Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (28) Surah: Soerat al-Kahf (De spelonk)
وَٱصۡبِرۡ نَفۡسَكَ مَعَ ٱلَّذِينَ يَدۡعُونَ رَبَّهُم بِٱلۡغَدَوٰةِ وَٱلۡعَشِيِّ يُرِيدُونَ وَجۡهَهُۥۖ وَلَا تَعۡدُ عَيۡنَاكَ عَنۡهُمۡ تُرِيدُ زِينَةَ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۖ وَلَا تُطِعۡ مَنۡ أَغۡفَلۡنَا قَلۡبَهُۥ عَن ذِكۡرِنَا وَٱتَّبَعَ هَوَىٰهُ وَكَانَ أَمۡرُهُۥ فُرُطٗا
Ndipo dzikakamize kukhala pamodzi ndi amene akupempha Mbuye wawo m’mawa ndi madzulo uku akufunafuna nkhope Yake (chiyanjo Chake), ndipo maso ako asachoke pa iwo ndi (kuyang’ana ena) ncholinga chofuna zokongoletsa za moyo wa dziko lapansi; ndipo usamumvere amene mtima wake tauiwalitsa kutikumbukira ndikumangotsatira zilakolako zake, ndipo zinthu zake nkukhala zotaika (zosalongosoka).[259]
[259] Ndime iyi idavumbulutsidwa pamene Uyaina Bun Huswaini ndi mnzake adadza kwa Mtumiki ndi kumpeza atakhala pamodzi ndi omtsatira (Maswahaba) osauka monga: Ammaru, Suhaibu ndi Bilali ndi ena onga iwo. Iwo adati kwa Mtumiki (s.a.w): “Ukadawapirikitsa anthu wambawa, ndiye kuti tikadakhala nawe nkumamvera zimene ukulalikira. Koma ife tikunyansidwa ndi ulaliki wako poona kuti nthawi zonse ukukhala ndi anthu onyozeka amene simabwana.” Choncho Qur’an idatsika kumuuza Mtumiki (s.a.w) kuti: “Usawathamangitse anthu omwe akupempha Allah m’mawa ndi madzulo ngakhale kuti ndionyozeka.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (28) Surah: Soerat al-Kahf (De spelonk)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit