Check out the new design

د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه سورت: یونس   آیت:
وَلَوۡ أَنَّ لِكُلِّ نَفۡسٖ ظَلَمَتۡ مَا فِي ٱلۡأَرۡضِ لَٱفۡتَدَتۡ بِهِۦۗ وَأَسَرُّواْ ٱلنَّدَامَةَ لَمَّا رَأَوُاْ ٱلۡعَذَابَۖ وَقُضِيَ بَيۡنَهُم بِٱلۡقِسۡطِ وَهُمۡ لَا يُظۡلَمُونَ
Ndipo kukadakhala kuti munthu aliyense amene adachita zoipa, nkukhala nazo zonse zam’dziko akadapereka zonse kuti adziombole nazo (pamene adzaona kuopsa kwa chilango cha tsikulo). Ndipo akadzachiona chilango, adzayesetsa kubisa madandaulo (awo; koma adzaonekera poyera). Ndipo kudzaweruzidwa mwachilungamo pakati pawo, ndipo iwo sadzaponderezedwa.
عربي تفسیرونه:
أَلَآ إِنَّ لِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِۗ أَلَآ إِنَّ وَعۡدَ ٱللَّهِ حَقّٞ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Tamverani! Ndithu zonse za kumwamba ndi pansi nza Allah. Tamverani! Ndithu lonjezo la Allah ndi loona, koma ambiri a iwo sadziwa.
عربي تفسیرونه:
هُوَ يُحۡيِۦ وَيُمِيتُ وَإِلَيۡهِ تُرۡجَعُونَ
Iye (Allah ndi amene) amapereka moyo ndi imfa. Ndipo kwa Iye (nonsenu) mudzabwezedwa.
عربي تفسیرونه:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ قَدۡ جَآءَتۡكُم مَّوۡعِظَةٞ مِّن رَّبِّكُمۡ وَشِفَآءٞ لِّمَا فِي ٱلصُّدُورِ وَهُدٗى وَرَحۡمَةٞ لِّلۡمُؤۡمِنِينَ
E inu anthu! Ndithu ulaliki wakudzerani kuchokera kwa Mbuye wanu ndi machiritso a matenda omwe ali m’mitima mwanu, ndiponso nchiongoko ndi chifundo kwa okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
قُلۡ بِفَضۡلِ ٱللَّهِ وَبِرَحۡمَتِهِۦ فَبِذَٰلِكَ فَلۡيَفۡرَحُواْ هُوَ خَيۡرٞ مِّمَّا يَجۡمَعُونَ
Nena: “Chifukwa cha ubwino wa Allah ndi chifundo Chake (mwapeza zimenezi), choncho asangalalire zimenezi.” Izi ndizabwino kwambiri kuposa zimene akusonkhanitsa (m’zinthu za dziko lapansi).
عربي تفسیرونه:
قُلۡ أَرَءَيۡتُم مَّآ أَنزَلَ ٱللَّهُ لَكُم مِّن رِّزۡقٖ فَجَعَلۡتُم مِّنۡهُ حَرَامٗا وَحَلَٰلٗا قُلۡ ءَآللَّهُ أَذِنَ لَكُمۡۖ أَمۡ عَلَى ٱللَّهِ تَفۡتَرُونَ
Nena: “Kodi mukuona bwanji, rizq lomwe Allah wakutsitsirani? Kenako inu lina mwa ilo mwalichita kukhala loletsedwa (la haramu), ndipo lina mwa ilo kukhala lololedwa (la halali).” Nena: “Kodi Allah adakulolezani (kuchita zimenezo), kapena mukumpekera Allah bodza?”
عربي تفسیرونه:
وَمَا ظَنُّ ٱلَّذِينَ يَفۡتَرُونَ عَلَى ٱللَّهِ ٱلۡكَذِبَ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۗ إِنَّ ٱللَّهَ لَذُو فَضۡلٍ عَلَى ٱلنَّاسِ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ لَا يَشۡكُرُونَ
Kodi ali ndi ganizo lotani amene akumpekera Allah bodza pa za tsiku la Qiyâma? Ndithu Allah Ndi mwini ubwino wochuluka kwa anthu. Koma ambiri a iwo sathokoza.
عربي تفسیرونه:
وَمَا تَكُونُ فِي شَأۡنٖ وَمَا تَتۡلُواْ مِنۡهُ مِن قُرۡءَانٖ وَلَا تَعۡمَلُونَ مِنۡ عَمَلٍ إِلَّا كُنَّا عَلَيۡكُمۡ شُهُودًا إِذۡ تُفِيضُونَ فِيهِۚ وَمَا يَعۡزُبُ عَن رَّبِّكَ مِن مِّثۡقَالِ ذَرَّةٖ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا فِي ٱلسَّمَآءِ وَلَآ أَصۡغَرَ مِن ذَٰلِكَ وَلَآ أَكۡبَرَ إِلَّا فِي كِتَٰبٖ مُّبِينٍ
Ndipo siutanganidwa ndi ntchito iliyonse, ndiponso simuwerenga m’menemo (chinthu chilichonse) cha m’Qur’an ndipo simuchita ntchito ina iliyonse (inu anthu) koma Ife timakhala mboni pa inu pamene mukutanganidwa nayo. Ndipo sichibisika kwa Mbuye wako chinthu chilichonse ngakhale cholemera ngati nyelere, m’nthaka ngakhale kumwamba. Ndipo ngakhale chocheperapo zedi kuposa pamenepo kapena chokulirapo koma chili m’kuku (la Allah) lofotokoza chilichonse.
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه سورت: یونس
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا - د ژباړو فهرست (لړلیک)

خالد إبراهيم بيتالا ژباړلی دی.

بندول