Check out the new design

د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه سورت: یوسف   آیت:
قَالَ مَعَاذَ ٱللَّهِ أَن نَّأۡخُذَ إِلَّا مَن وَجَدۡنَا مَتَٰعَنَا عِندَهُۥٓ إِنَّآ إِذٗا لَّظَٰلِمُونَ
(Yûsuf) adati: “Ha! tikudzitchinjiriza mwa Allah, sitingagwire wina koma yemwe chuma chathu tachipeza ndi iye, kuopa kuti tingakhale ochita zoipa.”
عربي تفسیرونه:
فَلَمَّا ٱسۡتَيۡـَٔسُواْ مِنۡهُ خَلَصُواْ نَجِيّٗاۖ قَالَ كَبِيرُهُمۡ أَلَمۡ تَعۡلَمُوٓاْ أَنَّ أَبَاكُمۡ قَدۡ أَخَذَ عَلَيۡكُم مَّوۡثِقٗا مِّنَ ٱللَّهِ وَمِن قَبۡلُ مَا فَرَّطتُمۡ فِي يُوسُفَۖ فَلَنۡ أَبۡرَحَ ٱلۡأَرۡضَ حَتَّىٰ يَأۡذَنَ لِيٓ أَبِيٓ أَوۡ يَحۡكُمَ ٱللَّهُ لِيۖ وَهُوَ خَيۡرُ ٱلۡحَٰكِمِينَ
Choncho, pamene adataya mtima za iye, adapita pambali kukanong’onezana. Wamkulu wawo adati: “Kodi simudziwa kuti bambo wanu adatenga lonjezo kuchokera kwa inu m’dzina la Allah (kuti mudzam’bweza iyeyo?) ndiponso kale mudalakwa (pa mapangano anu) pa za Yûsuf. Choncho sindichoka dziko lino kufikira atandilola bambo (kutero) kapena Allah andilamule (zondichotsa kuno pomasulidwa m’bale wangayu); Iye Ngwabwino polamula kuposa olamula.”
عربي تفسیرونه:
ٱرۡجِعُوٓاْ إِلَىٰٓ أَبِيكُمۡ فَقُولُواْ يَٰٓأَبَانَآ إِنَّ ٱبۡنَكَ سَرَقَ وَمَا شَهِدۡنَآ إِلَّا بِمَا عَلِمۡنَا وَمَا كُنَّا لِلۡغَيۡبِ حَٰفِظِينَ
“Bwererani kwa bambo wanu ndipo mukawauze (kuti): “E bambo wathu! Ndithu mwana wanu waba. Ndipo ife sitidaikire umboni (wakuti wakuba achitidwe ukapolo) koma pa zomwe tidazidziwa (kuti mwa ife mulibe wakuba), ndipo sitidali kudziwa zamseri.”
عربي تفسیرونه:
وَسۡـَٔلِ ٱلۡقَرۡيَةَ ٱلَّتِي كُنَّا فِيهَا وَٱلۡعِيرَ ٱلَّتِيٓ أَقۡبَلۡنَا فِيهَاۖ وَإِنَّا لَصَٰدِقُونَ
“Ndipo afunseni anthu a m’mudzi momwe tidalimo ndi a pa ulendo omwe tadza nawo, ndipo ndithudi ife tikunena zoona.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ بَلۡ سَوَّلَتۡ لَكُمۡ أَنفُسُكُمۡ أَمۡرٗاۖ فَصَبۡرٞ جَمِيلٌۖ عَسَى ٱللَّهُ أَن يَأۡتِيَنِي بِهِمۡ جَمِيعًاۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡعَلِيمُ ٱلۡحَكِيمُ
(Ya’qub) adati: “Koma mitima yanu yakukometserani chinthu. (Kwanga ndi) kupirira kwabwino kokha basi. Mwina Allah adzandibweretsera onse pamodzi. Ndithudi, Iye Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.”
عربي تفسیرونه:
وَتَوَلَّىٰ عَنۡهُمۡ وَقَالَ يَٰٓأَسَفَىٰ عَلَىٰ يُوسُفَ وَٱبۡيَضَّتۡ عَيۡنَاهُ مِنَ ٱلۡحُزۡنِ فَهُوَ كَظِيمٞ
Ndipo adawachokera ndikunena (kuti): “Ha! kudandaula kwanga za Yûsuf!” Ndipo maso ake adayera chifukwa cha kudandaula ndipo iye adadzazidwa ndi chisoni.
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ تَٱللَّهِ تَفۡتَؤُاْ تَذۡكُرُ يُوسُفَ حَتَّىٰ تَكُونَ حَرَضًا أَوۡ تَكُونَ مِنَ ٱلۡهَٰلِكِينَ
(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Simusiya kumkumbukira Yûsuf (ndikulira) mpaka mufika podwala, kapena mukhala mwa owonongeka (ndi imfa).”
عربي تفسیرونه:
قَالَ إِنَّمَآ أَشۡكُواْ بَثِّي وَحُزۡنِيٓ إِلَى ٱللَّهِ وَأَعۡلَمُ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
(Iye) adati: “Ndithu ine ndikusuma dandaulo langa ndi kukhumata kwanga kwa Allah, ndipo ndikudziwa kupyolera mwa Allah zomwe simukudziwa.”
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه سورت: یوسف
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - خالد ابراهیم بتیالا - د ژباړو فهرست (لړلیک)

خالد إبراهيم بيتالا ژباړلی دی.

بندول