Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas * - Vertimų turinys


Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Al-Džinn   Aja (Korano eilutė):

Sūra Al-Džinn

قُلۡ أُوحِيَ إِلَيَّ أَنَّهُ ٱسۡتَمَعَ نَفَرٞ مِّنَ ٱلۡجِنِّ فَقَالُوٓاْ إِنَّا سَمِعۡنَا قُرۡءَانًا عَجَبٗا
Nena (iwe Mtumiki (s.a.w), kwa anthu ako): “Kwavumbulutsidwa kwa ine kuti gulu la ziwanda lidamvetsera (kuwerenga kwanga kwa Qur’an) ndipo lidanena (kumtundu wawo): ndithu tamvetsera Qur’an yodabwitsa (ikuwerengedwa).
Tafsyrai arabų kalba:
يَهۡدِيٓ إِلَى ٱلرُّشۡدِ فَـَٔامَنَّا بِهِۦۖ وَلَن نُّشۡرِكَ بِرَبِّنَآ أَحَدٗا
Ikuitanira kuchilungamo, ndipo taikhulupirira. Ndipo sitimphatikiza aliyense ndi Mbuye wathu, (pa mapemphero).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّهُۥ تَعَٰلَىٰ جَدُّ رَبِّنَا مَا ٱتَّخَذَ صَٰحِبَةٗ وَلَا وَلَدٗا
Ndipo ndithu ukulu ndi ulemelero wa Mbuye wathu watukuka; sadadzipangire mkazi kapena mwana.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّهُۥ كَانَ يَقُولُ سَفِيهُنَا عَلَى ٱللَّهِ شَطَطٗا
Ndipo ndithu mbuli za mwa ife zakhala zikunenera Allah mawu abodza (okhala kutali ndi choonadi).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا ظَنَنَّآ أَن لَّن تَقُولَ ٱلۡإِنسُ وَٱلۡجِنُّ عَلَى ٱللَّهِ كَذِبٗا
Ndipo ndithu ife tinkaganiza kuti anthu ndi ziwanda sangamnenere Allah zabodza (zosayenera ulemelero Wake).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّهُۥ كَانَ رِجَالٞ مِّنَ ٱلۡإِنسِ يَعُوذُونَ بِرِجَالٖ مِّنَ ٱلۡجِنِّ فَزَادُوهُمۡ رَهَقٗا
Ndipo ndithu padali amuna a mu wanthu amapempha chitetezo kwa amuna amziwanda, ndipo adawaonjezera (amuna amziwanda) kupitiriza machimo (awo, kupulikira ndi kuchenjelera anthu).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّهُمۡ ظَنُّواْ كَمَا ظَنَنتُمۡ أَن لَّن يَبۡعَثَ ٱللَّهُ أَحَدٗا
Ndipo ndithu iwo amaganiza monga momwe mumaganizira inu kuti Allah sadzaukitsa aliyense.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا لَمَسۡنَا ٱلسَّمَآءَ فَوَجَدۡنَٰهَا مُلِئَتۡ حَرَسٗا شَدِيدٗا وَشُهُبٗا
Ndithu ife tidafuna kukafika kumwamba; tidakupeza kutadzala alonda (angelo) amphamvu ndi zenje za moto.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا كُنَّا نَقۡعُدُ مِنۡهَا مَقَٰعِدَ لِلسَّمۡعِۖ فَمَن يَسۡتَمِعِ ٱلۡأٓنَ يَجِدۡ لَهُۥ شِهَابٗا رَّصَدٗا
Ndithu ife tidali kukhala m’menemo (kale) mokhala momvetsera; (mobera nkhani zakumwamba). Koma amene afune kumvetsera tsopano apeza chenje cha moto chikudikilira (kuti chimgwere iye ndi kumuononga).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا لَا نَدۡرِيٓ أَشَرٌّ أُرِيدَ بِمَن فِي ٱلۡأَرۡضِ أَمۡ أَرَادَ بِهِمۡ رَبُّهُمۡ رَشَدٗا
Ndithu ife sitikudziwa chilango chimene akuwafunira a m’dziko (polondera kumwamba, kuletsa kumvetsera nkhani zakumeneko); kapena Mbuye wawo akuwafunira zabwino ndi chilungamo (pa zimenezo)!
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا مِنَّا ٱلصَّٰلِحُونَ وَمِنَّا دُونَ ذَٰلِكَۖ كُنَّا طَرَآئِقَ قِدَدٗا
Ndithu ena mwa ife ndi abwino koma ena sali choncho. Tili njira zosiyanasiyana.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا ظَنَنَّآ أَن لَّن نُّعۡجِزَ ٱللَّهَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَن نُّعۡجِزَهُۥ هَرَبٗا
Ndithu ife tidadziwa kuti Allah sitingathe kumlepheretsa (lamulo Lake pa ife paliponse tingakhale) pa dziko lapansi, ndipo sitingamlepheretsenso pomzemba ndi kuthawira (kumwamba).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا لَمَّا سَمِعۡنَا ٱلۡهُدَىٰٓ ءَامَنَّا بِهِۦۖ فَمَن يُؤۡمِنۢ بِرَبِّهِۦ فَلَا يَخَافُ بَخۡسٗا وَلَا رَهَقٗا
Ndipo ife pamene tachimva chiongoko (Qur’an) tachikhulupirira ndipo amene ati akhulupirire mwa Mbuye wake saopa kumchepetsera (chabwino kapena kumuonjezera machimo ake).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّا مِنَّا ٱلۡمُسۡلِمُونَ وَمِنَّا ٱلۡقَٰسِطُونَۖ فَمَنۡ أَسۡلَمَ فَأُوْلَٰٓئِكَ تَحَرَّوۡاْ رَشَدٗا
Ndithu mwa ife alipo Asilamu ndiponso mwa ife alipo opatuka (mu njira ya chilungamo); amene walowa m’Chisilamu, iwowo ndi amene alunjika njira ya choonadi.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَمَّا ٱلۡقَٰسِطُونَ فَكَانُواْ لِجَهَنَّمَ حَطَبٗا
Koma opatuka (kunjira ya chilungamo) adzakhala nkhuni za Jahannam.”
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَلَّوِ ٱسۡتَقَٰمُواْ عَلَى ٱلطَّرِيقَةِ لَأَسۡقَيۡنَٰهُم مَّآءً غَدَقٗا
Ndithu (anthu ndi ziwanda) akadalungama panjira ya chilungamo tikadawamwetsa madzi ambiri (okwanira nyengo zonse).
Tafsyrai arabų kalba:
لِّنَفۡتِنَهُمۡ فِيهِۚ وَمَن يُعۡرِضۡ عَن ذِكۡرِ رَبِّهِۦ يَسۡلُكۡهُ عَذَابٗا صَعَدٗا
Kuti tiwayese ndi zimenezo (mmene angamyamikire Allah pa mtendere Wake pa iwo). Koma amene anyozera kupembedza Mbuye wake, amlowetsa ku chilango chovuta (chimene sangathe kupirira nacho).
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّ ٱلۡمَسَٰجِدَ لِلَّهِ فَلَا تَدۡعُواْ مَعَ ٱللَّهِ أَحَدٗا
Ndithu misikiti ndi ya Allah yekha! Choncho, musapembedze aliyense pamodzi ndi Allah.
Tafsyrai arabų kalba:
وَأَنَّهُۥ لَمَّا قَامَ عَبۡدُ ٱللَّهِ يَدۡعُوهُ كَادُواْ يَكُونُونَ عَلَيۡهِ لِبَدٗا
Ndipo ndithu pamene adaima kapolo wa Allah (Muhammad{s.a.w}, pa Swala yake) uku akumpembedza (Allah), ziwanda zidatsala pang’ono kumgwera (chifukwa cha kuchuluka kwawo ndi kumzinga podabwa ndi zimene adaziona ndi kuzimva).
Tafsyrai arabų kalba:
قُلۡ إِنَّمَآ أَدۡعُواْ رَبِّي وَلَآ أُشۡرِكُ بِهِۦٓ أَحَدٗا
Nena: “Ndikumpembedza Mbuye wanga M’modzi (Yekha) ndipo sindingamphatikize ndi aliyense (m’mapemphero Ake).”
Tafsyrai arabų kalba:
قُلۡ إِنِّي لَآ أَمۡلِكُ لَكُمۡ ضَرّٗا وَلَا رَشَدٗا
Nena: “Ine ndilibe udindo wokupatsani mavuto kapena chilungamo (ndi zabwino).”
Tafsyrai arabų kalba:
قُلۡ إِنِّي لَن يُجِيرَنِي مِنَ ٱللَّهِ أَحَدٞ وَلَنۡ أَجِدَ مِن دُونِهِۦ مُلۡتَحَدًا
Nena: “Ine palibe anganditeteze ku chilango cha Allah (ngati nditamnyoza) sindingapeze malo (othawira kuchilango Chake) kupatula kwa Iye.”
Tafsyrai arabų kalba:
إِلَّا بَلَٰغٗا مِّنَ ٱللَّهِ وَرِسَٰلَٰتِهِۦۚ وَمَن يَعۡصِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَإِنَّ لَهُۥ نَارَ جَهَنَّمَ خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدًا
“Koma (mphamvu imene ndili nayo) ndikufikitsa uthenga wa Allah umene adanditumizira; ndithu amene anyoza Allah ndi Mtumiki Wake (ndi kupatuka pa chipembedzo cha (Allah) ndithu moto wa Jahannam ndi wake, akakhala m’menemo muyaya.”
Tafsyrai arabų kalba:
حَتَّىٰٓ إِذَا رَأَوۡاْ مَا يُوعَدُونَ فَسَيَعۡلَمُونَ مَنۡ أَضۡعَفُ نَاصِرٗا وَأَقَلُّ عَدَدٗا
Mpaka pomwe adzaziona zimene alonjezedwa ndipamene adzadziwa (kuti) kodi ndani mwini mthandizi wofooka ndiponso wochepekedwa mchiwerengero (cha omtsatira, iwo kapena Asilamu).”
Tafsyrai arabų kalba:
قُلۡ إِنۡ أَدۡرِيٓ أَقَرِيبٞ مَّا تُوعَدُونَ أَمۡ يَجۡعَلُ لَهُۥ رَبِّيٓ أَمَدًا
Nena (kuti): “Sindikudziwa ngati zomwe mukulonjezedwa (za chilango) zili pafupi, kapena Mbuye wanga azitalikitsa.”
Tafsyrai arabų kalba:
عَٰلِمُ ٱلۡغَيۡبِ فَلَا يُظۡهِرُ عَلَىٰ غَيۡبِهِۦٓ أَحَدًا
“(Iye) ndi wodziwa zobisika; sazionetsa zobisika Zake kwa aliyense (mzolengedwa Zake),”
Tafsyrai arabų kalba:
إِلَّا مَنِ ٱرۡتَضَىٰ مِن رَّسُولٖ فَإِنَّهُۥ يَسۡلُكُ مِنۢ بَيۡنِ يَدَيۡهِ وَمِنۡ خَلۡفِهِۦ رَصَدٗا
“Kupatula Mtumiki (Wake) amene wamuyanja; (iyeyo amamdziwitsa zobisikazo) ndipo ndithu amamuikira alonda kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake (omulonda).”
Tafsyrai arabų kalba:
لِّيَعۡلَمَ أَن قَدۡ أَبۡلَغُواْ رِسَٰلَٰتِ رَبِّهِمۡ وَأَحَاطَ بِمَا لَدَيۡهِمۡ وَأَحۡصَىٰ كُلَّ شَيۡءٍ عَدَدَۢا
“Kuti adziwe ngati afikitsa uthenga wa Mbuye wawo, ndipo wawazungulira (podziwa zonse zili kwa iwo) ndipo wadziwa kuchuluka kwa zinthu zonse zimene zilipo; (palibe chobisika kwa Iye).”
Tafsyrai arabų kalba:
 
Reikšmių vertimas Sūra: Sūra Al-Džinn
Sūrų turinys Puslapio numeris
 
Kilniojo Korano reikšmių vertimas - Čevų k. vertimas - Vertimų turinys

Kilniojo Korano reikšmių vertimas į čevų k., išvertė Khaled Ibrahim Betala. 2020 m. leidimas.

Uždaryti