Ndipo omwe achite cha uve (chigololo) mwa akazi anu, afunireni mboni zinayi za mwa inu zoikira umboni pa iwo. Ngati ataikira umboni (kuti achitadi cha uvecho), atsekereni m’nyumba kufikira imfa idzawapeze, kapena Allah adzawaikire njira ina (monga kuphedwa).[114]
[114] (Ndime 15-16) Izi ndi ndime zimene zikufotokoza za zilango zolanga nazo awa:-
a) Akazi amene amachitana ukwati akazi okhaokha
b) Amuna amene amachitana ukwati amuna okhaokha
c) Akazi ndi amuna amene akuchitana ukwati pamalo achabe a pathupi. Zinthu zonsezi nzoipa kwabasi.
Ndithudi kulapa kovomerezeka ndi Allah nkwa omwe amachita zoipa mwa umbuli kenako nkulapa mwachangu. Amenewo ndiomwe Allah amawalandira kulapa kwawo. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri Ngwanzeru zakuya.[115]
[115] Ndime iyi ikusonyeza kuti Allah amalandira kulapa kuchokera kwa aliyense amene walapa. Komatu kuti kulapako kuvomerezeke, pafunika zinthu ziwiri:-
a) Akachita uchimo alape mwachangu. Osati azingopitiriza kulakwako mpaka akadzaona kuti ali pafupi kufa ndiye nkuyamba kulapa, zoterezi iyayi.
b) Uchimowo ukhale kuti adauchita chifukwa cha umbuli. Apa zikutanthauza kuti panthawiyo iye adadzazidwa ndi zilakolako za uchimo ndipo zidamchititsa kuti achimwe. Koma osati tchimolo likhale lolichita tsiku ndi tsiku popanda kulabadira chilichonse. Kulapa kwa uchimo wotero Allah sangakulandire. Ndipo mmalo mwake akamulanga ndi chilango chaukali.
Kulapa sikungalandiridwe pa omwe akuchita zoipa mpaka imfa kumfikira m’modzi wa iwo (pamenepo) nkunena: “Ndithudi ine ndikulapa tsopano.” Ngakhalenso pa omwe akufa ali osakhulupirira. Iwo tawakonzera chilango chopweteka.
E inu amene mwakhulupirira! Sikovomerezedwa kwa inu kuwalowa chokolo akazi mowakakamiza. Ndipo musawaletse (kukwatiwa ndi amuna ena) ndi cholinga choti muwalande zina mwa zomwe mudawapatsa, (nkosaloledwa kutero) kupatula ngati atachita choipa choonekera. Ndipo khalani nawo mwa ubwino. Ngati mutawada (musalekane nawo), mwina mungade chinthu chomwe Allah waika zabwino zambiri mkati mwake.[116]
[116] Nthawi ya umbuli, chikhalidwe cha Arabu chidali chonchi:- Tate wa munthu akamwalira ana ake amamlowera chokolo akazi ake omwe sadabereke anawo. Mwana aliyense amalowa chokolo mwa mkazi watate wake yemwe sadali mayi wake wom’bala.
a) Akafuna kumkwatira adali kumtenga.
b) Ndipo akafuna kumkwatitsa kwa mwamuna wina, amamlamula ndalama mwamunayo iye natenga ndalamazo.
c) Kapena amangomuvutitsavutitsa kuti akafuna adziombole yekha pomlipira ndalama mwanayo.
d) Kapena amangommanga kuti asakwatiwenso mpaka imfa yake. Choncho apa Allah akuletsa machitidwe oipawa.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
തിരയൽ ഫലങ്ങൾ:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".