Check out the new design

വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ വിവർത്തനം - ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബറ്റിയാലാ * - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക


പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: ന്നിസാഅ്   ആയത്ത്:
وَمَا كَانَ لِمُؤۡمِنٍ أَن يَقۡتُلَ مُؤۡمِنًا إِلَّا خَطَـٔٗاۚ وَمَن قَتَلَ مُؤۡمِنًا خَطَـٔٗا فَتَحۡرِيرُ رَقَبَةٖ مُّؤۡمِنَةٖ وَدِيَةٞ مُّسَلَّمَةٌ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦٓ إِلَّآ أَن يَصَّدَّقُواْۚ فَإِن كَانَ مِن قَوۡمٍ عَدُوّٖ لَّكُمۡ وَهُوَ مُؤۡمِنٞ فَتَحۡرِيرُ رَقَبَةٖ مُّؤۡمِنَةٖۖ وَإِن كَانَ مِن قَوۡمِۭ بَيۡنَكُمۡ وَبَيۡنَهُم مِّيثَٰقٞ فَدِيَةٞ مُّسَلَّمَةٌ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِۦ وَتَحۡرِيرُ رَقَبَةٖ مُّؤۡمِنَةٖۖ فَمَن لَّمۡ يَجِدۡ فَصِيَامُ شَهۡرَيۡنِ مُتَتَابِعَيۡنِ تَوۡبَةٗ مِّنَ ٱللَّهِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلِيمًا حَكِيمٗا
Ndipo sikoyenera kwa wokhulupirira kupha wokhulupilila (mnzake mwadala) pokhapokha mwangozi. Ndipo yemwe wapha wokhulupilila mwangozi, apereke ufulu kwa kapolo wa Chisilamu ndi dipo lomwe alipereke kwa ofedwawo pokhapokha akakana okha (amulowa mmalo a womwalilayo), monga m’njira ya sadaka. Ngati wophedwayo ndi mnansi wa adani anu pomwe ali wokhulupilila, perekani ufulu kwa kapolo wa Chisilamu, (palibenso dipo lina). Ngati wophedwayo ndi mmodzi wa anthu omwe pakati panu ndi iwo pali chipangano (chosamenyana nkhondo), ndiye kuti amulowammalo ake apatsidwe dipo; apatsidwenso ufulu kapolo wa Chisilamu. Ndipo ngati sadapeze (zoterozo), asale miyezi iwiri yotsatana. Iyo ndiyo njira yolapira (pa uchimo wotere) yochokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa Ngwanzeru zakuya.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
وَمَن يَقۡتُلۡ مُؤۡمِنٗا مُّتَعَمِّدٗا فَجَزَآؤُهُۥ جَهَنَّمُ خَٰلِدٗا فِيهَا وَغَضِبَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِ وَلَعَنَهُۥ وَأَعَدَّ لَهُۥ عَذَابًا عَظِيمٗا
Ndipo amene angaphe wokhulupilila mwadala, mphoto yake ndi Jahannam; mmenemo adzakhala nthawi yaitali. Ndipo Allah amkwiira ndi kumtembelera ndi kumkonzera chilango chachikulu.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا ضَرَبۡتُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَتَبَيَّنُواْ وَلَا تَقُولُواْ لِمَنۡ أَلۡقَىٰٓ إِلَيۡكُمُ ٱلسَّلَٰمَ لَسۡتَ مُؤۡمِنٗا تَبۡتَغُونَ عَرَضَ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا فَعِندَ ٱللَّهِ مَغَانِمُ كَثِيرَةٞۚ كَذَٰلِكَ كُنتُم مِّن قَبۡلُ فَمَنَّ ٱللَّهُ عَلَيۡكُمۡ فَتَبَيَّنُوٓاْۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٗا
E inu amene mwakhulupirira! Mukayenda pa njira ya Allah, musachite chinthu pokhapokha mutaonetsetsa bwino. Ndipo musanene kwa amene akukulonjerani Salamu (kuti): “Sindiwe wokhulupirira,” (nkumupha). Mukufuna zinthu zamdziko lapansi komatu kwa Allah kuli zopeza zambiri. Umo ndi momwe inunso mudalili kale; koma Allah adakuchitirani chifundo (choncho mudalowa m’Chisilamu. Penyetsetsani bwinobwino). Ndithu Allah Ngodziwa bwinobwino nkhani zonse zimene muchita.
അറബി ഖുർആൻ വിവരണങ്ങൾ:
 
പരിഭാഷ അദ്ധ്യായം: ന്നിസാഅ്
സൂറത്തുകളുടെ സൂചിക പേജ് നമ്പർ
 
വിശുദ്ധ ഖുർആൻ പരിഭാഷ - ചെവ്വ വിവർത്തനം - ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബറ്റിയാലാ - വിവർത്തനങ്ങളുടെ സൂചിക

ഖാലിദ് ഇബ്രാഹിം ബേത്താല അതു വിവർത്തനം ചെയ്തു.

അടക്കുക