Check out the new design

पवित्र कुरअानको अर्थको अनुवाद - चेवा अनुवाद : खालिद इब्राहीम बेतियाला । * - अनुवादहरूको सूची


अर्थको अनुवाद सूरः: अन्फाल   श्लोक:
ذَٰلِكَ بِأَنَّ ٱللَّهَ لَمۡ يَكُ مُغَيِّرٗا نِّعۡمَةً أَنۡعَمَهَا عَلَىٰ قَوۡمٍ حَتَّىٰ يُغَيِّرُواْ مَا بِأَنفُسِهِمۡ وَأَنَّ ٱللَّهَ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Izo, (posawadzera miliri yotere) nchifukwa chakuti Allah sasintha chisomo (Chake) chimene wachipereka kwa anthu mpaka anthuwo asinthe okha zomwe zili m’mitima mwawo, (posiya kuthokoza Allah nayamba kuyenda m’njira zolakwira Allah). Ndithu Allah Ngwakumva Ngodziwa chilichonse.
अरबी व्याख्याहरू:
كَدَأۡبِ ءَالِ فِرۡعَوۡنَ وَٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡۚ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِ رَبِّهِمۡ فَأَهۡلَكۡنَٰهُم بِذُنُوبِهِمۡ وَأَغۡرَقۡنَآ ءَالَ فِرۡعَوۡنَۚ وَكُلّٞ كَانُواْ ظَٰلِمِينَ
(Khalidwe lawo lili) ngati khalidwe la anthu a Farawo ndi omwe adalipo patsogolo pawo. Adatsutsa zizindikiro za Mbuye wawo. Choncho, tidawaononga chifukwa cha machimo awo, ndipo tidawamiza anthu a Farawo. Ndipo onse adali ochita zoipa.
अरबी व्याख्याहरू:
إِنَّ شَرَّ ٱلدَّوَآبِّ عِندَ ٱللَّهِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ فَهُمۡ لَا يُؤۡمِنُونَ
Ndithu nyama zoipitsitsa kwa Allah ndi amene sakhulupirira. (amamkana Allah ngakhale choonadi akuchidziwa bwinobwino), choncho iwo sakhulupirira
अरबी व्याख्याहरू:
ٱلَّذِينَ عَٰهَدتَّ مِنۡهُمۡ ثُمَّ يَنقُضُونَ عَهۡدَهُمۡ فِي كُلِّ مَرَّةٖ وَهُمۡ لَا يَتَّقُونَ
Omwe unapangana nawo chipangano kenako naaswa chipangano chawo panthawi iliyonse (imene mwapangana), ndiponso iwo saopa Allah.
अरबी व्याख्याहरू:
فَإِمَّا تَثۡقَفَنَّهُمۡ فِي ٱلۡحَرۡبِ فَشَرِّدۡ بِهِم مَّنۡ خَلۡفَهُمۡ لَعَلَّهُمۡ يَذَّكَّرُونَ
Choncho, ngati uwapeza ku nkhondo, (menyana nawo), uwabalalitse (kuti likhale phunziro kwa) amene ali pambuyo pawo kuti iwo azindikire.
अरबी व्याख्याहरू:
وَإِمَّا تَخَافَنَّ مِن قَوۡمٍ خِيَانَةٗ فَٱنۢبِذۡ إِلَيۡهِمۡ عَلَىٰ سَوَآءٍۚ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يُحِبُّ ٱلۡخَآئِنِينَ
Ngati uopa kusakhulupirika kwa anthu (omwe unapangana nawo chipangano), atayire (chipangano chawocho), mwachilungamo; ndithu Allah sakonda (anthu) osakhulupirika.
अरबी व्याख्याहरू:
وَلَا يَحۡسَبَنَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ سَبَقُوٓاْۚ إِنَّهُمۡ لَا يُعۡجِزُونَ
Ndipo (anthu) amene sadakhulupirire asaganize kuti ampitilira (Allah kotero kuti sachita kanthu ndi iwo), iwo sangamulepheretse Allah (chimene akufuna kuchita pa iwo).
अरबी व्याख्याहरू:
وَأَعِدُّواْ لَهُم مَّا ٱسۡتَطَعۡتُم مِّن قُوَّةٖ وَمِن رِّبَاطِ ٱلۡخَيۡلِ تُرۡهِبُونَ بِهِۦ عَدُوَّ ٱللَّهِ وَعَدُوَّكُمۡ وَءَاخَرِينَ مِن دُونِهِمۡ لَا تَعۡلَمُونَهُمُ ٱللَّهُ يَعۡلَمُهُمۡۚ وَمَا تُنفِقُواْ مِن شَيۡءٖ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ يُوَفَّ إِلَيۡكُمۡ وَأَنتُمۡ لَا تُظۡلَمُونَ
Ndipo akonzekereni mmene mungathere ndi mphamvu zanu (zonse zomenyera nkhondo), ndiponso poikiratu mahatchi odikira nkhondo kuti muwaopseze nazo adani a Allah ndi adani anu (amene mukuwadziwa) ndiponso (ndi) ena omwe (inu) simukuwadziwa. Koma Allah akuwadziwa. Ndipo chilichonse mungapereke pa njira ya Allah chidzalipidwa kwa inu modzadza ndipo simuzaponderezedwa.
अरबी व्याख्याहरू:
۞ وَإِن جَنَحُواْ لِلسَّلۡمِ فَٱجۡنَحۡ لَهَا وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱللَّهِۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndipo ngati (awo adani) apendekera kumbali yokhalirana mwa mtendere, nawenso pendekera (ku mbaliyo) ukatero yadzamira kwa Allah. Ndithudi Iye Ngwakumva, Ngodziwa.
अरबी व्याख्याहरू:
 
अर्थको अनुवाद सूरः: अन्फाल
अध्यायहरूको (सूरःहरूको) सूची رقم الصفحة
 
पवित्र कुरअानको अर्थको अनुवाद - चेवा अनुवाद : खालिद इब्राहीम बेतियाला । - अनुवादहरूको सूची

यसलाई खालिद इब्राहिम पेटाला ले अनुवाद गरे।

बन्द गर्नुस्