पवित्र कुरअानको अर्थको अनुवाद - चेवा अनुवाद * - अनुवादहरूको सूची


अर्थको अनुवाद सूरः: सूरतुर्रहमान   श्लोक:

सूरतुर्रहमान

ٱلرَّحۡمَٰنُ
(Allah) Wachifundo chochuluka!
अरबी व्याख्याहरू:
عَلَّمَ ٱلۡقُرۡءَانَ
Waphunzitsa Qur’an.
अरबी व्याख्याहरू:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ
Adalenga munthu.
अरबी व्याख्याहरू:
عَلَّمَهُ ٱلۡبَيَانَ
Adamphunzitsa kuyankhula.
अरबी व्याख्याहरू:
ٱلشَّمۡسُ وَٱلۡقَمَرُ بِحُسۡبَانٖ
Dzuwa ndi mwezi zikuyenda mwachiwerengero.
अरबी व्याख्याहरू:
وَٱلنَّجۡمُ وَٱلشَّجَرُ يَسۡجُدَانِ
Zomera zopanda tsinde ndi mitengo, zikulambira (Allah pachilichonse chimene wafuna mwa izo).
अरबी व्याख्याहरू:
وَٱلسَّمَآءَ رَفَعَهَا وَوَضَعَ ٱلۡمِيزَانَ
Ndipo thambo adalitukula kumwamba ndipo adakhazikitsa sikelo (ya chilungamo).
अरबी व्याख्याहरू:
أَلَّا تَطۡغَوۡاْ فِي ٱلۡمِيزَانِ
Kuti musapyole malire ndi kuchita chinyengo poyesa.
अरबी व्याख्याहरू:
وَأَقِيمُواْ ٱلۡوَزۡنَ بِٱلۡقِسۡطِ وَلَا تُخۡسِرُواْ ٱلۡمِيزَانَ
Choncho yesani sikelo mwachilungamo ndipo musapungule muyeso.
अरबी व्याख्याहरू:
وَٱلۡأَرۡضَ وَضَعَهَا لِلۡأَنَامِ
Ndipo nthaka adaiyala (ndi kuikonza) kuti ikhale ya zolengedwa.
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهَا فَٰكِهَةٞ وَٱلنَّخۡلُ ذَاتُ ٱلۡأَكۡمَامِ
M’menemo muli zipatso ndi mitengo ya kanjedza yokhala ndi mapava (a zipatso).
अरबी व्याख्याहरू:
وَٱلۡحَبُّ ذُو ٱلۡعَصۡفِ وَٱلرَّيۡحَانُ
Ndi mbewu zamakoko (kuti chikhale chakudya cha inu ndi ziweto zanu), ndipo mulinso m’menemo mmera wafungo labwino.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ مِن صَلۡصَٰلٖ كَٱلۡفَخَّارِ
Adalenga munthu kuchokera ku dongo lolira monga ziwiya zadongo.
अरबी व्याख्याहरू:
وَخَلَقَ ٱلۡجَآنَّ مِن مَّارِجٖ مِّن نَّارٖ
Ndipo adalenga ziwanda kuchokera ku malawi a moto (wopanda utsi.)
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
رَبُّ ٱلۡمَشۡرِقَيۡنِ وَرَبُّ ٱلۡمَغۡرِبَيۡنِ
Mbuye wa kuvuma kuwiri ndiponso Mbuye wa kuzambwe kuwiri.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
مَرَجَ ٱلۡبَحۡرَيۡنِ يَلۡتَقِيَانِ
Adaika nyanja ziwiri zokumana (yamadzi amchere, ndi yamadzi ozizira).
अरबी व्याख्याहरू:
بَيۡنَهُمَا بَرۡزَخٞ لَّا يَبۡغِيَانِ
Pakati pake pali chitsekerezo, sizilowana;
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
يَخۡرُجُ مِنۡهُمَا ٱللُّؤۡلُؤُ وَٱلۡمَرۡجَانُ
M’menemo mumatuluka ngale zing’onozing’ono ndi ngale zikuluzikulu.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
وَلَهُ ٱلۡجَوَارِ ٱلۡمُنشَـَٔاتُ فِي ٱلۡبَحۡرِ كَٱلۡأَعۡلَٰمِ
Ndipo (Iye) ali nazo zombo (zimene zapangidwa ndi manja anu), zoyenda panyanja, zazikuluzikulu ngati mapiri.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
كُلُّ مَنۡ عَلَيۡهَا فَانٖ
Zonse zili pamenepo (pa dziko) nzakutha.
अरबी व्याख्याहरू:
وَيَبۡقَىٰ وَجۡهُ رَبِّكَ ذُو ٱلۡجَلَٰلِ وَٱلۡإِكۡرَامِ
Ndipo idzatsala nkhope ya Mbuye wako yaulemelero ndi mtendere.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
يَسۡـَٔلُهُۥ مَن فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۚ كُلَّ يَوۡمٍ هُوَ فِي شَأۡنٖ
(Onse) akumwamba ndi pansi akupempha Iye (zofuna zawo)! Tsiku lililonse Iye ali ndi zochita (monga kupatsa uyu ulemelero, ndi kutsitsa uyu).
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa zamitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
سَنَفۡرُغُ لَكُمۡ أَيُّهَ ٱلثَّقَلَانِ
Posachedwapa (patsiku la chiweruziro), tidzaikapo mtima pa chiwerengero chanu (cha zochita zanu) inu anthu ndi ziwanda.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
يَٰمَعۡشَرَ ٱلۡجِنِّ وَٱلۡإِنسِ إِنِ ٱسۡتَطَعۡتُمۡ أَن تَنفُذُواْ مِنۡ أَقۡطَارِ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ فَٱنفُذُواْۚ لَا تَنفُذُونَ إِلَّا بِسُلۡطَٰنٖ
E inu ziwanda ndi anthu! Ngati mungathe kutuluka m’mphepete mwa thambo ndi nthaka (pothawa Allah), tulukani! Simungathe kutuluka pokhapokha ndi mphamvu. (Koma inu simungathe kutero.)
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
يُرۡسَلُ عَلَيۡكُمَا شُوَاظٞ مِّن نَّارٖ وَنُحَاسٞ فَلَا تَنتَصِرَانِ
Mudzathiridwa malawi a moto ndi mtovu wa moto wosungunuka ndipo simungathe kupulumuka (ku chilango chimenechi).
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فَإِذَا ٱنشَقَّتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ وَرۡدَةٗ كَٱلدِّهَانِ
(Kumbuka) pamene thambo lidzang’ambika ndi kukhala lofiira ngati chikopa chofiira (kapena ngati mafuta oyaka).
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فَيَوۡمَئِذٖ لَّا يُسۡـَٔلُ عَن ذَنۢبِهِۦٓ إِنسٞ وَلَا جَآنّٞ
Ndipo patsikulo munthu ndi chiwanda, sadzafunsidwa (aliyense) za tchimo lake.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
يُعۡرَفُ ٱلۡمُجۡرِمُونَ بِسِيمَٰهُمۡ فَيُؤۡخَذُ بِٱلنَّوَٰصِي وَٱلۡأَقۡدَامِ
Adzadziwika oipa (pakati pa anthu ndi ziwanda) ndi zizindikiro zawo (zowazindikiritsa). Ndipo adzagwidwa maliombo awo ndi mapazi awo (ndi kuponyedwa ku Jahena).
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
((Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
هَٰذِهِۦ جَهَنَّمُ ٱلَّتِي يُكَذِّبُ بِهَا ٱلۡمُجۡرِمُونَ
(Kudzanenedwa mowadandaulitsa): Iyi ndi Jahannam yomwe adali kuitsutsa oipa.
अरबी व्याख्याहरू:
يَطُوفُونَ بَيۡنَهَا وَبَيۡنَ حَمِيمٍ ءَانٖ
Adzakhala akuyenda pakati pa moto ndi pakati pa madzi owira, otentha kwambiri.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
وَلِمَنۡ خَافَ مَقَامَ رَبِّهِۦ جَنَّتَانِ
Koma amene waopa kuti adzaimitsidwa kwa Mbuye wake (pa nthawi ya chiweruziro), adzalandira minda iwiri (yaikulu yamtendere).
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
ذَوَاتَآ أَفۡنَانٖ
(Minda ya mitengo) yanthambi zofwanthamuka.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهِمَا عَيۡنَانِ تَجۡرِيَانِ
M’menemo muli akasupe awiri, omwe akuyenda.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهِمَا مِن كُلِّ فَٰكِهَةٖ زَوۡجَانِ
M’menemo muli zipatso za mtundu uliwonse, mitundu iwiri iwiri.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
مُتَّكِـِٔينَ عَلَىٰ فُرُشِۭ بَطَآئِنُهَا مِنۡ إِسۡتَبۡرَقٖۚ وَجَنَى ٱلۡجَنَّتَيۡنِ دَانٖ
Atatsamira pa zoyala, mkati mwake mosokelera veleveti wochindikala; ndipo zipatso zam’minda iwiriyi nzapafupi (kuzithyola).
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهِنَّ قَٰصِرَٰتُ ٱلطَّرۡفِ لَمۡ يَطۡمِثۡهُنَّ إِنسٞ قَبۡلَهُمۡ وَلَا جَآنّٞ
M’mindamo muli akazi oyang’ana amuna awo okha basi, (mawuthu) omwe sadakhalepo malo amodzi ndi munthu kapena chiwanda asadakumane ndi iwo.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
كَأَنَّهُنَّ ٱلۡيَاقُوتُ وَٱلۡمَرۡجَانُ
Kukongola kwake (akaziwo) kuli ngati ngale zikuluzikulu ndi zing’onozing’ono.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
هَلۡ جَزَآءُ ٱلۡإِحۡسَٰنِ إِلَّا ٱلۡإِحۡسَٰنُ
Malipiro a ntchito zabwino ndikulandira zabwino basi.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
وَمِن دُونِهِمَا جَنَّتَانِ
Ndipo kuonjezera paminda iwiri (ija) palinso minda ina iwiri.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
مُدۡهَآمَّتَانِ
Yobiriwira, kwambiri.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهِمَا عَيۡنَانِ نَضَّاخَتَانِ
M’menemo muli akasupe awiri ofwamphuka madzi mwaphamvu.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهِمَا فَٰكِهَةٞ وَنَخۡلٞ وَرُمَّانٞ
Mmenemo muli zipatso, mitengo yakanjedza ndi yamikangaza.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
فِيهِنَّ خَيۡرَٰتٌ حِسَانٞ
M’menemo muli akazi amakhalidwe abwino, owala nkhope.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
حُورٞ مَّقۡصُورَٰتٞ فِي ٱلۡخِيَامِ
Okongola maso, achikhalire m’mahema (m’matenti) awo.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
لَمۡ يَطۡمِثۡهُنَّ إِنسٞ قَبۡلَهُمۡ وَلَا جَآنّٞ
Amene sadakhalepo malo amodzi ndi munthu kapena chiwanda asadakumane ndi iwo.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
مُتَّكِـِٔينَ عَلَىٰ رَفۡرَفٍ خُضۡرٖ وَعَبۡقَرِيٍّ حِسَانٖ
Uku atatsamira misamiro yawofuwofu yokutidwa ndi zobiriwira; ndi zoyala zokongola, zakapangidwe kabwino.
अरबी व्याख्याहरू:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكُمَا تُكَذِّبَانِ
(Inu zolengedwa za mitundu iwiri, anthu ndi ziwanda), kodi ndi mtendere uti wa Mbuye wanu umene mukuukana (kuti si Wake?)
अरबी व्याख्याहरू:
تَبَٰرَكَ ٱسۡمُ رَبِّكَ ذِي ٱلۡجَلَٰلِ وَٱلۡإِكۡرَامِ
Latukuka ndi kudalitsika dzina la Mbuye wako Mwini ulemelero ndi ufulu.
अरबी व्याख्याहरू:
 
अर्थको अनुवाद सूरः: सूरतुर्रहमान
अध्यायहरूको (सूरःहरूको) सूची رقم الصفحة
 
पवित्र कुरअानको अर्थको अनुवाद - चेवा अनुवाद - अनुवादहरूको सूची

पवित्र कुर्आनको अर्थको चेवा भाषामा अनुवाद, अनुवादक : खालिद इब्राहीम बेताला, प्रकाशन : २०२० ।

बन्द गर्नुस्