُواْ مِنۡ أَقۡطَارِ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ فَٱنفُذُواْۚ لَا تَنفُذُونَ إِلَّا بِسُلۡطَٰنٖ
E inu ziwanda ndi anthu! Ngati mungathe kutuluka m’mphepete mwa thambo ndi nthaka (pothawa Allah), tulukani! Simungathe kutuluka pokhapokha ndi mphamvu. (Koma inu simungathe kutero.)
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
يُرۡسَلُ عَلَيۡكُمَا شُوَاظٞ مِّن نَّارٖ وَنُحَاسٞ فَلَا تَنتَصِرَانِ
Mudzathiridwa malawi a moto ndi mtovu wa moto wosungunuka ndipo simungathe kupulumuka (ku chilango chimenechi).
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فَإِذَا ٱنشَقَّتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ وَرۡدَةٗ كَٱلدِّهَانِ
(Kumbuka) pamene thambo lidzang’ambika ndi kukhala lofiira ngati chikopa chofiira (kapena ngati mafuta oyaka).
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فَيَوۡمَئِذٖ لَّا يُسۡـَٔلُ عَن ذَنۢبِهِۦٓ إِنسٞ وَلَا جَآنّٞ
Ndipo patsikulo munthu ndi chiwanda, sadzafunsidwa (aliyense) za tchimo lake.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
يُعۡرَفُ ٱلۡمُجۡرِمُونَ بِسِيمَٰهُمۡ فَيُؤۡخَذُ بِٱلنَّوَٰصِي وَٱلۡأَقۡدَامِ
Adzadziwika oipa (pakati pa anthu ndi ziwanda) ndi zizindikiro zawo (zowazindikiritsa). Ndipo adzagwidwa maliombo awo ndi mapazi awo (ndi kuponyedwa ku Jahena).
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
((Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
هَٰذِهِۦ جَهَنَّمُ ٱلَّتِي يُكَذِّبُ بِهَا ٱلۡمُجۡرِمُونَ
(Kudzanenedwa mowadandaulitsa): Iyi ndi Jahannam yomwe adali kuitsutsa oipa.
Tafsyrai arabų kalba:
يَطُوفُونَ بَيۡنَهَا وَبَيۡنَ حَمِيمٍ ءَانٖ
Adzakhala akuyenda pakati pa moto ndi pakati pa madzi owira, otentha kwambiri.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
وَلِمَنۡ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِۦ جَنَّتَانِ
Koma amene waopa kuti adzaimitsidwa kwa Mbuye wake (pa nthawi ya chiweruziro), adzalandira minda iwiri (yaikulu yamtendere).
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
ذَوَاتَآ أَفۡنَانٖ
(Minda ya mitengo) yanthambi zofwanthamuka.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهِمَا عَيۡنَانِ تَجۡرِيَانِ
M’menemo muli akasupe awiri, omwe akuyenda.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهِمَا مِن كُلِّ فَٰكِهَةٖ زَوۡجَانِ
M’menemo muli zipatso za mtundu uliwonse, mitundu iwiri iwiri.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
مُتَّكِـِٔينَ عَلَىٰ فُرُشِۭ بَطَآئِنُهَا مِنۡ إِسۡتَبۡرَقٖۚ وَجَنَى ٱلۡجَنَّتَيۡنِ دَانٖ
Atatsamira pa zoyala, mkati mwake mosokelera veleveti wochindikala; ndipo zipatso zam’minda iwiriyi nzapafupi (kuzithyola).
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهِنَّ قَٰصِرَٰتُ ٱلطَّرۡفِ لَمۡ يَطۡمِثۡهُنَّ إِنسٞ قَبۡلَهُمۡ وَلَا جَآنّٞ
M’mindamo muli akazi oyang’ana amuna awo okha basi, (mawuthu) omwe sadakhalepo malo amodzi ndi munthu kapena chiwanda asadakumane ndi iwo.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
كَأَنَّهُنَّ ٱلۡيَاقُوتُ وَٱلۡمَرۡجَانُ
Kukongola kwake (akaziwo) kuli ngati ngale zikuluzikulu ndi zing’onozing’ono.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
هَلۡ جَزَآءُ ٱلۡإِحۡسَٰنِ إِلَّا ٱلۡإِحۡسَٰنُ
Malipiro a ntchito zabwino ndikulandira zabwino basi.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
وَمِن دُونِهِمَا جَنَّتَانِ
Ndipo kuonjezera paminda iwiri (ija) palinso minda ina iwiri.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
مُدۡهَآمَّتَانِ
Yobiriwira, kwambiri.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهِمَا عَيۡنَانِ نَضَّاخَتَانِ
M’menemo muli akasupe awiri ofwamphuka madzi mwaphamvu.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهِمَا فَٰكِهَةٞ وَنَخۡلٞ وَرُمَّانٞ
Mmenemo muli zipatso, mitengo yakanjedza ndi yamikangaza.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
فِيهِنَّ خَيۡرَٰتٌ حِسَانٞ
M’menemo muli akazi amakhalidwe abwino, owala nkhope.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
حُورٞ مَّقۡصُورَٰتٞ فِي ٱلۡخِيَامِ
Okongola maso, achikhalire m’mahema (m’matenti) awo.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
لَمۡ يَطۡمِثۡهُنَّ إِنسٞ قَبۡلَهُمۡ وَلَا جَآنّٞ
Amene sadakhalepo malo amodzi ndi munthu kapena chiwanda asadakumane ndi iwo.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
مُتَّكِـِٔينَ عَلَىٰ رَفۡرَفٍ خُضۡرٖ وَعَبۡقَرِيٍّ حِسَانٖ
Uku atatsamira misamiro yawofuwofu yokutidwa ndi zobiriwira; ndi zoyala zokongola, zakapangidwe kabwino.
Tafsyrai arabų kalba:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
Tafsyrai arabų kalba:
تَبَٰرَكَ ٱسۡمُ رَبِّكَ ذِي ٱلۡجَلَٰلِ وَٱلۡإِكۡرَامِ
Latukuka ndi kudalitsika dzina la Mbuye wako Mwini ulemelero ndi ufulu.
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Ar-Rahmaan
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas - Vertimų turinys

Kilniojo Korano reikšmių vertimas į čevų k., išvertė Khaled Ibrahim Betala. 2020 m. leidimas.

Uždaryti