Check out the new design

Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: Al-An’am   Aja (Korano eilutė):
ذَٰلِكُمُ ٱللَّهُ رَبُّكُمۡۖ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۖ خَٰلِقُ كُلِّ شَيۡءٖ فَٱعۡبُدُوهُۚ وَهُوَ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ وَكِيلٞ
Ameneyu ndi Allah, Mbuye wanu; palibe wina woti nkumpembedza mwa choonadi koma Iye. Mlengi wa chinthu chilichonse. Choncho, mpembedzeni. Iye ndi Muyang’aniri wa chinthu chilichonse.
Tafsyrai arabų kalba:
لَّا تُدۡرِكُهُ ٱلۡأَبۡصَٰرُ وَهُوَ يُدۡرِكُ ٱلۡأَبۡصَٰرَۖ وَهُوَ ٱللَّطِيفُ ٱلۡخَبِيرُ
Maso samufika (kuti nkumuona); koma Iye amawafika maso (amawaona pamodzi ndi eni masowo). Iye Ngodziwa zobisika kwambiri, Ngodziwa zoonekera.
Tafsyrai arabų kalba:
قَدۡ جَآءَكُم بَصَآئِرُ مِن رَّبِّكُمۡۖ فَمَنۡ أَبۡصَرَ فَلِنَفۡسِهِۦۖ وَمَنۡ عَمِيَ فَعَلَيۡهَاۚ وَمَآ أَنَا۠ عَلَيۡكُم بِحَفِيظٖ
(Nena iwe Mtumiki): “Ndithu umboni otsimikizika wakufikani kuchokera kwa Mbuye wanu, choncho amene atsekule maso ake nkuyang’ana ndiye kuti (zotsatira zake zabwino) zili pa iye mwini. Ndipo amene atseke maso ake zili pa iye mwini (zotsatira zake zoipa). Ndipo ine sindili muyang’anili wanu.”
Tafsyrai arabų kalba:
وَكَذَٰلِكَ نُصَرِّفُ ٱلۡأٓيَٰتِ وَلِيَقُولُواْ دَرَسۡتَ وَلِنُبَيِّنَهُۥ لِقَوۡمٖ يَعۡلَمُونَ
Motero tikulongosola mwatsatanetsatane zizindikiro, (kuti azindikire). Ndikuti anene: “Wachita kuphunzira (izi, si Allah amene wakuuza.” Ndipo tazibwerezabwereza chonchi) kuti tilongosole ndi kufotokoza momveka kwa anthu odziwa.
Tafsyrai arabų kalba:
ٱتَّبِعۡ مَآ أُوحِيَ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَۖ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا هُوَۖ وَأَعۡرِضۡ عَنِ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Tsata zimene zavumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako. Palibe wopembedzedwa mwa choonadi koma Iye. Ndipo apewe opembedza mafano.
Tafsyrai arabų kalba:
وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَآ أَشۡرَكُواْۗ وَمَا جَعَلۡنَٰكَ عَلَيۡهِمۡ حَفِيظٗاۖ وَمَآ أَنتَ عَلَيۡهِم بِوَكِيلٖ
Ndipo Allah akadafuna sakadamphatikiza (ndi mafano), ndipo sitidakuike pa iwo kukhala muyang’aniri wawo. Ndipo iwe suli muyimiliri wawo.
Tafsyrai arabų kalba:
وَلَا تَسُبُّواْ ٱلَّذِينَ يَدۡعُونَ مِن دُونِ ٱللَّهِ فَيَسُبُّواْ ٱللَّهَ عَدۡوَۢا بِغَيۡرِ عِلۡمٖۗ كَذَٰلِكَ زَيَّنَّا لِكُلِّ أُمَّةٍ عَمَلَهُمۡ ثُمَّ إِلَىٰ رَبِّهِم مَّرۡجِعُهُمۡ فَيُنَبِّئُهُم بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo usawatukwane amene akupembedza (mafano) kusiya Allah, kuopera kuti angamtukwane Allah mwamwano popanda kuzindikira. Motero taukometsera m’badwo ulionse ntchito zake. Potsiriza adzabwerera kwa Mbuye wawo, choncho, Iye adzawauza zonse zomwe adali kuchita.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَقۡسَمُواْ بِٱللَّهِ جَهۡدَ أَيۡمَٰنِهِمۡ لَئِن جَآءَتۡهُمۡ ءَايَةٞ لَّيُؤۡمِنُنَّ بِهَاۚ قُلۡ إِنَّمَا ٱلۡأٓيَٰتُ عِندَ ٱللَّهِۖ وَمَا يُشۡعِرُكُمۡ أَنَّهَآ إِذَا جَآءَتۡ لَا يُؤۡمِنُونَ
Ndipo (akafiri) adalumbira Allah ndi malumbiro awo amphamvu kuti ngati chitawadzera chozizwitsa ndithu adzachikhulupirira. Nena: “Zozizwitsa zili kwa Allah (sizili mmanja mwanga). Kodi nchinthu chanji chingakudziwitseni (inu Asilamu) kuti (ngakhale) chitaza (chozizwitsacho) iwo sangakhulupirire?”
Tafsyrai arabų kalba:
وَنُقَلِّبُ أَفۡـِٔدَتَهُمۡ وَأَبۡصَٰرَهُمۡ كَمَا لَمۡ يُؤۡمِنُواْ بِهِۦٓ أَوَّلَ مَرَّةٖ وَنَذَرُهُمۡ فِي طُغۡيَٰنِهِمۡ يَعۡمَهُونَ
Ndipo titembenuza mitima yawo ndi maso awo (kotero kuti sangathe kuchikhulupirira ngakhale atachiona chozizwitsacho) monga momwe sadaikhulupirire (Qur’an) poyamba ndipo tiwasiya akuyumbayumba m’machimo awo.
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: Al-An’am
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Vertimas į čevų k. - Khalid Ibrahim Bitala - Vertimų turinys

Išvertė Khalid Ibrahim Bitala.

Uždaryti